Add parallel Print Page Options

Chikalata Chowuluka

Ndinayangʼananso ndipo taonani ndinaona chikalata chimene chimawuluka.

Mngelo uja anandifunsa kuti, “Kodi ukuona chiyani?”

Ndinayankha kuti, “Ndikuona chikalata chikuwuluka, mulitali mwake mamita asanu ndi anayi ndipo mulifupi mwake mamita anayi ndi theka.”

Ndipo mngeloyo anandiwuza kuti, “Awa ndi matemberero amene akupita pa dziko lonse lapansi; potsata zimene zalembedwa mʼkati mwa chikalatamo, aliyense wakuba adzachotsedwa, ndipo potsata zomwe zalembedwa kunja kwake, aliyense wolumbira zabodza adzachotsedwanso. Yehova Wamphamvuzonse akunena kuti, ‘Temberero limeneli ndidzalitumiza, ndipo lidzalowa mʼnyumba ya munthu wakuba ndi munthu wolumbira zabodza mʼdzina langa. Lidzakhala mʼnyumbamo mpaka kuyiwonongeratu, matabwa ake ndi miyala yake yomwe.’ ”

Mkazi mu Dengu

Kenaka mngelo amene amayankhula nane uja anabwera patsogolo panga ndipo anandiwuza kuti, “Kweza maso ako tsopano kuti uwone kuti ndi chiyani chikubwerachi.”

Ndinafunsa kuti, “Kodi chimenechi nʼchiyani?”

Mngeloyo anayankha kuti, “Limeneli ndi dengu loyezera.” Ndipo anawonjezera kunena kuti, “Umenewu ndi uchimo wa anthu mʼdziko lonse.”

Pamenepo chovundikira chake chamtovu chinatukulidwa, ndipo mʼdengumo munali mutakhala mkazi. Mngeloyo anati, “Chimenechi ndi choyipa,” ndipo anamukankhira mkaziyo mʼdengu muja, nabwezera chovundikira chamtovu chija pamwamba pake.

Kenaka ndinayangʼananso, ndipo ndinaona akazi awiri akuwuluka kubwera kumene kunali ine; akuwuluzika ndi mphepo. Iwo anali ndi mapiko ngati a kakowa, ndipo ananyamula dengu lija, kupita nalo pakati pa mlengalenga ndi dziko lapansi.

10 Ine ndinafunsa mngelo amene amayankhula nane kuti, “Dengulo akupita nalo kuti?”

11 Iye anayankha kuti, “Ku dziko la Babuloni kuti akalimangire nyumba. Nyumbayo ikadzatha, adzayikamo dengulo.”

The Flying Scroll

I looked again, and there before me was a flying scroll.(A)

He asked me, “What do you see?”(B)

I answered, “I see a flying scroll, twenty cubits long and ten cubits wide.[a]

And he said to me, “This is the curse(C) that is going out over the whole land; for according to what it says on one side, every thief(D) will be banished, and according to what it says on the other, everyone who swears falsely(E) will be banished. The Lord Almighty declares, ‘I will send it out, and it will enter the house of the thief and the house of anyone who swears falsely(F) by my name. It will remain in that house and destroy it completely, both its timbers and its stones.(G)’”

The Woman in a Basket

Then the angel who was speaking to me came forward and said to me, “Look up and see what is appearing.”

I asked, “What is it?”

He replied, “It is a basket.(H)” And he added, “This is the iniquity[b] of the people throughout the land.”

Then the cover of lead was raised, and there in the basket sat a woman! He said, “This is wickedness,” and he pushed her back into the basket and pushed its lead cover down on it.(I)

Then I looked up—and there before me were two women, with the wind in their wings! They had wings like those of a stork,(J) and they lifted up the basket between heaven and earth.

10 “Where are they taking the basket?” I asked the angel who was speaking to me.

11 He replied, “To the country of Babylonia[c](K) to build a house(L) for it. When the house is ready, the basket will be set there in its place.”(M)

Footnotes

  1. Zechariah 5:2 That is, about 30 feet long and 15 feet wide or about 9 meters long and 4.5 meters wide
  2. Zechariah 5:6 Or appearance
  3. Zechariah 5:11 Hebrew Shinar