Add parallel Print Page Options

Yesu Apita Kuphwando Lamisasa

Zitatha izi Yesu anayendayenda mu Galileya, ndi cholinga chakuti asafike ku Yudeya chifukwa Ayuda kumeneko amadikira kuti amuphe. Koma phwando la Ayuda lamisasa litayandikira, abale a Yesu anati kwa Iye, “Inu muyenera kuchoka kuno ndi kupita ku Yudeya, kuti ophunzira anu akaone zodabwitsa zomwe mumachita. Palibe wina aliyense amene amafuna kukhala wodziwika amachita zinthu mseri. Popeza Inu mukuchita zinthu izi, mudzionetsere nokha ku dziko la pansi.” Pakuti ngakhale abale ake omwe sanamukhulupirire.

Choncho Yesu anawawuza iwo kuti, “Nthawi yanga yoyenera sinafike; kwa inu nthawi ina iliyonse ndi yoyenera. Dziko lapansi silingakudeni inu, koma limandida Ine chifukwa Ine ndimachitira umboni kuti zomwe limachita ndi zoyipa. Inu pitani kuphwando. Ine sindipita tsopano kuphwando ili chifukwa kwa Ine nthawi yoyenera sinafike.” Atanena izi, Iye anakhalabe mu Galileya.

10 Komabe, abale ake atanyamuka kupita kuphwando, Iye anapitanso, osati moonekera, koma mseri. 11 Tsopano kuphwandoko Ayuda anakamufunafuna ndi kumafunsana kuti, “Kodi munthu ameneyu ali kuti?”

12 Pakuti pa chigulu cha anthu panali kunongʼona ponseponse za Iye. Ena ankanena kuti, “Iye ndi munthu wabwino.”

Ena ankayankha kuti, “Ayi, Iye amanamiza anthu.” 13 Koma panalibe amene ankanena kalikonse poyera za Iye chifukwa choopa Ayuda.

Yesu Aphunzitsa pa Phwando

14 Phwando lili pakatikati, Yesu anapita ku bwalo la Nyumba ya Mulungu ndi kuyamba kuphunzitsa. 15 Ayuda anadabwa ndipo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu nzeru izi anazitenga kuti popanda kuphunzira?”

16 Yesu anayankha kuti, “Chiphunzitso changa si cha Ine ndekha. Chimachokera kwa Iye amene anandituma. 17 Ngati munthu asankha kuchita chifuniro cha Mulungu, adzazindikira ngati chiphunzitso changa nʼchochokera kwa Mulungu kapena ngati ndi mwa Ine ndekha. 18 Iye amene amayankhula za Iye mwini amatero kuti adzipezere ulemu, koma amene amagwira ntchito kuti amene anamutuma alandire ulemu, ameneyo ndiye munthu woona; mu mtima mwake mulibe chinyengo chilichonse. 19 Kodi Mose sanakupatseni lamulo? Komatu palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene akusunga lamulo. Nʼchifukwa chiyani mukufuna kundipha Ine?”

20 Gulu la anthu linayankha kuti, “Iwe ndiye wagwidwa ndi ziwanda. Ndani akufuna kukupha?”

21 Yesu anawawuza kuti, “Ine ndinachita chodabwitsa chimodzi ndipo inu mwadabwa. 22 Koma, chifukwa chakuti Mose anakulamulani kuti muzichita mdulidwe (ngakhale kuti sunachokere kwa Mose, koma kwa makolo anu), inuyo mumachita mdulidwe mwana tsiku la Sabata. 23 Tsopano ngati mwana angachite mdulidwe pa Sabata kuti lamulo la Mose lisaswedwe, nʼchifukwa chiyani mukundipsera mtima chifukwa chochiritsa munthu pa Sabata? 24 Musamaweruze potengera maonekedwe chabe, koma weruzani molungama.”

Kodi Yesu ndi Khristu?

25 Pa nthawi imeneyi anthu ena a ku Yerusalemu anayamba kufunsana kuti, “Kodi uyu si munthu uja akufuna kumuphayu? 26 Uyu ali apa, kuyankhula poyera, ndipo iwo sakunena kanthu kwa Iye. Kodi olamulira atsimikizadi kuti Iye ndi Khristu? 27 Koma ife tikudziwa kumene achokera munthuyu; pamene Khristu adzabwere, palibe amene adzadziwa kumene akuchokera.”

28 Kenaka Yesu, akuphunzitsabe mʼbwalo la Nyumba ya Mulungu anafuwula kuti, “Zoona, mukundidziwa Ine, ndipo mukudziwa kumene ndikuchokera. Ine sindili pano mwa Ine ndekha, koma Iye amene anandituma Ine ndi woona. Inu simukumudziwa, 29 koma Ine ndikumudziwa chifukwa ndichokera kwa Iyeyo ndipo ndiye amene anandituma Ine.”

30 Chifukwa cha izi iwo anayesa kumugwira Iye, koma palibe aliyense amene anayika dzanja lake pa Iye, chifukwa nthawi yake inali isanafike. 31 Komabe, ambiri a mʼchigulucho anamukhulupirira Iye. Iwo anati, “Kodi pamene Khristu abwera, adzachita zizindikiro zodabwitsa zambiri kuposa munthu uyu?”

32 Afarisi anamva chigulucho chikunongʼona zinthu zotere za Iye. Kenaka akulu a ansembe ndi Afarisi anatumiza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu kuti akamumange Iye.

33 Yesu anati, “Ine ndili ndi inu kwa kanthawi kochepa chabe, ndipo kenaka ndizipita kwa Iye amene anandituma Ine. 34 Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza; ndipo kumene Ine ndili inu simungathe kubwera.”

35 Ayuda anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi munthu uyu akuganizira zoti apite kuti kumene ife sitingathe kumupeza Iye? Kodi Iye adzapita kumene anthu amakhala mobalalikana pakati pa Agriki, ndi kuphunzitsa Agriki? 36 Kodi Iye amatanthauza chiyani pamene anati, ‘Inu mudzandifunafuna koma simudzandipeza,’ ndi ‘Kumene Ine ndili, inu simungathe kubwera?’ ”

Mitsinje ya Madzi Opatsa Moyo

37 Pa tsiku lomaliza ndi lalikulu kwambiri laphwando, Yesu anayimirira nafuwula nati, “Ngati munthu ali ndi ludzu, abwere kwa Ine kuti adzamwe. 38 Malemba kuti ‘Aliyense amene akhulupirira Ine, mitsinje yamadzi amoyo idzatuluka kuchokera mʼkati mwake.’ ” 39 Ponena izi Iye amatanthauza Mzimu Woyera, amene adzalandire amene amakhulupirira Iye. Pa nthawiyi nʼkuti Mzimu Woyera asanaperekedwe, pakuti Yesu anali asanalemekezedwe.

40 Pakumva mawu ake, ena a anthuwo anati, “Zoonadi munthu uyu ndi mneneri.”

41 Ena anati, “Iye ndiye Khristu.”

Komanso ena anafunsa kuti, “Kodi Khristu angachokere bwanji ku Galileya? 42 Kodi Malemba samanena kuti Khristu adzachokera mʼbanja la Davide, ndi ku Betelehemu mu mzinda umene Davide anakhalamo?” 43 Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu. 44 Ena anafuna kumugwira Iye, koma palibe amene anayika dzanja pa Iye.

Kusakhulupirira kwa Atsogoleri a Ayuda

45 Pomaliza asilikali a mʼNyumba ya Mulungu anabwerera kwa akulu a ansembe ndi Afarisi amene anawafunsa iwo kuti, “Kodi ndi chifukwa chiyani simunamugwire Iye?”

46 Asilikali aja anati, “Palibe wina amene anayankhula ngati Munthu ameneyo nʼkale lonse.”

47 Afarisi anawadzudzula nati, “Kodi mukutanthauza kuti Iye anakunamizani inunso?” 48 “Kodi alipo ena a olamulira kapena a Afarisi, anamukhulupirira Iye? 49 Ayi! Koma gulu limene silidziwa malamulo ndi lotembereredwa.”

50 Nekodimo, amene anapita kwa Yesu poyamba paja ndipo anali mmodzi wa iwo, anafunsa kuti, 51 “Kodi lamulo lathu limatsutsa munthu popanda kumva mbali yake kuti tipeze chimene wachita?”

52 Iwo anayankha kuti, “Kodi ndiwenso wochokera ku Galileya? Tayangʼananso, ndipo udzapeza kuti mneneri sachokera ku Galileya.”

[Mipukutu yoyambirira ndi maumboni akale mulibe 7:53 mpaka 8:11]

Za Mkazi Wachigololo

53 Kenaka onse anachoka, napita kwawo.

Jesus Goes to the Festival of Tabernacles

After this, Jesus went around in Galilee. He did not want[a] to go about in Judea because the Jewish leaders(A) there were looking for a way to kill him.(B) But when the Jewish Festival of Tabernacles(C) was near, Jesus’ brothers(D) said to him, “Leave Galilee and go to Judea, so that your disciples there may see the works you do. No one who wants to become a public figure acts in secret. Since you are doing these things, show yourself to the world.” For even his own brothers did not believe in him.(E)

Therefore Jesus told them, “My time(F) is not yet here; for you any time will do. The world cannot hate you, but it hates me(G) because I testify that its works are evil.(H) You go to the festival. I am not[b] going up to this festival, because my time(I) has not yet fully come.” After he had said this, he stayed in Galilee.

10 However, after his brothers had left for the festival, he went also, not publicly, but in secret. 11 Now at the festival the Jewish leaders were watching for Jesus(J) and asking, “Where is he?”

12 Among the crowds there was widespread whispering about him. Some said, “He is a good man.”

Others replied, “No, he deceives the people.”(K) 13 But no one would say anything publicly about him for fear of the leaders.(L)

Jesus Teaches at the Festival

14 Not until halfway through the festival did Jesus go up to the temple courts and begin to teach.(M) 15 The Jews(N) there were amazed and asked, “How did this man get such learning(O) without having been taught?”(P)

16 Jesus answered, “My teaching is not my own. It comes from the one who sent me.(Q) 17 Anyone who chooses to do the will of God will find out(R) whether my teaching comes from God or whether I speak on my own. 18 Whoever speaks on their own does so to gain personal glory,(S) but he who seeks the glory of the one who sent him is a man of truth; there is nothing false about him. 19 Has not Moses given you the law?(T) Yet not one of you keeps the law. Why are you trying to kill me?”(U)

20 “You are demon-possessed,”(V) the crowd answered. “Who is trying to kill you?”

21 Jesus said to them, “I did one miracle,(W) and you are all amazed. 22 Yet, because Moses gave you circumcision(X) (though actually it did not come from Moses, but from the patriarchs),(Y) you circumcise a boy on the Sabbath. 23 Now if a boy can be circumcised on the Sabbath so that the law of Moses may not be broken, why are you angry with me for healing a man’s whole body on the Sabbath? 24 Stop judging by mere appearances, but instead judge correctly.”(Z)

Division Over Who Jesus Is

25 At that point some of the people of Jerusalem began to ask, “Isn’t this the man they are trying to kill?(AA) 26 Here he is, speaking publicly, and they are not saying a word to him. Have the authorities(AB) really concluded that he is the Messiah?(AC) 27 But we know where this man is from;(AD) when the Messiah comes, no one will know where he is from.”

28 Then Jesus, still teaching in the temple courts,(AE) cried out, “Yes, you know me, and you know where I am from.(AF) I am not here on my own authority, but he who sent me is true.(AG) You do not know him, 29 but I know him(AH) because I am from him and he sent me.”(AI)

30 At this they tried to seize him, but no one laid a hand on him,(AJ) because his hour had not yet come.(AK) 31 Still, many in the crowd believed in him.(AL) They said, “When the Messiah comes, will he perform more signs(AM) than this man?”

32 The Pharisees heard the crowd whispering such things about him. Then the chief priests and the Pharisees sent temple guards to arrest him.

33 Jesus said, “I am with you for only a short time,(AN) and then I am going to the one who sent me.(AO) 34 You will look for me, but you will not find me; and where I am, you cannot come.”(AP)

35 The Jews said to one another, “Where does this man intend to go that we cannot find him? Will he go where our people live scattered(AQ) among the Greeks,(AR) and teach the Greeks? 36 What did he mean when he said, ‘You will look for me, but you will not find me,’ and ‘Where I am, you cannot come’?”(AS)

37 On the last and greatest day of the festival,(AT) Jesus stood and said in a loud voice, “Let anyone who is thirsty come to me and drink.(AU) 38 Whoever believes(AV) in me, as Scripture has said,(AW) rivers of living water(AX) will flow from within them.”[c](AY) 39 By this he meant the Spirit,(AZ) whom those who believed in him were later to receive.(BA) Up to that time the Spirit had not been given, since Jesus had not yet been glorified.(BB)

40 On hearing his words, some of the people said, “Surely this man is the Prophet.”(BC)

41 Others said, “He is the Messiah.”

Still others asked, “How can the Messiah come from Galilee?(BD) 42 Does not Scripture say that the Messiah will come from David’s descendants(BE) and from Bethlehem,(BF) the town where David lived?” 43 Thus the people were divided(BG) because of Jesus. 44 Some wanted to seize him, but no one laid a hand on him.(BH)

Unbelief of the Jewish Leaders

45 Finally the temple guards went back to the chief priests and the Pharisees, who asked them, “Why didn’t you bring him in?”

46 “No one ever spoke the way this man does,”(BI) the guards replied.

47 “You mean he has deceived you also?”(BJ) the Pharisees retorted. 48 “Have any of the rulers or of the Pharisees believed in him?(BK) 49 No! But this mob that knows nothing of the law—there is a curse on them.”

50 Nicodemus,(BL) who had gone to Jesus earlier and who was one of their own number, asked, 51 “Does our law condemn a man without first hearing him to find out what he has been doing?”

52 They replied, “Are you from Galilee, too? Look into it, and you will find that a prophet does not come out of Galilee.”(BM)


[The earliest manuscripts and many other ancient witnesses do not have John 7:53—8:11. A few manuscripts include these verses, wholly or in part, after John 7:36, John 21:25, Luke 21:38 or Luke 24:53.]

53 Then they all went home,

Footnotes

  1. John 7:1 Some manuscripts not have authority
  2. John 7:8 Some manuscripts not yet
  3. John 7:38 Or me. And let anyone drink 38 who believes in me.” As Scripture has said, “Out of him (or them) will flow rivers of living water.”