Add parallel Print Page Options

Mpesa ndi Nthambi

15 “Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate anga ndiye mwini munda. Iye amadula nthambi iliyonse ya mwa Ine imene sibala chipatso, koma nthambi iliyonse imene imabala chipatso amayisadzira bwino kuti ibale zipatso zambiri. Inu ndinu oyera kale chifukwa cha mawu amene ndayankhula inu. Khalani mwa Ine, monga Ine ndili mwa inu. Palibe nthambi imene ingabereke chipatso pa yokha ngati sinalumikizike ku mpesa. Chomwechonso inu simungathe kubereka chipatso pokhapokha mutakhala mwa Ine.

“Ine ndine mpesa; inu ndinu nthambi zake. Ngati munthu akhala mwa Ine ndi Ine mwa iye, adzabereka zipatso zambiri; popanda Ine simungathe kuchita kanthu. Ngati wina aliyense sakhala mwa Ine, iyeyo ali ngati nthambi imene yatayidwa ndi kufota. Nthambi zotero zimatoledwa, kuponyedwa pa moto ndi kupsa. Ngati inu mukhala mwa Ine ndipo mawu anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene mukufuna ndipo mudzapatsidwa. Atate anga amalemekezedwa mukamabereka zipatso zochuluka, ndipo potero mudzionetsa kuti ndinu ophunzira anga.

“Monga momwe Atate amandikondera Ine, Inenso ndakukondani. Tsopano khalani mʼchikondi changa. 10 Ngati mumvera malamulo anga, mudzakhala mʼchikondi changa, monga Ine ndimamvera malamulo a Atate anga, ndipo ndimakhala mʼchikondi chawo. 11 Ine ndakuwuzani izi kuti chimwemwe changa chikhale mwa Inu, kuti chimwemwe chanu chikhale chokwanira. 12 Lamulo langa ndi ili: ‘Kondanani wina ndi mnzake monga Ine ndakonda inu.’ 13 Palibe munthu ali ndi chikondi choposa ichi, choti munthu nʼkutaya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake. 14 Inu ndinu abwenzi anga ngati muchita zimene Ine ndikulamulani. 15 Ine sindikutchulaninso antchito, chifukwa wantchito sadziwa zimene bwana wake akuchita. Mʼmalo mwake Ine ndakutchani abwenzi pakuti zilizonse zimene ndinaphunzira kwa Atate, Ine ndakudziwitsani. 16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani kuti mupite ndi kukabereka zipatso, zipatso zake za nthawi yayitali. Choncho Atate adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa. 17 Lamulo langa ndi ili: ‘Muzikondana.’

Dziko Lapansi Limada Ophunzira a Yesu

18 “Ngati dziko lapansi lidana nanu, dziwani kuti linayamba kudana ndi Ine. 19 Inu mukanakhala anthu a dziko lapansi, dziko lapansi likanakukondani ngati anthu ake omwe. Koma mmene zilili, inu si anthu a dziko lapansi. Ine ndakusankhani kuchokera mʼdziko lapansi, nʼchifukwa chake dziko lapansi limakudani. 20 Kumbukirani mawu amene ndinayankhula nanu akuti, ‘Palibe wantchito amene amaposa bwana wake.’ Ngati anandizunza Ine, iwo adzakuzunzaninso inu. Ngati anamvera chiphunzitso changa, iwo adzamvera chanunso. 21 Iwo adzakuchitani zimenezi chifukwa cha dzina langa, popeza sakudziwa amene anandituma Ine. 22 Ine ndikanapanda kubwera ndi kuyankhula nawo, sakanakhala ndi mlandu. Koma tsopano alibe choti nʼkukanira mlandu wawo. 23 Iye amene amadana ndi Ine amadananso Atate anga. 24 Ine ndikanapanda kuchita pakati pawo zinthu zimene wina aliyense sanachitepo, iwo sakanakhala ochimwa. Koma tsopano aona zodabwitsa izi, komabe akundida Ine pamodzi ndi Atate anga. 25 Koma zatere kuti zikwaniritse zimene zinalembedwa mʼmalamulo awo: ‘Iwo anandida Ine popanda chifukwa.’

Ntchito ya Mzimu Woyera

26 “Nkhoswe ikadzabwera imene Ine ndidzakutumizireni kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu Woyera wachoonadi amene achokera kwa Atate, Iyeyo adzandichitira umboni Ine. 27 Inunso mudzandichitira umboni Ine, popeza mwakhala nane kuchokera pachiyambi.”

The Vine and the Branches

15 “I am(A) the true vine,(B) and my Father is the gardener. He cuts off every branch in me that bears no fruit,(C) while every branch that does bear fruit(D) he prunes[a] so that it will be even more fruitful. You are already clean because of the word I have spoken to you.(E) Remain in me, as I also remain in you.(F) No branch can bear fruit by itself; it must remain in the vine. Neither can you bear fruit unless you remain in me.

“I am the vine; you are the branches. If you remain in me and I in you, you will bear much fruit;(G) apart from me you can do nothing. If you do not remain in me, you are like a branch that is thrown away and withers; such branches are picked up, thrown into the fire and burned.(H) If you remain in me(I) and my words remain in you, ask whatever you wish, and it will be done for you.(J) This is to my Father’s glory,(K) that you bear much fruit, showing yourselves to be my disciples.(L)

“As the Father has loved me,(M) so have I loved you. Now remain in my love. 10 If you keep my commands,(N) you will remain in my love, just as I have kept my Father’s commands and remain in his love. 11 I have told you this so that my joy may be in you and that your joy may be complete.(O) 12 My command is this: Love each other as I have loved you.(P) 13 Greater love has no one than this: to lay down one’s life for one’s friends.(Q) 14 You are my friends(R) if you do what I command.(S) 15 I no longer call you servants, because a servant does not know his master’s business. Instead, I have called you friends, for everything that I learned from my Father I have made known to you.(T) 16 You did not choose me, but I chose you and appointed you(U) so that you might go and bear fruit(V)—fruit that will last—and so that whatever you ask in my name the Father will give you.(W) 17 This is my command: Love each other.(X)

The World Hates the Disciples

18 “If the world hates you,(Y) keep in mind that it hated me first. 19 If you belonged to the world, it would love you as its own. As it is, you do not belong to the world, but I have chosen you(Z) out of the world. That is why the world hates you.(AA) 20 Remember what I told you: ‘A servant is not greater than his master.’[b](AB) If they persecuted me, they will persecute you also.(AC) If they obeyed my teaching, they will obey yours also. 21 They will treat you this way because of my name,(AD) for they do not know the one who sent me.(AE) 22 If I had not come and spoken to them,(AF) they would not be guilty of sin; but now they have no excuse for their sin.(AG) 23 Whoever hates me hates my Father as well. 24 If I had not done among them the works no one else did,(AH) they would not be guilty of sin.(AI) As it is, they have seen, and yet they have hated both me and my Father. 25 But this is to fulfill what is written in their Law:(AJ) ‘They hated me without reason.’[c](AK)

The Work of the Holy Spirit

26 “When the Advocate(AL) comes, whom I will send to you from the Father(AM)—the Spirit of truth(AN) who goes out from the Father—he will testify about me.(AO) 27 And you also must testify,(AP) for you have been with me from the beginning.(AQ)

Footnotes

  1. John 15:2 The Greek for he prunes also means he cleans.
  2. John 15:20 John 13:16
  3. John 15:25 Psalms 35:19; 69:4