Add parallel Print Page Options

Kuweruzidwa kwa Mitundu ya Anthu

“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo,
    nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse
    ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati.
Kumeneko ndidzawaweruza
    chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli,
pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu
    ndikugawa dziko langa.
Anagawana anthu anga pochita maere
    ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere;
anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo
    kuti iwo amwe.

“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu. Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano. Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.

“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu. Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.

Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina:
    Konzekerani nkhondo!
Dzutsani ankhondo amphamvu!
    Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Sulani makasu anu kuti akhale malupanga
    ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo.
Munthu wofowoka anene kuti,
    “Ndine wamphamvu!”
11 Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse,
    ndipo musonkhane kumeneko.

Tumizani ankhondo anu Yehova!

12 “Mitundu ya anthu idzuke;
    ipite ku Chigwa cha Yehosafati,
pakuti kumeneko Ine ndidzakhala
    ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Tengani chikwakwa chodulira tirigu,
    pakuti mbewu zakhwima.
Bwerani dzapondeni mphesa,
    pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza
    ndipo mitsuko ikusefukira;
kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”

14 Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu,
    mʼchigwa cha chiweruzo!
Pakuti tsiku la Yehova layandikira
    mʼchigwa cha chiweruzo.
15 Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa,
    ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni
    ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu;
    dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka.
Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake,
    linga la anthu a ku Israeli.

Madalitso a Anthu a Mulungu

17 “Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu,
    ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika.
Yerusalemu adzakhala wopatulika;
    alendo sadzamuthiranso nkhondo.

18 “Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano,
    ndipo zitunda zidzayenderera mkaka;
    mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi.
Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova
    ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Koma Igupto adzasanduka bwinja,
    Edomu adzasanduka chipululu,
chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda
    mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya
    ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke
    ndidzakhululuka.”

Yehova amakhala mu Ziyoni!

The Nations Judged

[a]“In those days and at that time,
    when I restore the fortunes(A) of Judah(B) and Jerusalem,
I will gather(C) all nations
    and bring them down to the Valley of Jehoshaphat.[b](D)
There I will put them on trial(E)
    for what they did to my inheritance, my people Israel,
because they scattered(F) my people among the nations
    and divided up my land.
They cast lots(G) for my people
    and traded boys for prostitutes;
    they sold girls for wine(H) to drink.

“Now what have you against me, Tyre and Sidon(I) and all you regions of Philistia?(J) Are you repaying me for something I have done? If you are paying me back, I will swiftly and speedily return on your own heads what you have done.(K) For you took my silver and my gold and carried off my finest treasures to your temples.[c](L) You sold the people of Judah and Jerusalem to the Greeks,(M) that you might send them far from their homeland.

“See, I am going to rouse them out of the places to which you sold them,(N) and I will return(O) on your own heads what you have done. I will sell your sons(P) and daughters to the people of Judah,(Q) and they will sell them to the Sabeans,(R) a nation far away.” The Lord has spoken.(S)

Proclaim this among the nations:
    Prepare for war!(T)
Rouse the warriors!(U)
    Let all the fighting men draw near and attack.
10 Beat your plowshares into swords
    and your pruning hooks(V) into spears.(W)
Let the weakling(X) say,
    “I am strong!”(Y)
11 Come quickly, all you nations from every side,
    and assemble(Z) there.

Bring down your warriors,(AA) Lord!

12 “Let the nations be roused;
    let them advance into the Valley of Jehoshaphat,(AB)
for there I will sit
    to judge(AC) all the nations on every side.
13 Swing the sickle,(AD)
    for the harvest(AE) is ripe.
Come, trample the grapes,(AF)
    for the winepress(AG) is full
    and the vats overflow—
so great is their wickedness!”

14 Multitudes,(AH) multitudes
    in the valley(AI) of decision!
For the day of the Lord(AJ) is near
    in the valley of decision.(AK)
15 The sun and moon will be darkened,
    and the stars no longer shine.(AL)
16 The Lord will roar(AM) from Zion
    and thunder from Jerusalem;(AN)
    the earth and the heavens will tremble.(AO)
But the Lord will be a refuge(AP) for his people,
    a stronghold(AQ) for the people of Israel.

Blessings for God’s People

17 “Then you will know(AR) that I, the Lord your God,(AS)
    dwell in Zion,(AT) my holy hill.(AU)
Jerusalem will be holy;(AV)
    never again will foreigners invade her.(AW)

18 “In that day the mountains will drip new wine,(AX)
    and the hills will flow with milk;(AY)
    all the ravines of Judah will run with water.(AZ)
A fountain will flow out of the Lord’s house(BA)
    and will water the valley of acacias.[d](BB)
19 But Egypt(BC) will be desolate,
    Edom(BD) a desert waste,
because of violence(BE) done to the people of Judah,
    in whose land they shed innocent blood.
20 Judah will be inhabited forever(BF)
    and Jerusalem through all generations.
21 Shall I leave their innocent blood unavenged?(BG)
    No, I will not.(BH)

The Lord dwells in Zion!(BI)

Footnotes

  1. Joel 3:1 In Hebrew texts 3:1-21 is numbered 4:1-21.
  2. Joel 3:2 Jehoshaphat means the Lord judges; also in verse 12.
  3. Joel 3:5 Or palaces
  4. Joel 3:18 Or Valley of Shittim