Add parallel Print Page Options

Magaleta Anayi

Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona magaleta anayi akutuluka pakati pa mapiri awiri, mapiri amkuwa. Galeta loyamba limakokedwa ndi akavalo ofiira, lachiwiri ndi akavalo akuda, lachitatu ndi akavalo oyera, ndipo lachinayi ndi akavalo otuwa a mawanga ofiirira, onsewa anali akavalo amphamvu kwambiri. Ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane uja kuti, “Kodi mbuye wanga chimenechi nʼchiyani?”

Mngeloyo anandiyankha kuti, “Imeneyi ndi mizimu inayi yakumwamba, imene ikuchokera pamaso pa Ambuye wa dziko lonse. Galeta la akavalo akuda likupita ku dziko la kumpoto, galeta la akavalo oyera likutsatira, ndipo galeta la akavalo amawanga ofiirira likupita ku dziko la kummwera.”

Pamene akavalo amphamvuwa ankapita, anali ndi changu chofuna kuyendera dziko lapansi. Ndipo iye anati, “Pitani, kayendereni dziko lapansi!”

Pamenepo anandiyitana, “Taona, akavalo amene apita ku dziko la kumpoto apumulitsa Mzimu wanga kumeneko.”

Chipewa Chaufumu cha Yoswa

Yehova anayankhula nane kuti, 10 “Landira mphatso kuchokera kwa anthu amene abwera ku ukapolo, Helidai, Tobiya ndi Yedaya, amene achokera ku Babuloni. Tsiku lomwelo pita ku nyumba ya Yosiya mwana wa Zefaniya. 11 Tenga siliva ndi golide upange chipewa chaufumu, ndipo uchiyike pamutu pa mkulu wa ansembe, Yoswa mwana wa Yehozadaki. 12 Muwuze kuti zimene akunena Yehova Wamphamvuzonse ndi izi: ‘Taonani, munthu wotchedwa Nthambi ndi ameneyu, ndipo adzaphuka pomwe alipo ndi kumanga Nyumba ya Yehova. 13 Ndiye amene adzamange Nyumba ya Yehova, adzalandira ulemerero waufumu ndipo adzalamulira pa mpando wake waufumu. Adzakhalanso wansembe pa mpando wake waufumu. Ndipo padzakhala mtendere.’ 14 Chipewa cha ufumucho adzachipereka kwa Helemu, Tobiya, Yedaya, ndi kwa Heni mwana wa Zefaniya, kuti chikhale chikumbutso mʼNyumba ya Yehova. 15 Anthu okhala kutali adzabwera kudzathandiza kumanga Nyumba ya Yehova, ndipo iwe udzadziwa kuti Yehova Wamphamvuzonse wandituma kwa iwe. Zimenezi zidzachitika ngati mudzamvera mwachangu Yehova Mulungu wanu.”

Four Chariots

I looked up again, and there before me were four chariots(A) coming out from between two mountains—mountains of bronze. The first chariot had red horses, the second black,(B) the third white,(C) and the fourth dappled—all of them powerful. I asked the angel who was speaking to me, “What are these, my lord?”

The angel answered me, “These are the four spirits[a](D) of heaven, going out from standing in the presence of the Lord of the whole world.(E) The one with the black horses is going toward the north country, the one with the white horses toward the west,[b] and the one with the dappled horses toward the south.”

When the powerful horses went out, they were straining to go throughout the earth.(F) And he said, “Go throughout the earth!” So they went throughout the earth.

Then he called to me, “Look, those going toward the north country have given my Spirit[c] rest(G) in the land of the north.”(H)

A Crown for Joshua

The word of the Lord came to me: 10 “Take silver and gold from the exiles Heldai, Tobijah and Jedaiah, who have arrived from Babylon.(I) Go the same day to the house of Josiah son of Zephaniah. 11 Take the silver and gold and make a crown,(J) and set it on the head of the high priest, Joshua(K) son of Jozadak.[d](L) 12 Tell him this is what the Lord Almighty says: ‘Here is the man whose name is the Branch,(M) and he will branch out from his place and build the temple of the Lord.(N) 13 It is he who will build the temple of the Lord, and he will be clothed with majesty and will sit and rule on his throne. And he[e] will be a priest(O) on his throne. And there will be harmony between the two.’ 14 The crown will be given to Heldai,[f] Tobijah, Jedaiah and Hen[g] son of Zephaniah as a memorial(P) in the temple of the Lord. 15 Those who are far away will come and help to build the temple of the Lord,(Q) and you will know that the Lord Almighty has sent me to you.(R) This will happen if you diligently obey(S) the Lord your God.”

Footnotes

  1. Zechariah 6:5 Or winds
  2. Zechariah 6:6 Or horses after them
  3. Zechariah 6:8 Or spirit
  4. Zechariah 6:11 Hebrew Jehozadak, a variant of Jozadak
  5. Zechariah 6:13 Or there
  6. Zechariah 6:14 Syriac; Hebrew Helem
  7. Zechariah 6:14 Or and the gracious one, the