Add parallel Print Page Options

“Itana ngati ungathe, koma ndani adzakuyankhe?
    Kodi ndi kwa mngelo uti ungapezeko thandizo?
Mkwiyo umapha chitsiru,
    ndipo njiru imawononga wopusa.
Ine ndinaona chitsiru chitamera mizu,
    koma mwadzidzidzi nyumba yake inatembereredwa.
Ana ake alibe ndi chitetezo chomwe;
    amaponderezedwa mʼbwalo la milandu popanda owateteza.
Anthu anjala amamudyera zokolola zake,
    amamutengera ndi za pa minga pomwe,
    ndipo anthu akhwinthi amafunkha chuma chake.
Pakuti masautso satuluka mʼfumbi,
    ndipo kuwukira sikuchokera mʼdothi.
Komatu munthu amabadwira kuti azunzike
    monga momwe mbaliwali zimathethekera mlengalenga.

“Koma ndikanakhala ine, ndikanamudandawulira Mulungu;
    ndikanapereka mlandu wanga kwa Iye.
Iye amachita zozizwitsa zimene sizimvetsetseka,
    zodabwitsa zimene sizingatheke kuwerengedwa.
10 Iye amagwetsa mvula pa dziko lapansi,
    ndipo amathirira minda ya anthu.
11 Iye amakweza anthu wamba,
    ndipo iwo amene akulira amawayika pa malo otetezedwa.
12 Iyeyo amalepheretsa chiwembu cha anthu ochenjera,
    kotero kuti cholinga chawo sichipindula kanthu.
13 Iye amakola anthu ochenjera mu msampha wa kuchenjera kwawo,
    ndipo zolinga za atambwali amazithetsa msangamsanga.
14 Mdima umawagwera nthawi yamasana;
    nthawi yamasana amayenda moyambasayambasa monga nthawi ya usiku.
15 Mulungu amapulumutsa amphawi ku lupanga la mʼkamwa mwawo;
    amawapulumutsa mʼmanja mwa anthu amphamvu.
16 Choncho osauka ali ndi chiyembekezo,
    ndipo anthu opanda chilungamo amawatseka pakamwa.

17 “Wodala munthu amene Mulungu amamudzudzula;
    nʼchifukwa chake usanyoze chilango cha Wamphamvuzonse.
18 Pakuti Iye amavulaza koma amamanganso mabalawo;
    Iye amakantha munthu, komanso manja ake amachiritsa.
19 Pakuti adzakupulumutsa ku masautso nthawi ndi nthawi,
    mavuto angachuluke bwanji, sadzakukhudza ndi pangʼono pomwe.
20 Pa nthawi ya njala adzakulanditsa ku imfa,
    ndipo nthawi ya nkhondo adzakupulumutsa ku lupanga.
21 Adzakuteteza kwa anthu osinjirira,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha pamene chiwonongeko chafika.
22 Uzidzaseka pa nthawi ya chiwonongeko ndi ya njala,
    ndipo palibe chifukwa chochitira mantha ndi zirombo za mʼdziko lapansi.
23 Pakuti udzachita pangano ndi miyala ya mʼmunda mwako,
    ndipo nyama zakuthengo zidzakhala nawe mwamtendere.
24 Udzadziwa kuti nyumba yako ndi malo otetezedwa;
    udzawerengera katundu wako ndipo sudzapeza kanthu kamene kasowapo.
25 Udzadziwa kuti ana ako adzakhala ambiri,
    ndipo zidzukulu zako zidzakhala ngati udzu wa mʼdziko lapansi.
26 Udzafika ku manda utakalamba,
    monga mitolo ya zokolola pa nyengo yake.

27 “Ife tafufuza zimenezi ndipo ndi zoona,
    choncho uzimvere ndi kuzitsata.”

“Call if you will, but who will answer you?(A)
    To which of the holy ones(B) will you turn?
Resentment(C) kills a fool,
    and envy slays the simple.(D)
I myself have seen(E) a fool taking root,(F)
    but suddenly(G) his house was cursed.(H)
His children(I) are far from safety,(J)
    crushed in court(K) without a defender.(L)
The hungry consume his harvest,(M)
    taking it even from among thorns,
    and the thirsty pant after his wealth.
For hardship does not spring from the soil,
    nor does trouble sprout from the ground.(N)
Yet man is born to trouble(O)
    as surely as sparks fly upward.

“But if I were you, I would appeal to God;
    I would lay my cause before him.(P)
He performs wonders(Q) that cannot be fathomed,(R)
    miracles that cannot be counted.(S)
10 He provides rain for the earth;(T)
    he sends water on the countryside.(U)
11 The lowly he sets on high,(V)
    and those who mourn(W) are lifted(X) to safety.
12 He thwarts the plans(Y) of the crafty,
    so that their hands achieve no success.(Z)
13 He catches the wise(AA) in their craftiness,(AB)
    and the schemes of the wily are swept away.(AC)
14 Darkness(AD) comes upon them in the daytime;
    at noon they grope as in the night.(AE)
15 He saves the needy(AF) from the sword in their mouth;
    he saves them from the clutches of the powerful.(AG)
16 So the poor(AH) have hope,
    and injustice shuts its mouth.(AI)

17 “Blessed is the one whom God corrects;(AJ)
    so do not despise the discipline(AK) of the Almighty.[a](AL)
18 For he wounds, but he also binds up;(AM)
    he injures, but his hands also heal.(AN)
19 From six calamities he will rescue(AO) you;
    in seven no harm will touch you.(AP)
20 In famine(AQ) he will deliver you from death,
    and in battle from the stroke of the sword.(AR)
21 You will be protected from the lash of the tongue,(AS)
    and need not fear(AT) when destruction comes.(AU)
22 You will laugh(AV) at destruction and famine,(AW)
    and need not fear the wild animals.(AX)
23 For you will have a covenant(AY) with the stones(AZ) of the field,
    and the wild animals will be at peace with you.(BA)
24 You will know that your tent is secure;(BB)
    you will take stock of your property and find nothing missing.(BC)
25 You will know that your children will be many,(BD)
    and your descendants like the grass of the earth.(BE)
26 You will come to the grave in full vigor,(BF)
    like sheaves gathered in season.(BG)

27 “We have examined this, and it is true.
    So hear it(BH) and apply it to yourself.”(BI)

Footnotes

  1. Job 5:17 Hebrew Shaddai; here and throughout Job