Yobu 37
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
37 “Mtima wanga ukulumphalumpha pa chimenechinso
ndipo ukuchoka mʼmalo mwake.
2 Tamverani! Tamverani kubangula kwa liwu lake,
kugunda kumene kukuchokera mʼkamwa mwake.
3 Iye amaponya chingʼaningʼani chake pansi pa thambo lonse
ndipo amachitumiza ku dziko lapansi.
4 Pambuyo pake kubangula kwake kumamveka.
Iye amabangula ndi liwu lake laulemerero.
Pamene wabangula,
palibe chimene amalephera kuchita.
5 Liwu la Mulungu limabangula mʼnjira zambiri zodabwitsa
Iye amachita zinthu zazikulu zimene sitingathe kuzimvetsa.
6 Amalamula chisanu chowundana kuti, ‘Igwa pa dziko lapansi,’
ndipo amalamulanso mvula yamawawa kuti, ‘Khala mvula yamphamvu.’
7 Kuti anthu onse amene anawalenga athe kuzindikira ntchito yake.
Iye amalepheretsa anthu kugwira ntchito zawo.
8 Zirombo zimakabisala
ndipo zimakhala mʼmaenje mwawo.
9 Mphepo yamkuntho imatuluka ku malo ake,
kuzizira kumatuluka mʼmphepo yamkunthoyo.
10 Mpweya wa Mulungu umawunditsa madzi
ndipo madzi a mʼnyanja amawuma kuti gwaa.
11 Iye amadzaza mitambo ndi madzi a mvula,
amabalalitsa zingʼaningʼani zake kuchokera mʼmitambomo.
12 Mulungu amayendetsa mitamboyo
mozungulirazungulira dziko lonse lapansi
kuti ichite zonse zimene Iye akufuna pa dziko lapansi.
13 Iye amagwetsa mvula kuti alange anthu,
kapena kubweretsa chinyontho pa dziko lapansi kuti aonetse chikondi chake.
14 “Abambo Yobu, tamvani izi;
imani ndipo muganizire ntchito zodabwitsa za Mulungu.
15 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayendetsera mitambo
ndi kuchititsa kuti kukhale zingʼaningʼani?
16 Kodi mukudziwa momwe Mulungu amayalira mitambo,
ntchito zodabwitsa za Iye amene ndi wanzeru zangwiro?
17 Inu amene mʼzovala zanu mumatuluka thukuta
pamene kunja kwatentha chifukwa cha mphepo yakummwera,
18 kodi mungathe kuthandizana naye kutambasula thambo
limene ndi lolimba ngati chitsulo?
19 “Tiwuzeni ife zoti tikanene kwa Iye;
sitingathe kufotokoza mlandu wathu chifukwa cha mdima umene uli mwa ife.
20 Kodi nʼkofunika kumudziwitsa Mulungu kuti ndili naye mawu?
Kodi kutero sikuchita ngati kupempha kuti ndiwonongeke?
21 Tsopano munthu sangathe kuyangʼana dzuwa,
ndi kunyezimira mlengalenga,
kuwomba kwa mphepo kutachotsa mitambo yonse.
22 Kuwala kwake kumaonekera cha kumpoto;
Mulungu amabwera ndi ulemerero woopsa.
23 Wamphamvuzonse sitingathe kumufikira pafupi ndi wa mphamvu zoposa;
pa chiweruzo chake cholungama ndi mʼchilungamo chake chachikulu Iye sapondereza anthu ozunzika.
24 Nʼchifukwa chake anthu amamuopa kwambiri,
kodi saganizira za onse amene amaganiza kuti ndi anzeru?”
Job 37
New International Version
37 “At this my heart pounds(A)
and leaps from its place.
2 Listen!(B) Listen to the roar of his voice,(C)
to the rumbling that comes from his mouth.(D)
3 He unleashes his lightning(E) beneath the whole heaven
and sends it to the ends of the earth.(F)
4 After that comes the sound of his roar;
he thunders(G) with his majestic voice.(H)
When his voice resounds,
he holds nothing back.
5 God’s voice thunders(I) in marvelous ways;(J)
he does great things beyond our understanding.(K)
6 He says to the snow,(L) ‘Fall on the earth,’
and to the rain shower, ‘Be a mighty downpour.’(M)
7 So that everyone he has made may know his work,(N)
he stops all people from their labor.[a](O)
8 The animals take cover;(P)
they remain in their dens.(Q)
9 The tempest comes out from its chamber,(R)
the cold from the driving winds.(S)
10 The breath of God produces ice,
and the broad waters become frozen.(T)
11 He loads the clouds with moisture;(U)
he scatters his lightning(V) through them.(W)
12 At his direction they swirl around
over the face of the whole earth
to do whatever he commands them.(X)
13 He brings the clouds to punish people,(Y)
or to water his earth and show his love.(Z)
14 “Listen(AA) to this, Job;
stop and consider God’s wonders.(AB)
15 Do you know how God controls the clouds
and makes his lightning(AC) flash?(AD)
16 Do you know how the clouds hang poised,(AE)
those wonders of him who has perfect knowledge?(AF)
17 You who swelter in your clothes
when the land lies hushed under the south wind,(AG)
18 can you join him in spreading out the skies,(AH)
hard as a mirror of cast bronze?(AI)
19 “Tell us what we should say to him;(AJ)
we cannot draw up our case(AK) because of our darkness.(AL)
20 Should he be told that I want to speak?
Would anyone ask to be swallowed up?
21 Now no one can look at the sun,(AM)
bright as it is in the skies
after the wind has swept them clean.
22 Out of the north he comes in golden splendor;(AN)
God comes in awesome majesty.(AO)
23 The Almighty is beyond our reach and exalted in power;(AP)
in his justice(AQ) and great righteousness, he does not oppress.(AR)
24 Therefore, people revere him,(AS)
for does he not have regard for all the wise(AT) in heart?[b]”
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.