Add parallel Print Page Options

Kugawa kwa Dziko la Kumadzulo kwa Yorodani

14 Umu ndi mmene Aisraeli analandirira cholowa chawo mʼdziko la Kanaani. Eliezara wansembe, Yoswa mwana wa Nuni pamodzi ndi akuluakulu a mafuko a Israeli ndiwo anagawa dzikolo kugawira Aisraeli. Madera anagawidwa mwa maere kwa mafuko asanu ndi anayi ndi theka, monga momwe Yehova analamulira kudzera mwa Mose. Mose anapereka kwa mafuko awiri ndi theka dziko la kummawa kwa Yorodani, koma fuko la Levi lokha silinagawiridwe malo. Tsono fuko la Yosefe analigawa pawiri, Manase ndi Efereimu. Mose sanawagawire malo mabanja a fuko la Levi, koma iwo anangolandira mizinda imene ankakhalamo pamodzi ndi malo amene ankawetako nkhosa ndi ngʼombe zawo. Choncho Aisraeli anagawana dzikolo, monga momwe Yehova analamulira Mose.

Apereka Hebroni kwa Kalebe

Tsono anthu a fuko la Yuda anabwera kwa Yoswa ku Giligala, ndipo Kalebe mwana wa Yefune Mkeni anati kwa iye, “Inu mukudziwa zimene Yehova ananena kwa Mose munthu wa Mulungu za inu ndi ine ku Kadesi Barinea. Nthawi imene Mose mtumiki wa Yehova anandituma kuchokera ku Kadesi Barinea kudzayendera dzikoli ndinali ndi zaka makumi anayi. Ndipo nditabwerako ndinamuwuza zoona zokhazokha monga momwe ndinaonera. Koma abale anga amene ndinapita nawo anachititsa anthu mantha. Komabe ine ndinamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wonse. Kotero tsiku limenelo Mose anandilonjeza kuti, ‘Dziko limene unayendamo lidzakhala lako ndiponso la ana ako kwamuyaya chifukwa unamvera Yehova Mulungu wanga ndi mtima wako wonse.’

10 “Tsono papita zaka 45 chiyankhulire Yehova zimenezi kwa Mose. Nthawi imeneyo nʼkuti Aisraeli akuyendayenda mʼchipululu. Yehova wandisunga ndipo tsopano ndili ndi zaka 85. 11 Komabe ndikanali ndi mphamvu lero, monga ndinalili tsiku lija Mose anandituma. Ndili ndi mphamvu moti ndikhoza kupita ku nkhondo kapena kuchita kanthu kena kalikonse. 12 Tsopano ndipatseni dziko la ku mapiri limene Yehova anandilonjeza tsiku lija. Inu munamva nthawi ija kuti Aanaki anali kumeneko ndipo kuti mizinda yawo inali ikuluikulu ndi yotetezedwa. Komabe Yehova atakhala nane ndidzawathamangitsa monga Iye ananenera.”

13 Ndipo Yoswa anadalitsa Kalebe mwana wa Yefune ndi kumupatsa Hebroni kukhala dziko lake. 14 Choncho dera la Hebroni lakhala lili la Kalebe mwana wa Yefune Mkeni mpaka lero chifukwa anamvera Yehova Mulungu wa Israeli ndi mtima wonse. 15 (Hebroni ankatchedwa Kiriati Ariba chifukwa cha Ariba amene anali munthu wamphamvu kwambiri pakati pa Aanaki).

Ndipo kenaka mʼdziko monse munakhala mtendere.

Division of the Land West of the Jordan

14 Now these are the areas the Israelites received as an inheritance(A) in the land of Canaan, which Eleazar(B) the priest, Joshua son of Nun and the heads of the tribal clans of Israel(C) allotted(D) to them.(E) Their inheritances were assigned by lot(F) to the nine and a half tribes,(G) as the Lord had commanded through Moses. Moses had granted the two and a half tribes their inheritance east of the Jordan(H) but had not granted the Levites an inheritance among the rest,(I) for Joseph’s descendants had become two tribes—Manasseh and Ephraim.(J) The Levites received no share of the land but only towns to live in, with pasturelands for their flocks and herds.(K) So the Israelites divided the land, just as the Lord had commanded Moses.(L)

Allotment for Caleb

Now the people of Judah approached Joshua at Gilgal,(M) and Caleb son of Jephunneh(N) the Kenizzite said to him, “You know what the Lord said to Moses the man of God(O) at Kadesh Barnea(P) about you and me.(Q) I was forty years old when Moses the servant of the Lord sent me from Kadesh Barnea(R) to explore the land.(S) And I brought him back a report according to my convictions,(T) but my fellow Israelites who went up with me made the hearts of the people melt in fear.(U) I, however, followed the Lord my God wholeheartedly.(V) So on that day Moses swore to me, ‘The land on which your feet have walked will be your inheritance(W) and that of your children(X) forever, because you have followed the Lord my God wholeheartedly.’[a]

10 “Now then, just as the Lord promised,(Y) he has kept me alive for forty-five years since the time he said this to Moses, while Israel moved(Z) about in the wilderness. So here I am today, eighty-five years old!(AA) 11 I am still as strong(AB) today as the day Moses sent me out; I’m just as vigorous(AC) to go out to battle now as I was then. 12 Now give me this hill country that the Lord promised me that day.(AD) You yourself heard then that the Anakites(AE) were there and their cities were large and fortified,(AF) but, the Lord helping me, I will drive them out just as he said.”

13 Then Joshua blessed(AG) Caleb son of Jephunneh(AH) and gave him Hebron(AI) as his inheritance.(AJ) 14 So Hebron has belonged to Caleb son of Jephunneh the Kenizzite ever since, because he followed the Lord, the God of Israel, wholeheartedly.(AK) 15 (Hebron used to be called Kiriath Arba(AL) after Arba,(AM) who was the greatest man among the Anakites.)

Then the land had rest(AN) from war.

Footnotes

  1. Joshua 14:9 Deut. 1:36