Add parallel Print Page Options

Zovala Zoyera za Mkulu wa Ansembe

Pamenepo anandionetsa Yoswa, mkulu wa ansembe, atayima pamaso pa mngelo wa Yehova, ndipo Satana anayima ku dzanja lake lamanja kuti atsutsane naye. Yehova anawuza Satana kuti, “Yehova akukudzudzula iwe Satana! Yehova amene wasankha Yerusalemu akukudzudzula! Kodi munthu uyu sali ngati chikuni choyaka chofumula pa moto?”

Tsono Yoswa anali atavala zovala zalitsiro pa nthawi imene anayima pamaso pa mngelo. Mngelo uja anawuza anzake amene anali naye kuti, “Muvuleni zovala zake zalitsirizo.”

Kenaka anawuza Yoswa kuti, “Taona, ndachotsa tchimo lako, ndipo ndikuveka zovala zokongola.”

Ndipo ine ndinati, “Muvekeni nduwira yopatulika pamutu pake.” Choncho anamuveka nduwira yopatulika pamutu pake, namuvekanso zovala zatsopano. Nthawiyi nʼkuti mngelo wa Yehova atayima pambali.

Mngelo wa Yehova analimbikitsa Yoswa kuti, “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Ngati uyenda mʼnjira zanga ndi kusunga malamulo anga, pamenepo udzalamulira nyumba yanga ndi kuyangʼanira mabwalo anga, ndipo ndidzakulolani kuti mudzakhale pamodzi ndi amene ali panowa.

“ ‘Mvera tsono, iwe Yoswa mkulu wa ansembe, pamodzi ndi anzako amene wakhala nawowa, amene ndi chizindikiro cha zinthu zimene zikubwera: Ine ndidzabweretsa mtumiki wanga, wotchedwa Nthambi. Taona, mwala wokongola umene ndayika patsogolo pa Yoswa! Pa mwala umenewu pali maso asanu ndi awiri, ndipo Ine ndidzalembapo mawu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse, ‘ndipo ndidzachotsa tchimo la dziko lino tsiku limodzi.

10 “ ‘Tsiku limenelo aliyense adzayitana mnzake kuti akhale pansi pa mtengo wamphesa ndi wa mkuyu,’ akutero Yehova Wamphamvuzonse.”

Clean Garments for the High Priest

Then he showed me Joshua(A) the high priest standing before the angel of the Lord, and Satan[a](B) standing at his right side to accuse him. The Lord said to Satan, “The Lord rebuke you,(C) Satan! The Lord, who has chosen(D) Jerusalem, rebuke you! Is not this man a burning stick(E) snatched from the fire?”(F)

Now Joshua was dressed in filthy clothes as he stood before the angel. The angel said to those who were standing before him, “Take off his filthy clothes.”

Then he said to Joshua, “See, I have taken away your sin,(G) and I will put fine garments(H) on you.”

Then I said, “Put a clean turban(I) on his head.” So they put a clean turban on his head and clothed him, while the angel of the Lord stood by.

The angel of the Lord gave this charge to Joshua: “This is what the Lord Almighty says: ‘If you will walk in obedience to me and keep my requirements,(J) then you will govern my house(K) and have charge(L) of my courts, and I will give you a place among these standing here.(M)

“‘Listen, High Priest(N) Joshua, you and your associates seated before you, who are men symbolic(O) of things to come: I am going to bring my servant, the Branch.(P) See, the stone I have set in front of Joshua!(Q) There are seven eyes[b](R) on that one stone,(S) and I will engrave an inscription on it,’ says the Lord Almighty, ‘and I will remove the sin(T) of this land in a single day.

10 “‘In that day each of you will invite your neighbor to sit(U) under your vine and fig tree,(V)’ declares the Lord Almighty.”

Footnotes

  1. Zechariah 3:1 Hebrew satan means adversary.
  2. Zechariah 3:9 Or facets