Add parallel Print Page Options

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

90 Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo
    pa mibado yonse.
Mapiri asanabadwe,
    musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,
    kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

Inu mumabwezera anthu ku fumbi,
    mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”
Pakuti zaka 1,000 pamaso panu
    zili ngati tsiku limene lapita
    kapena ngati kamphindi ka usiku.
Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,
    iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,
ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,
    pofika madzulo wauma ndi kufota.

Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;
    ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.
Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,
    machimo athu obisika poonekera pamaso panu.
Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;
    timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.
10 Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,
    kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;
komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,
    zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11 Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?
    Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.
12 Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,
    kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13 Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?
    Achitireni chifundo atumiki anu.
14 Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,
    kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.
15 Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,
    kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.
16 Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,
    kukongola kwanu kwa ana awo.

17 Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;
    tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;
    inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

BOOK IV

Psalms 90–106

Psalm 90

A prayer of Moses the man of God.

Lord, you have been our dwelling place(A)
    throughout all generations.
Before the mountains were born(B)
    or you brought forth the whole world,
    from everlasting to everlasting(C) you are God.(D)

You turn people back to dust,
    saying, “Return to dust, you mortals.”(E)
A thousand years in your sight
    are like a day that has just gone by,
    or like a watch in the night.(F)
Yet you sweep people away(G) in the sleep of death—
    they are like the new grass of the morning:
In the morning it springs up new,
    but by evening it is dry and withered.(H)

We are consumed by your anger
    and terrified by your indignation.
You have set our iniquities before you,
    our secret sins(I) in the light of your presence.(J)
All our days pass away under your wrath;
    we finish our years with a moan.(K)
10 Our days may come to seventy years,(L)
    or eighty,(M) if our strength endures;
yet the best of them are but trouble and sorrow,(N)
    for they quickly pass, and we fly away.(O)
11 If only we knew the power of your anger!
    Your wrath(P) is as great as the fear that is your due.(Q)
12 Teach us to number our days,(R)
    that we may gain a heart of wisdom.(S)

13 Relent, Lord! How long(T) will it be?
    Have compassion on your servants.(U)
14 Satisfy(V) us in the morning with your unfailing love,(W)
    that we may sing for joy(X) and be glad all our days.(Y)
15 Make us glad for as many days as you have afflicted us,
    for as many years as we have seen trouble.
16 May your deeds be shown to your servants,
    your splendor to their children.(Z)

17 May the favor[a] of the Lord our God rest on us;
    establish the work of our hands for us—
    yes, establish the work of our hands.(AA)

Footnotes

  1. Psalm 90:17 Or beauty