Add parallel Print Page Options

30 “Koma tsopano akundinyoza,
    ana angʼonoangʼono kwa ine,
anthu amene makolo awo sindikanawalola
    kuti azithandizana ndi agalu anga kuweta nkhosa zanga.
Kodi mphamvu zawo ndi za phindu lanji kwa ine,
    pakuti mphamvu zawo zinatha kale?
Anali atatheratu kuwonda ndi njala,
    ankayendayenda mʼdziko lopanda madzi,
    mʼchipululu usiku.
Ankathyola therere ndi masamba owawa,
    ndipo chakudya chawo chinali mizu ya mitengo ya masache.
Anapirikitsidwa pakati pa anthu anzawo,
    akuwakuwiza ngati kuti anali akuba.
Anawumirizidwa kukhala ku zigwembe za mitsinje yowuma,
    pakati pa matanthwe ndi mʼmaenje a mʼnthaka.
Ankalira ngati nyama kuthengo
    ndipo ankawunjikana pamodzi pa ziyangoyango.
Anali anthu achabechabe ndi wopanda dzina,
    anathamangitsidwa mʼdziko.

“Ndipo tsopano ana awo akundiyimba nyimbo zachipongwe;
    ineyo ndasanduka chisudzo chawo.
10 Iwo amanyansidwa nane ndipo amandithawa;
    akandiona salephera kundilavulira mʼmaso mwangamu.
11 Tsopano pakuti Mulungu wakhwefula uta wanga ndipo wandisautsa,
    iwowo analekeratu kundiopa.
12 Ku dzanja langa lamanja anthu akulimbana nane;
    andikumbira dzenje loti ndigweremo ndikamayenda,
    andipangira mitumbira ya nkhondo kuti alimbane nane.
13 Iwo anditsekera njira;
    akufuna kundichititsa ngozi,
    popanda wina aliyense wowaletsa.
14 Akundithamangitsa ngati madzi olowera pa mpanda wobowoka,
    iwo akubwererabwerera pakati pa chipasupasu.
15 Zoopsa zandithetsa mphamvu;
    ulemu wanga wachita ngati wauluzika ndi mphepo,
    chuma changa chija chazimirira ngati mtambo.

16 “Ndipo tsopano mtima wanga wachokamo;
    ndili mʼmasiku amasautso.
17 Mafupa anga akuphwanya usiku pakuti
    zowawa zanga sizikuleka.
18 Mʼmphamvu zake Mulungu wakhala ngati chovala changa;
    Iye wandigwira ngati chovala chondithina pa khosi.
19 Wandiponya mʼmatope,
    ndipo ndasanduka ngati fumbi ndi phulusa.

20 “Inu Mulungu, ine ndikulirira kwa Inu, koma simukundiyankha;
    ndikayimirira, Inu simundiyangʼana nʼkomwe.
21 Inuyo mumandichitira zankhanza;
    mumandizunza ndi dzanja lanu lamphamvu.
22 Mwandinyamulira ku mphepo ndipo mwandiwulutsa ndi mphepoyo;
    mwandiponya mʼmphepo ya mkuntho.
23 Ndikudziwa kuti Inu mudzandifikitsa ku imfa,
    kumalo kumene amoyo onse adzapitako.

24 “Ndithudi palibe munthu amene amalanga munthu wosweka mtima,
    amene akupempha thandizo mʼmasautso ake.
25 Kodi ine sindinalire nawo iwo amene anali pamavuto?
    Kodi mtima wanga sunamvere chisoni anthu osauka?
26 Koma pamene ndinkayembekezera zabwino, zoyipa ndiye zinandigwera;
    pamene ndinkafunafuna kuwala, mdima ndiye unandigwera.
27 Kuwawa kwa mʼkati mwanga sikukuleka;
    ndili mʼmasiku amasautso.
28 Ndikuyenda wothimbirira, komatu osati ndi dzuwa;
    ndimayimirira pa msonkhano ndi kupempha chithandizo molira.
29 Ndasanduka mʼbale wa nkhandwe,
    mnzawo wa akadzidzi.
30 Khungu langa layamba kuda ndipo likufunduka;
    thupi langa likutentha chifukwa cha kuphwanya kwa thupi.
31 Pangwe wanga wasanduka woyimbira maliro,
    ndipo chitoliro changa chikuyimbira anthu olira.

30 “But now they mock me,(A)
    men younger than I,
whose fathers I would have disdained
    to put with my sheep dogs.(B)
Of what use was the strength of their hands to me,
    since their vigor had gone from them?
Haggard from want and hunger,
    they roamed[a] the parched land(C)
    in desolate wastelands(D) at night.(E)
In the brush they gathered salt herbs,(F)
    and their food[b] was the root of the broom bush.(G)
They were banished from human society,
    shouted at as if they were thieves.
They were forced to live in the dry stream beds,
    among the rocks and in holes in the ground.(H)
They brayed(I) among the bushes(J)
    and huddled in the undergrowth.
A base and nameless brood,(K)
    they were driven out of the land.(L)

“And now those young men mock me(M) in song;(N)
    I have become a byword(O) among them.
10 They detest me(P) and keep their distance;
    they do not hesitate to spit in my face.(Q)
11 Now that God has unstrung my bow(R) and afflicted me,(S)
    they throw off restraint(T) in my presence.
12 On my right(U) the tribe[c] attacks;
    they lay snares(V) for my feet,(W)
    they build their siege ramps against me.(X)
13 They break up my road;(Y)
    they succeed in destroying me.(Z)
    ‘No one can help him,’ they say.
14 They advance as through a gaping breach;(AA)
    amid the ruins they come rolling in.
15 Terrors(AB) overwhelm me;(AC)
    my dignity is driven away as by the wind,
    my safety vanishes like a cloud.(AD)

16 “And now my life ebbs away;(AE)
    days of suffering grip me.(AF)
17 Night pierces my bones;
    my gnawing pains never rest.(AG)
18 In his great power(AH) God becomes like clothing to me[d];
    he binds me like the neck of my garment.
19 He throws me into the mud,(AI)
    and I am reduced to dust and ashes.(AJ)

20 “I cry out to you,(AK) God, but you do not answer;(AL)
    I stand up, but you merely look at me.
21 You turn on me ruthlessly;(AM)
    with the might of your hand(AN) you attack me.(AO)
22 You snatch me up and drive me before the wind;(AP)
    you toss me about in the storm.(AQ)
23 I know you will bring me down to death,(AR)
    to the place appointed for all the living.(AS)

24 “Surely no one lays a hand on a broken man(AT)
    when he cries for help in his distress.(AU)
25 Have I not wept for those in trouble?(AV)
    Has not my soul grieved for the poor?(AW)
26 Yet when I hoped for good, evil came;
    when I looked for light, then came darkness.(AX)
27 The churning inside me never stops;(AY)
    days of suffering confront me.(AZ)
28 I go about blackened,(BA) but not by the sun;
    I stand up in the assembly and cry for help.(BB)
29 I have become a brother of jackals,(BC)
    a companion of owls.(BD)
30 My skin grows black(BE) and peels;(BF)
    my body burns with fever.(BG)
31 My lyre is tuned to mourning,(BH)
    and my pipe(BI) to the sound of wailing.

Footnotes

  1. Job 30:3 Or gnawed
  2. Job 30:4 Or fuel
  3. Job 30:12 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  4. Job 30:18 Hebrew; Septuagint power he grasps my clothing