Add parallel Print Page Options

Yehova anayankhula ndi Yoweli mwana wa Petueli.

Kubwera kwa Dzombe

Inu akuluakulu, imvani izi;
    mvetserani, nonse amene mumakhala mʼdziko.
Kodi zinthu zokhala ngati izi zinayamba zaonekapo mʼnthawi yanu,
    kapena mʼnthawi ya makolo anu?
Muwafotokozere ana anu,
    ndipo ana anuwo afotokozere ana awo,
    ndipo ana awo adzafotokozere mʼbado winawo.
Chimene dzombe losamera mapiko lasiya
    dzombe lowuluka ladya;
chimene dzombe lowuluka lasiya
    dzombe lalingʼono ladya;
chimene dzombe lalingʼono lasiya
    chilimamine wadya.

Dzukani, inu zidakwa ndipo mulire!
    Lirani mofuwula, inu nonse amene mumamwa vinyo;
lirani mofuwula chifukwa cha vinyo watsopano,
    pakuti wachotsedwa pakamwa panu.
Mtundu wa anthu wathira nkhondo dziko langa,
    wamphamvu ndi wosawerengeka;
uli ndi mano a mkango,
    zibwano za mkango waukazi.
Wawononga mphesa zanga
    ndipo wathyola mitengo yanga ya mkuyu.
Wakungunula makungwa ake
    ndi kuwataya,
    kusiya nthambi zake zili mbee.

Lirani ngati namwali wovala chiguduli,
    chifukwa cha mwamuna wa utsikana wake.
Chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa
    sizikuperekedwa ku nyumba ya Yehova.
Ansembe akulira,
    amene amatumikira pamaso pa Yehova.
10 Minda yaguga,
    nthaka yauma;
tirigu wawonongeka,
    vinyo watsopano watha,
    mitengo ya mafuta yauma.
11 Khalani ndi nkhawa, inu alimi,
    lirani mofuwula inu alimi a mphesa;
imvani chisoni chifukwa cha tirigu ndi barele,
    pakuti zokolola za mʼmunda zawonongeka.
12 Mpesa wauma
    ndipo mtengo wamkuyu wafota;
makangadza, kanjedza ndi mitengo ya apulosi,
    mitengo yonse ya mʼmunda yauma.
Ndithudi chimwemwe cha anthu
    chatheratu.

Mulungu Ayitana Anthu kuti Atembenuke

13 Inu ansembe, valani ziguduli ndipo lirani;
    lirani mofuwula, inu amene mumatumikira pa guwa lansembe.
Bwerani, fundani ziguduli usiku wonse,
    inu amene mumatumikira pamaso pa Mulungu wanga;
pakuti chopereka cha chakudya ndi cha chakumwa
    sizikupezekanso mʼnyumba ya Mulungu wanu.
14 Lengezani tsiku lopatulika losala zakudya,
    itanani msonkhano wopatulika.
Sonkhanitsani akuluakulu
    ndi anthu onse okhala mʼdziko
ku nyumba ya Yehova Mulungu wanu
    ndipo alirire Yehova.

15 Kalanga ine tsikulo!
    Pakuti tsiku la Yehova layandikira;
    lidzabwera ngati chiwonongeko chochokera kwa Wamphamvuzonse.

16 Kodi chakudya chathu sichachotsedwa
    ife tikuona?
Kodi mʼnyumba ya Mulungu wathu
    simulibe chimwemwe ndi chisangalalo?
17 Mbewu zikunyala
    poti pansi ndi powuma.
Nyumba zosungiramo zinthu zawonongeka;
    nkhokwe zapasuka
    popeza tirigu wauma.
18 Taonani mmene zikulirira ziweto;
    ngʼombe zikungoyenda uku ndi uku
chifukwa zilibe msipu;
    ngakhalenso nkhosa zikusauka.

19 Kwa Inu Yehova ndilirira,
    pakuti moto wapsereza msipu wakuthengo,
    malawi amoto apsereza mitengo yonse ya mʼtchire.
20 Ngakhale nyama zakuthengo zikulirira Inu;
    timitsinje tonse taphwa
    ndipo moto wapsereza msipu wa kuthengo.

The word of the Lord that came(A) to Joel(B) son of Pethuel.

An Invasion of Locusts

Hear this,(C) you elders;(D)
    listen, all who live in the land.(E)
Has anything like this ever happened in your days
    or in the days of your ancestors?(F)
Tell it to your children,(G)
    and let your children tell it to their children,
    and their children to the next generation.(H)
What the locust(I) swarm has left
    the great locusts have eaten;
what the great locusts have left
    the young locusts have eaten;
what the young locusts have left(J)
    other locusts[a] have eaten.(K)

Wake up, you drunkards, and weep!
    Wail, all you drinkers of wine;(L)
wail because of the new wine,
    for it has been snatched(M) from your lips.
A nation has invaded my land,
    a mighty army without number;(N)
it has the teeth(O) of a lion,
    the fangs of a lioness.
It has laid waste(P) my vines
    and ruined my fig trees.(Q)
It has stripped off their bark
    and thrown it away,
    leaving their branches white.

Mourn like a virgin in sackcloth(R)
    grieving for the betrothed of her youth.
Grain offerings and drink offerings(S)
    are cut off from the house of the Lord.
The priests are in mourning,(T)
    those who minister before the Lord.
10 The fields are ruined,
    the ground is dried up;(U)
the grain is destroyed,
    the new wine(V) is dried up,
    the olive oil fails.(W)

11 Despair, you farmers,(X)
    wail, you vine growers;
grieve for the wheat and the barley,(Y)
    because the harvest of the field is destroyed.(Z)
12 The vine is dried up
    and the fig tree is withered;(AA)
the pomegranate,(AB) the palm and the apple[b] tree—
    all the trees of the field—are dried up.(AC)
Surely the people’s joy
    is withered away.

A Call to Lamentation

13 Put on sackcloth,(AD) you priests, and mourn;
    wail, you who minister(AE) before the altar.
Come, spend the night in sackcloth,
    you who minister before my God;
for the grain offerings and drink offerings(AF)
    are withheld from the house of your God.
14 Declare a holy fast;(AG)
    call a sacred assembly.
Summon the elders
    and all who live in the land(AH)
to the house of the Lord your God,
    and cry out(AI) to the Lord.(AJ)

15 Alas for that(AK) day!
    For the day of the Lord(AL) is near;
    it will come like destruction from the Almighty.[c](AM)

16 Has not the food been cut off(AN)
    before our very eyes—
joy and gladness(AO)
    from the house of our God?(AP)
17 The seeds are shriveled
    beneath the clods.[d](AQ)
The storehouses are in ruins,
    the granaries have been broken down,
    for the grain has dried up.
18 How the cattle moan!
    The herds mill about
because they have no pasture;(AR)
    even the flocks of sheep are suffering.(AS)

19 To you, Lord, I call,(AT)
    for fire(AU) has devoured the pastures(AV) in the wilderness
    and flames have burned up all the trees of the field.
20 Even the wild animals pant for you;(AW)
    the streams of water have dried up(AX)
    and fire has devoured the pastures(AY) in the wilderness.

Footnotes

  1. Joel 1:4 The precise meaning of the four Hebrew words used here for locusts is uncertain.
  2. Joel 1:12 Or possibly apricot
  3. Joel 1:15 Hebrew Shaddai
  4. Joel 1:17 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.