Add parallel Print Page Options

Yesu Adzipempherera Yekha

17 Yesu atatha kunena izi, anayangʼana kumwamba ndipo anapemphera:

“Atate, nthawi yafika. Lemekezani Mwana wanu, kuti Mwana wanuyo akulemekezeni Inu. Pakuti Inu munamupatsa Iye ulamuliro pa anthu onse kuti apereke moyo wosatha kwa onse amene mwamupatsa. Tsono moyo wosathawo ndi uwu: Iwo akudziweni Inu, Mulungu yekhayo woona, ndi Yesu Khristu, amene Inu mwamutuma. Ine ndabweretsa ulemerero wanu pa dziko pamene ndamaliza ntchito imene munandipatsa kuti ndi igwire. Ndipo tsopano, Atate, ndilemekezeni Ine pamaso panu ndi ulemerero uja umene ndinali nawo kwa Inu dziko lapansi lisanayambe.

Yesu Apempherera Ophunzira Ake

“Ine ndawadziwitsa za Inu anthu amene munandipatsa mʼdziko lapansi. Iwo anali anu. Inu munawapereka kwa Ine ndipo amvera mawu anu. Tsopano akudziwa kuti zonse zimene munandipatsa nʼzochokera kwa Inu. Pakuti Ine ndiwapatsa mawu amene Inu munandipatsa ndipo awalandira. Iwo akudziwa ndithu kuti Ine ndinachokera kwa Inu, ndipo akukhulupirira kuti Inu ndiye amene munandituma Ine. Ine ndikuwapempherera. Ine sindikupempherera dziko lapansi, koma anthu amene Inu mwandipatsa, pakuti ndi anu. 10 Zonse zimene Ine ndili nazo ndi zanu, ndipo zonse zimene Inu muli nazo ndi zanga. Choncho Ine ndalemekezedwa mwa iwowo. 11 Ine sindikukhalanso mʼdziko lapansi nthawi yayitali, koma iwo akanali mʼdziko lapansi. Ine ndikubwera kwa Inu. Atate Woyera, atetezeni ndi mphamvu za dzina lanu. Dzina limene munandipatsa Ine, kuti iwo akhale amodzi monga Ife tili amodzi. 12 Pamene ndinali nawo, ndinawateteza ndi kuwasunga mosamala mʼdzina limene munandipatsa. Palibe ndi mmodzi yemwe amene anatayika kupatula yekhayo amene anayenera kuwonongeka kuti malemba akwaniritsidwe.

13 “Tsopano ndikubwera kwa Inu. Ndikunena izi ndikanali mʼdziko lapansi, kuti iwo akhale ndi muyeso wodzaza wachimwemwe changa mʼkati mwawo. 14 Ine ndawapatsa mawu anu ndipo dziko lapansi likudana nawo, pakuti sali a dziko lapansi monga Ine sindilinso wa dziko lapansi. 15 Sindikupempha kuti muwachotse mʼdziko lapansi koma kuti muwateteze kwa woyipayo. 16 Iwo si a dziko lapansi, monga Ine sindilinso wa dziko lapansi. 17 Ayeretseni ndi choonadi chanu. Mawu anu ndiye choonadi. 18 Monga Inu munandituma Ine mʼdziko lapansi, Inenso ndikuwatuma mʼdziko lapansi. 19 Chifukwa cha iwowa Ine ndikudziyeretsa, kuti iwo ayeretsedwenso kwenikweni.

Yesu Apempherera Okhulupirira Onse

20 “Ine sindikupempherera iwo okhawa, komanso amene adzandikhulupirira chifukwa cha uthenga wawo. 21 Ndikuwapempherera kuti onsewa akhale amodzi. Monga Inu Atate muli mwa Ine ndi Ine mwa Inu, iwonso akhale mwa Ife kuti dziko lapansi likhulupirire kuti Inu munandituma Ine. 22 Ine ndawapatsa ulemerero umene munandipatsa Ine, kuti akhale amodzi monga Ife tili amodzi. 23 Ine ndikhale mwa iwo ndipo Inu mwa Ine kuti umodzi wawo ukhale wangwiro. Choncho dziko lapansi lidzadziwa kuti Inu munandituma Ine ndipo Inu mwawakonda iwowa monga momwe Inu munandikondera Ine.

24 “Atate, Ine ndikufuna kuti anthu amene mwandipatsa Ine adzakhale ndi Ine kumene kuli Ine, ndi kuona ulemerero wanga, ulemerero umene munandipatsa chifukwa Inu munandikonda dziko lapansi lisanalengedwe.

25 “Atate wolungama, ngakhale kuti dziko lapansi silikudziwani Inu, Ine ndimakudziwani, ndipo iwo amadziwa kuti Inu munandituma Ine. 26 Ine ndawadziwitsa dzina lanu, ndipo ndidzapitiriza kuwadziwitsa dzina lanulo, kuti chikondi chomwe munandikonda nacho chikhale mwa iwo, ndipo Ine mwa iwo.”

Jesus Prays to Be Glorified

17 After Jesus said this, he looked toward heaven(A) and prayed:

“Father, the hour has come.(B) Glorify your Son, that your Son may glorify you.(C) For you granted him authority over all people(D) that he might give eternal life(E) to all those you have given him.(F) Now this is eternal life: that they know you,(G) the only true God, and Jesus Christ, whom you have sent.(H) I have brought you glory(I) on earth by finishing the work you gave me to do.(J) And now, Father, glorify me(K) in your presence with the glory I had with you(L) before the world began.(M)

Jesus Prays for His Disciples

“I have revealed you[a](N) to those whom you gave me(O) out of the world. They were yours; you gave them to me and they have obeyed your word. Now they know that everything you have given me comes from you. For I gave them the words you gave me(P) and they accepted them. They knew with certainty that I came from you,(Q) and they believed that you sent me.(R) I pray for them.(S) I am not praying for the world, but for those you have given me,(T) for they are yours. 10 All I have is yours, and all you have is mine.(U) And glory has come to me through them. 11 I will remain in the world no longer, but they are still in the world,(V) and I am coming to you.(W) Holy Father, protect them by the power of[b] your name, the name you gave me, so that they may be one(X) as we are one.(Y) 12 While I was with them, I protected them and kept them safe by[c] that name you gave me. None has been lost(Z) except the one doomed to destruction(AA) so that Scripture would be fulfilled.(AB)

13 “I am coming to you now,(AC) but I say these things while I am still in the world, so that they may have the full measure of my joy(AD) within them. 14 I have given them your word and the world has hated them,(AE) for they are not of the world any more than I am of the world.(AF) 15 My prayer is not that you take them out of the world but that you protect them from the evil one.(AG) 16 They are not of the world, even as I am not of it.(AH) 17 Sanctify them by[d] the truth; your word is truth.(AI) 18 As you sent me into the world,(AJ) I have sent them into the world.(AK) 19 For them I sanctify myself, that they too may be truly sanctified.(AL)

Jesus Prays for All Believers

20 “My prayer is not for them alone. I pray also for those who will believe in me through their message, 21 that all of them may be one,(AM) Father, just as you are in me and I am in you.(AN) May they also be in us so that the world may believe that you have sent me.(AO) 22 I have given them the glory that you gave me,(AP) that they may be one as we are one(AQ) 23 I in them and you in me—so that they may be brought to complete unity. Then the world will know that you sent me(AR) and have loved them(AS) even as you have loved me.

24 “Father, I want those you have given me(AT) to be with me where I am,(AU) and to see my glory,(AV) the glory you have given me because you loved me before the creation of the world.(AW)

25 “Righteous Father, though the world does not know you,(AX) I know you, and they know that you have sent me.(AY) 26 I have made you[e] known to them,(AZ) and will continue to make you known in order that the love you have for me may be in them(BA) and that I myself may be in them.”

Footnotes

  1. John 17:6 Greek your name
  2. John 17:11 Or Father, keep them faithful to
  3. John 17:12 Or kept them faithful to
  4. John 17:17 Or them to live in accordance with
  5. John 17:26 Greek your name