Yona 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Pemphero la Yona
2 Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. 2 Iye anati:
“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,
ndipo Iye anandiyankha.
Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,
ndipo Inu munamva kulira kwanga.
3 Munandiponya mʼnyanja yozama,
mʼkati mwenimweni mwa nyanja,
ndipo madzi oyenda anandizungulira;
mafunde anu onse ndi mkokomo wake
zinandimiza.
4 Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa
pamaso panu;
komabe ndidzayangʼananso
ku Nyumba yanu yopatulika.’
5 Madzi wondimiza anandichititsa mantha,
nyanja yozama inandizungulira;
udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
6 Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;
mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.
Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,
Inu Yehova Mulungu wanga.
7 “Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,
ine ndinakumbukira Inu Yehova,
ndipo pemphero langa linafika kwa inu,
ku Nyumba yanu yopatulika.
8 “Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe
amataya chisomo chawo.
9 Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe
ndikuyimba nyimbo yamayamiko.
Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.
Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”
10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.
Jonah 2
New International Version
2 1 [a]From inside the fish Jonah prayed to the Lord his God. 2 He said:
“In my distress I called(A) to the Lord,(B)
and he answered me.
From deep in the realm of the dead(C) I called for help,
and you listened to my cry.
3 You hurled me into the depths,(D)
into the very heart of the seas,
and the currents swirled about me;
all your waves(E) and breakers
swept over me.(F)
4 I said, ‘I have been banished
from your sight;(G)
yet I will look again
toward your holy temple.’(H)
5 The engulfing waters threatened me,[b]
the deep surrounded me;
seaweed was wrapped around my head.(I)
6 To the roots of the mountains(J) I sank down;
the earth beneath barred me in forever.
But you, Lord my God,
brought my life up from the pit.(K)
7 “When my life was ebbing away,
I remembered(L) you, Lord,
and my prayer(M) rose to you,
to your holy temple.(N)
8 “Those who cling to worthless idols(O)
turn away from God’s love for them.
9 But I, with shouts of grateful praise,(P)
will sacrifice(Q) to you.
What I have vowed(R) I will make good.
I will say, ‘Salvation(S) comes from the Lord.’”
10 And the Lord commanded the fish, and it vomited Jonah onto dry land.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.