Add parallel Print Page Options

Yesu Aphunzitsa Nekodimo za Kubadwa Kwatsopano

Ndipo panali Mfarisi wotchedwa Nekodimo, wa mʼgulu lolamulira la Ayuda. Iye anabwera kwa Yesu usiku ndipo anati, “Rabi, ife tikudziwa kuti ndinu aphunzitsi wochokera kwa Mulungu, pakuti palibe amene angachite zizindikiro zodabwitsa zimene Inu mukuchita ngati Mulungu sali naye.”

Poyankha Yesu ananena kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti, ngati munthu sabadwanso mwatsopano sangathe kuona ufumu wa Mulungu.”

Nekodimo anati, “Kodi munthu angabadwenso bwanji atakalamba? Kodi angalowe kachiwiri mʼmimba ya amayi ake kuti abadwenso?”

Yesu anayankha kuti, “Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ngati munthu sabadwa mwa madzi ndi Mzimu Woyera, sangalowe mu ufumu wa Mulungu. Thupi limabereka thupi, koma Mzimu amabereka mzimu. Iwe usadabwe chifukwa ndakuwuza kuti, ‘Uyenera kubadwanso.’ Mphepo imawomba kulikonse kumene ikufuna. Ungathe kumva kuwomba kwake, koma sungathe kudziwa kumene ikuchokera kapena kumene ikupita. Nʼchimodzimodzi ndi amene abadwa ndi Mzimu Woyera.”

Nekodimo anafunsa kuti, “Kodi izi zingatheke bwanji?”

10 Yesu anati, “Iwe mphunzitsi wa Israeli, kodi sukuzindikira zimenezi? 11 Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti ife tiyankhula zimene tikuzidziwa ndi kuchitira umboni zimene taziona, komabe inu simuvomereza umboni wathu. 12 Ine ndikuyankhula kwa iwe zinthu za dziko lapansi ndipo sukukhulupirira. Nanga kodi udzakhulupirira bwanji ngati nditayankhula zinthu zakumwamba? 13 Palibe wina aliyense anapita kumwamba, koma yekhayo amene watsika kuchokera kumwamba, Mwana wa Munthu. 14 Tsono monga Mose anapachika njoka mʼchipululu, moteronso Mwana wa Munthu ayenera kupachikidwa, 15 kuti aliyense amene akhulupirira Iye akhale ndi moyo wosatha.

16 “Pakuti Mulungu anakonda dziko lapansi, kotero anapereka Mwana wake wobadwa yekha, kuti aliyense wokhulupirira Iye asatayike koma akhale ndi moyo wosatha. 17 Pakuti Mulungu sanatume Mwana wake ku dziko lapansi, kuti akaweruze, koma kuti akapulumutse dziko lapansi. 18 Aliyense wokhulupirira Iye saweruzidwa, koma aliyense wosakhulupirira waweruzidwa kale chifukwa sanakhulupirire dzina la Mwana wobadwa yekha wa Mulungu. 19 Ndipo chiweruzo ndi ichi: kuwunika kunabwera mʼdziko lapansi, koma anthu anakonda mdima mʼmalo mwa kuwunikako, chifukwa ntchito zawo zinali zoyipa. 20 Aliyense wochita zoyipa amadana ndi kuwunika, ndipo sabwera poyera chifukwa cha mantha kuti ntchito zake zingaonekere. 21 Koma aliyense wokhala mu choonadi amabwera ku kuwunika, kuti zionekere poyera zimene iye wachita zachitika kudzera mwa Mulungu.”

Yohane Mʼbatizi Achita Umboni za Yesu

22 Zitatha izi, Yesu ndi ophunzira ake anapita mʼmadera a ku midzi ya ku Yudeya, kumene Iye anakhala kanthawi akubatiza. 23 Ndipo Yohane amabatizanso ku Ainoni kufupi ndi Salimu, chifukwa kumeneko kunali madzi ambiri ndipo anthu amabwererabwererabe kudzabatizidwa. 24 (Apa nʼkuti Yohane asanatsekeredwe mʼndende). 25 Mkangano unabuka pakati pa ophunzira ena a Yohane ndi Ayuda ena pa zamwambo wodziyeretsa wa Ayuda. 26 Iwo anabwera kwa Yohane anati, “Rabi, munthu uja munali naye mbali inayo ya mu mtsinje wa Yorodani, amene munamuchitira umboni, taonani naye akubatizanso, ndipo aliyense akupita kwa Iye.”

27 Atamva zimenezi, Yohane anayankha kuti, “Munthu amalandira chokhacho chapatsidwa kwa iye kuchokera kumwamba. 28 Inuyo ndinu mboni zanga kuti ine ndinati, ‘Ine sindine Khristu koma ndatumidwa patsogolo pa Iye.’ 29 Mwini wake wa mkwatibwi ndi mkwati. Ndipo bwenzi lamkwati limadikira ndi kumvetsera iye, ndipo amakondwa akamva mawu a mkwatiyo. Ine changa ndi chimwemwe ndipo ndine wosangalala kwambiri. 30 Nʼkoyenera kuti Iyeyo akule, ine ndichepe.

31 “Iye wochokera kumwamba ndi wapamwamba pa onse: iye wochokera mʼdziko lapansi ndi wa dziko lapansi, ndipo amayankhula monga mmodzi wa adziko lapansi. Iye wochokera kumwamba ndi wopambana onse. 32 Iye achita umboni pa zimene waziona ndi kuzimva, koma palibe avomereza umboni wake. 33 Munthu amene amawulandira akutsimikizira kuti Mulungu ndi woona. 34 Pakuti amene Mulungu wamutuma amayankhula mawu a Mulungu; Mulungu wamupatsa Mzimu Woyera mopanda malire. 35 Atate amakonda Mwana ndipo apereka zonse mʼmanja mwake. 36 Aliyense wokhulupirira Mwanayo ali ndi moyo wosatha, koma iye amene samvera Mwanayo sadzawuona moyo, pakuti mkwiyo wa Mulungu umakhala pa iye.”

Jesus Teaches Nicodemus

Now there was a Pharisee, a man named Nicodemus(A) who was a member of the Jewish ruling council.(B) He came to Jesus at night and said, “Rabbi,(C) we know(D) that you are a teacher who has come from God. For no one could perform the signs(E) you are doing if God were not with him.”(F)

Jesus replied, “Very truly I tell you, no one can see the kingdom of God unless they are born again.[a](G)

“How can someone be born when they are old?” Nicodemus asked. “Surely they cannot enter a second time into their mother’s womb to be born!”

Jesus answered, “Very truly I tell you, no one can enter the kingdom of God unless they are born of water and the Spirit.(H) Flesh gives birth to flesh, but the Spirit[b] gives birth to spirit.(I) You should not be surprised at my saying, ‘You[c] must be born again.’ The wind blows wherever it pleases. You hear its sound, but you cannot tell where it comes from or where it is going. So it is with everyone born of the Spirit.”[d](J)

“How can this be?”(K) Nicodemus asked.

10 “You are Israel’s teacher,”(L) said Jesus, “and do you not understand these things? 11 Very truly I tell you, we speak of what we know,(M) and we testify to what we have seen, but still you people do not accept our testimony.(N) 12 I have spoken to you of earthly things and you do not believe; how then will you believe if I speak of heavenly things? 13 No one has ever gone into heaven(O) except the one who came from heaven(P)—the Son of Man.[e](Q) 14 Just as Moses lifted up the snake in the wilderness,(R) so the Son of Man must be lifted up,[f](S) 15 that everyone who believes(T) may have eternal life in him.”[g](U)

16 For God so loved(V) the world that he gave(W) his one and only Son,(X) that whoever believes(Y) in him shall not perish but have eternal life.(Z) 17 For God did not send his Son into the world(AA) to condemn the world, but to save the world through him.(AB) 18 Whoever believes in him is not condemned,(AC) but whoever does not believe stands condemned already because they have not believed in the name of God’s one and only Son.(AD) 19 This is the verdict: Light(AE) has come into the world, but people loved darkness instead of light because their deeds were evil.(AF) 20 Everyone who does evil hates the light, and will not come into the light for fear that their deeds will be exposed.(AG) 21 But whoever lives by the truth comes into the light, so that it may be seen plainly that what they have done has been done in the sight of God.

John Testifies Again About Jesus

22 After this, Jesus and his disciples went out into the Judean countryside, where he spent some time with them, and baptized.(AH) 23 Now John(AI) also was baptizing at Aenon near Salim, because there was plenty of water, and people were coming and being baptized. 24 (This was before John was put in prison.)(AJ) 25 An argument developed between some of John’s disciples and a certain Jew over the matter of ceremonial washing.(AK) 26 They came to John and said to him, “Rabbi,(AL) that man who was with you on the other side of the Jordan—the one you testified(AM) about—look, he is baptizing, and everyone is going to him.”

27 To this John replied, “A person can receive only what is given them from heaven. 28 You yourselves can testify that I said, ‘I am not the Messiah but am sent ahead of him.’(AN) 29 The bride belongs to the bridegroom.(AO) The friend who attends the bridegroom waits and listens for him, and is full of joy when he hears the bridegroom’s voice. That joy is mine, and it is now complete.(AP) 30 He must become greater; I must become less.”[h]

31 The one who comes from above(AQ) is above all; the one who is from the earth belongs to the earth, and speaks as one from the earth.(AR) The one who comes from heaven is above all. 32 He testifies to what he has seen and heard,(AS) but no one accepts his testimony.(AT) 33 Whoever has accepted it has certified that God is truthful. 34 For the one whom God has sent(AU) speaks the words of God, for God[i] gives the Spirit(AV) without limit. 35 The Father loves the Son and has placed everything in his hands.(AW) 36 Whoever believes in the Son has eternal life,(AX) but whoever rejects the Son will not see life, for God’s wrath remains on them.

Footnotes

  1. John 3:3 The Greek for again also means from above; also in verse 7.
  2. John 3:6 Or but spirit
  3. John 3:7 The Greek is plural.
  4. John 3:8 The Greek for Spirit is the same as that for wind.
  5. John 3:13 Some manuscripts Man, who is in heaven
  6. John 3:14 The Greek for lifted up also means exalted.
  7. John 3:15 Some interpreters end the quotation with verse 21.
  8. John 3:30 Some interpreters end the quotation with verse 36.
  9. John 3:34 Greek he