Add parallel Print Page Options

Pemphero la Yona

Yona ali mʼmimba mwa chinsomba chija anapemphera kwa Yehova Mulungu wake. Iye anati:

“Pamene ndinali mʼmavuto anga ndinayitana Yehova,
    ndipo Iye anandiyankha.
Ndili ku dziko la anthu akufa ndinapempha thandizo,
    ndipo Inu munamva kulira kwanga.
Munandiponya mʼnyanja yozama,
    mʼkati mwenimweni mwa nyanja,
    ndipo madzi oyenda anandizungulira;
mafunde anu onse ndi mkokomo wake
    zinandimiza.
Ndinati, ‘Ine ndachotsedwa
    pamaso panu;
komabe ndidzayangʼananso
    ku Nyumba yanu yopatulika.’
Madzi wondimiza anandichititsa mantha,
    nyanja yozama inandizungulira;
    udzu wa mʼmadzi zinakuta mutu wanga.
Ndinatsikira kunsi ndithu, mʼtsinde mwa mapiri;
    mipiringidzo ya dziko inanditsekereza kosatha.
Koma Inu munatulutsa moyo wanga mʼmandamo,
    Inu Yehova Mulungu wanga.

“Pamene moyo wanga umachoka mwa ine,
    ine ndinakumbukira Inu Yehova,
ndipo pemphero langa linafika kwa inu,
    ku Nyumba yanu yopatulika.

“Iwo amene amagwiritsitsa mafano achabechabe
    amataya chisomo chawo.
Koma ine ndidzapereka kwa Inu nsembe
    ndikuyimba nyimbo yamayamiko.
Chimene ndinalonjeza ndidzachikwaniritsa.
    Chipulumutso chimachokera kwa Yehova.”

10 Ndipo Yehova analamula chinsomba chija, ndipo chinakamusanza Yonayo mʼmbali mwa nyanja.

[a]From inside the fish Jonah prayed to the Lord his God. He said:

“In my distress I called(A) to the Lord,(B)
    and he answered me.
From deep in the realm of the dead(C) I called for help,
    and you listened to my cry.
You hurled me into the depths,(D)
    into the very heart of the seas,
    and the currents swirled about me;
all your waves(E) and breakers
    swept over me.(F)
I said, ‘I have been banished
    from your sight;(G)
yet I will look again
    toward your holy temple.’(H)
The engulfing waters threatened me,[b]
    the deep surrounded me;
    seaweed was wrapped around my head.(I)
To the roots of the mountains(J) I sank down;
    the earth beneath barred me in forever.
But you, Lord my God,
    brought my life up from the pit.(K)

“When my life was ebbing away,
    I remembered(L) you, Lord,
and my prayer(M) rose to you,
    to your holy temple.(N)

“Those who cling to worthless idols(O)
    turn away from God’s love for them.
But I, with shouts of grateful praise,(P)
    will sacrifice(Q) to you.
What I have vowed(R) I will make good.
    I will say, ‘Salvation(S) comes from the Lord.’”

10 And the Lord commanded the fish, and it vomited Jonah onto dry land.

Footnotes

  1. Jonah 2:1 In Hebrew texts 2:1 is numbered 1:17, and 2:1-10 is numbered 2:2-11.
  2. Jonah 2:5 Or waters were at my throat