Add parallel Print Page Options

Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
    inu mtundu wochititsa manyazi,
isanafike nthawi yachiweruzo,
    nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
    tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
    inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
    mwina mudzatetezedwa
    pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.

Za Afilisti

Gaza adzasiyidwa
    ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
    ndipo Ekroni adzazulidwa.
Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
    inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
    iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
    ndipo palibe amene adzatsale.”

Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
    lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
    adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
    mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
    adzabwezeretsa mtendere wawo.

Za Mowabu ndi Amoni

“Ndamva kunyoza kwa Mowabu
    ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
    ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
Choncho, pali Ine Wamoyo,”
    akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
    Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
    dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
    opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”

10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
    chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
    pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
    uliwonse ku dziko la kwawo.

Za Kusi

12 “Inunso anthu a ku Kusi,
    mudzaphedwa ndi lupanga.”

Za Asiriya

13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
    ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
    ndi owuma ngati chipululu.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
    pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
    adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
    mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
    nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala
    umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
    “Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
    kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
    ndi kupukusa mitu yawo.

Judah and Jerusalem Judged Along With the Nations

Judah Summoned to Repent

Gather together,(A) gather yourselves together,
    you shameful(B) nation,
before the decree takes effect
    and that day passes like windblown chaff,(C)
before the Lord’s fierce anger(D)
    comes upon you,
before the day of the Lord’s wrath(E)
    comes upon you.
Seek(F) the Lord, all you humble of the land,
    you who do what he commands.
Seek righteousness,(G) seek humility;(H)
    perhaps you will be sheltered(I)
    on the day of the Lord’s anger.

Philistia

Gaza(J) will be abandoned
    and Ashkelon(K) left in ruins.
At midday Ashdod will be emptied
    and Ekron uprooted.
Woe to you who live by the sea,
    you Kerethite(L) people;
the word of the Lord is against you,(M)
    Canaan, land of the Philistines.
He says, “I will destroy you,
    and none will be left.”(N)
The land by the sea will become pastures
    having wells for shepherds
    and pens for flocks.(O)
That land will belong
    to the remnant(P) of the people of Judah;
    there they will find pasture.
In the evening they will lie down
    in the houses of Ashkelon.
The Lord their God will care for them;
    he will restore their fortunes.[a](Q)

Moab and Ammon

“I have heard the insults(R) of Moab(S)
    and the taunts of the Ammonites,(T)
who insulted(U) my people
    and made threats against their land.(V)
Therefore, as surely as I live,”
    declares the Lord Almighty,
    the God of Israel,
“surely Moab(W) will become like Sodom,(X)
    the Ammonites(Y) like Gomorrah—
a place of weeds and salt pits,
    a wasteland forever.
The remnant of my people will plunder(Z) them;
    the survivors(AA) of my nation will inherit their land.(AB)

10 This is what they will get in return for their pride,(AC)
    for insulting(AD) and mocking
    the people of the Lord Almighty.(AE)
11 The Lord will be awesome(AF) to them
    when he destroys all the gods(AG) of the earth.(AH)
Distant nations will bow down to him,(AI)
    all of them in their own lands.

Cush

12 “You Cushites,[b](AJ) too,
    will be slain by my sword.(AK)

Assyria

13 He will stretch out his hand against the north
    and destroy Assyria,(AL)
leaving Nineveh(AM) utterly desolate
    and dry as the desert.(AN)
14 Flocks and herds(AO) will lie down there,
    creatures of every kind.
The desert owl(AP) and the screech owl(AQ)
    will roost on her columns.
Their hooting will echo through the windows,
    rubble will fill the doorways,
    the beams of cedar will be exposed.
15 This is the city of revelry(AR)
    that lived in safety.(AS)
She said to herself,
    “I am the one! And there is none besides me.”(AT)
What a ruin she has become,
    a lair for wild beasts!(AU)
All who pass by her scoff(AV)
    and shake their fists.(AW)

Footnotes

  1. Zephaniah 2:7 Or will bring back their captives
  2. Zephaniah 2:12 That is, people from the upper Nile region