Add parallel Print Page Options

Mawu a Elihu

32 Tsono anthu atatuwa analeka kumuyankha Yobu, chifukwa chakuti iyeyo ankadziona kuti ndi wolungama. Koma Elihu, mwana wa Barakeli, wa fuko la Buzi, wa banja la Ramu, anapsera mtima kwambiri Yobu chifukwa choti Yobuyo anakana kuvomera kuti anachimwa ndi kuti Mulungu anakhoza pomulanga. Anapseranso mtima abwenzi ake atatu aja chifukwa sanapeze njira yomutsutsira Yobu, ngakhale iwo anamupeza kuti anali wolakwa. Tsono Elihu anadikira kuti ayankhule ndi Yobu chifukwa choti abwenziwo anali akuluakulu kupambana iyeyo. Koma Elihu ataona kuti anthu atatuwo analibe mawu oti ayankhulenso, iye anapsa mtima.

Choncho Elihu mwana wa Barakeli wa fuko la Buzi anati:

“Ine ndine wamngʼono,
    inuyo ndinu akuluakulu,
nʼchifukwa chake ndimaopa,
    ndimachita mantha kuti ndikuwuzeni zimene ndimadziwa.
Ndimaganiza kuti, ‘Ayambe ndi akuluakulu kuyankhula;
    anthu amvulazakale ndiwo amaphunzitsa nzeru.’
Koma mzimu wa Mulungu mwa munthu,
    mpweya wa Wamphamvuzonse, ndi umene umapereka nzeru zomvetsa zinthu.
Si okalamba amene ali ndi nzeru,
    si amvulazakale okha amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu zimene zili zoyenera.

10 “Nʼchifukwa chake ndikuti, ‘Mvereni;
    inenso ndikukuwuzani zimene ndikuzidziwa.’
11 Ndadikira nthawi yonseyi,
    ndimamvetsera mwachidwi zimene mumayankhula,
pamene mumafunafuna mawu oti muyankhule,
12     ineyo ndinakumvetseranidi.
Koma palibe ndi mmodzi yemwe wa inu amene anatsutsa Yobu;
    palibe aliyense wa inu amene anamuyankha mawu ake.
13 Musanene kuti, ‘Ife tapeza nzeru;
    Mulungu ndiye amutsutse, osati munthu.’
14 Koma Yobu sanayankhule motsutsana ndi ine,
    ndipo ine sindimuyankha monga mmene inu mwamuyankhira.

15 “Iwo asokonezeka ndipo alibe choti ayankhulenso;
    mawu awathera.
16 Kodi ine ndidikire chifukwa iwo sakuyankhula tsopano,
    pakuti angoyima phee wopanda yankho?
17 Inenso ndiyankhulapo tsopano;
    nanenso ndinena zimene ndikudziwa.
18 Pakuti ndili nawo mawu ambiri,
    ndipo mtima wanga ukundikakamiza;
19 mʼkati mwanga ndili ngati botolo lodzaza ndi vinyo,
    ngati matumba a vinyo watsopano amene ali pafupi kuphulika.
20 Ndiyenera kuyankhula kuti mtima utsike;
    ndiyenera kutsekula pakamwa panga ndi kuyankha.
21 Sindidzakondera munthu wina aliyense,
    kapena kuyankhula zoshashalika,
22 pakuti ndikanakhala wa luso loyankhula moshashalika,
    Mlengi wanga akanandilanga msanga.”

Elihu

32 So these three men stopped answering Job,(A) because he was righteous in his own eyes.(B) But Elihu son of Barakel the Buzite,(C) of the family of Ram, became very angry with Job for justifying himself(D) rather than God.(E) He was also angry with the three friends,(F) because they had found no way to refute Job,(G) and yet had condemned him.[a](H) Now Elihu had waited before speaking to Job because they were older than he.(I) But when he saw that the three men had nothing more to say, his anger was aroused.

So Elihu son of Barakel the Buzite said:

“I am young in years,
    and you are old;(J)
that is why I was fearful,
    not daring to tell you what I know.
I thought, ‘Age should speak;
    advanced years should teach wisdom.’(K)
But it is the spirit[b](L) in a person,
    the breath of the Almighty,(M) that gives them understanding.(N)
It is not only the old[c] who are wise,(O)
    not only the aged(P) who understand what is right.(Q)

10 “Therefore I say: Listen to me;(R)
    I too will tell you what I know.(S)
11 I waited while you spoke,
    I listened to your reasoning;
while you were searching for words,
12     I gave you my full attention.
But not one of you has proved Job wrong;
    none of you has answered his arguments.(T)
13 Do not say, ‘We have found wisdom;(U)
    let God, not a man, refute(V) him.’
14 But Job has not marshaled his words against me,(W)
    and I will not answer him with your arguments.

15 “They are dismayed and have no more to say;
    words have failed them.(X)
16 Must I wait, now that they are silent,
    now that they stand there with no reply?
17 I too will have my say;
    I too will tell what I know.(Y)
18 For I am full of words,
    and the spirit(Z) within me compels me;(AA)
19 inside I am like bottled-up wine,
    like new wineskins ready to burst.(AB)
20 I must speak and find relief;
    I must open my lips and reply.(AC)
21 I will show no partiality,(AD)
    nor will I flatter anyone;(AE)
22 for if I were skilled in flattery,
    my Maker(AF) would soon take me away.(AG)

Footnotes

  1. Job 32:3 Masoretic Text; an ancient Hebrew scribal tradition Job, and so had condemned God
  2. Job 32:8 Or Spirit; also in verse 18
  3. Job 32:9 Or many; or great