Add parallel Print Page Options

Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse
    pa dziko lapansi,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;
    ndidzawononga mbalame zamlengalenga
    ndi nsomba za mʼnyanja.
Ndidzawononga anthu oyipa,
    ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”
            akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda
    ndi onse okhala mu Yerusalemu.
Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,
    mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:
amene amagwada pa madenga a nyumba zawo
    kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,
amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,
    komanso mʼdzina la Moleki,
amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,
    osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.
Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,
    chifukwa tsiku la Yehova layandikira.
Yehova wakonzekera kupereka nsembe;
    wapatula iwo amene wawayitana.
Pa tsiku la nsembe ya Yehova
    ndidzalanga akalonga
    ndi ana aamuna a mfumu
ndi onse amene amavala
    zovala zachilendo.
Pa tsiku limenelo ndidzalanga
    onse amene safuna kuponda pa chiwundo,
amene amadzaza nyumba ya ambuye awo
    ndi chiwawa ndi chinyengo.

10 “Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,
    “Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,
    kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,
    ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.
11 Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;
    a malonda anu onse adzapululidwa,
    ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.
12 Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale
    ndi kulanga onse amene sakulabadira,
    amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,
amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,
    chabwino kaya choyipa.’
13 Chuma chawo chidzafunkhidwa,
    nyumba zawo zidzagwetsedwa.
Adzamanga nyumba,
    koma osakhalamo;
adzadzala minda ya mpesa
    koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14 Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,
    layandikira ndipo lifika msanga.
Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,
    ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.
15 Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,
    tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,
tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,
    tsiku la mdima ndi lachisoni,
    tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.
16 Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,
    tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa
    ndi nsanja za pa ngodya.
17 Ndidzabweretsa msautso pa anthu
    ndipo adzayenda ngati anthu osaona,
    chifukwa achimwira Yehova,
magazi awo adzamwazika ngati fumbi
    ndi mnofu wawo ngati ndowe.
18 Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo
    sadzatha kuwapulumutsa
    pa tsiku la ukali wa Yehova.
Dziko lonse lapansi lidzanyeka
    mʼmoto wa nsanje yake
chifukwa adzakantha modzidzimutsa
    onse okhala pa dziko lapansi.

The word of the Lord that came to Zephaniah son of Cushi, the son of Gedaliah, the son of Amariah, the son of Hezekiah, during the reign of Josiah(A) son of Amon(B) king of Judah:

Judgment on the Whole Earth in the Day of the Lord

“I will sweep away everything
    from the face of the earth,”(C)
declares the Lord.
“I will sweep away both man and beast;(D)
    I will sweep away the birds in the sky(E)
    and the fish in the sea—
    and the idols that cause the wicked to stumble.”[a]

“When I destroy all mankind
    on the face of the earth,”(F)
declares the Lord,(G)
“I will stretch out my hand(H) against Judah
    and against all who live in Jerusalem.
I will destroy every remnant of Baal worship in this place,(I)
    the very names of the idolatrous priests(J)
those who bow down on the roofs
    to worship the starry host,(K)
those who bow down and swear by the Lord
    and who also swear by Molek,[b](L)
those who turn back from following(M) the Lord
    and neither seek(N) the Lord nor inquire(O) of him.”

Be silent(P) before the Sovereign Lord,
    for the day of the Lord(Q) is near.
The Lord has prepared a sacrifice;(R)
    he has consecrated those he has invited.

“On the day of the Lord’s sacrifice
    I will punish(S) the officials
    and the king’s sons(T)
and all those clad
    in foreign clothes.
On that day I will punish
    all who avoid stepping on the threshold,[c](U)
who fill the temple of their gods
    with violence and deceit.(V)

10 “On that day,(W)
    declares the Lord,
“a cry will go up from the Fish Gate,(X)
    wailing(Y) from the New Quarter,
    and a loud crash from the hills.
11 Wail,(Z) you who live in the market district[d];
    all your merchants will be wiped out,
    all who trade with[e] silver will be destroyed.(AA)
12 At that time I will search Jerusalem with lamps
    and punish those who are complacent,(AB)
    who are like wine left on its dregs,(AC)
who think, ‘The Lord will do nothing,(AD)
    either good or bad.’(AE)
13 Their wealth will be plundered,(AF)
    their houses demolished.
Though they build houses,
    they will not live in them;
though they plant vineyards,
    they will not drink the wine.”(AG)

14 The great day of the Lord(AH) is near(AI)
    near and coming quickly.
The cry on the day of the Lord is bitter;
    the Mighty Warrior shouts his battle cry.
15 That day will be a day of wrath—
    a day of distress and anguish,
        a day of trouble and ruin,
    a day of darkness(AJ) and gloom,
        a day of clouds and blackness(AK)
16     a day of trumpet and battle cry(AL)
against the fortified cities
    and against the corner towers.(AM)

17 “I will bring such distress(AN) on all people
    that they will grope about like those who are blind,(AO)
    because they have sinned against the Lord.
Their blood will be poured out(AP) like dust
    and their entrails like dung.(AQ)
18 Neither their silver nor their gold
    will be able to save them
    on the day of the Lord’s wrath.”(AR)

In the fire of his jealousy(AS)
    the whole earth will be consumed,(AT)
for he will make a sudden end
    of all who live on the earth.(AU)

Footnotes

  1. Zephaniah 1:3 The meaning of the Hebrew for this line is uncertain.
  2. Zephaniah 1:5 Hebrew Malkam
  3. Zephaniah 1:9 See 1 Samuel 5:5.
  4. Zephaniah 1:11 Or the Mortar
  5. Zephaniah 1:11 Or in