Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

Pambuyo pake Yobu anatsekula pakamwa pake nayamba kutemberera tsiku limene iyeyo anabadwa. Ndipo Yobu anati:

“Tsiku limene ine ndinabadwa litembereredwe
    ndi usiku umene ananena kuti, ‘Mwana wamwamuna wabadwa!’
Tsiku limenelo lisanduke mdima;
    Mulungu wa kumwambako asalilabadirenso;
    kuwala kusaonekenso pa tsikulo.
Mdima ndi mthunzi wa imfa zikhale pa tsiku limeneli;
    mtambo uphimbe tsikuli;
    mdima wandiweyani udetse kuwala kwake.
Usiku umenewo ukutidwe ndi mdima wandiweyani;
    usawerengedwenso pamodzi ndi masiku a chaka,
    kapena kukhala pa mwezi wina uliwonse.
Usiku umenewo usabweretse chilichonse chabwino;
    kusamvekenso nthungululu za chikondwerero.
Odziwa kutemberera masiku alitemberere tsikulo,
    iwo amene akonzekera kuwutsa Leviyatani.
Nyenyezi zake za mʼbandakucha zikhale mdima;
    tsikulo liyembekezere kucha pachabe
    ndipo lisaonenso kuwala koyamba kwa mʼbandakucha.
10 Pakuti tsiku limenelo ndiye ndinatuluka mʼmimba ya amayi anga
    ndipo ndi limene linandionetsa zovuta.

11 “Bwanji ine sindinawonongeke pamene ndinkabadwa
    ndi kufa pamene ndimatuluka mʼmimba?
12 Chifukwa chiyani panali mawondo wondilandirirapo
    ndi mawere woti andiyamwitsepo?
13 Pakuti tsopano bwenzi ndili gone mwamtendere;
    ndikanakhala nditagona tulo ndili pa mpumulo
14 pamodzi ndi mafumu ndi aphungu a dziko lapansi,
    amene anadzimangira nyumba zikuluzikulu zimene tsopano ndi mabwinja,
15 pamodzi ndi olamulira amene anali ndi golide,
    amene anadzaza nyumba zawo ndi siliva.
16 Kapena, bwanji sindinakwiriridwe pansi monga mwana wobadwa wakufa kale,
    ngati khanda limene silinaone kuwala kwa dzuwa?
17 Ku mandako anthu oyipa sakhalanso pa mavuto,
    ndipo kumeneko anthu otopa ali pa mpumulo.
18 A mʼndende kumeneko akusangalala ndi mtendere;
    sakumvanso mawu ofuwula a kapitawo wa akapolo.
19 Anthu wamba ndi anthu apamwamba ali kumeneko,
    ndipo kapolo ndi womasuka kwa mbuye wake.

20 “Chifukwa chiyani dzuwa limawalira iwo amene ali pa mavuto,
    ndipo moyo umapatsidwa kwa owawidwa mtima,
21 kwa iwo amene amalakalaka imfa imene sibwera,
    amene amayifunafuna imfayo kupambana chuma chobisika,
22 amene amakondwa ndi kusangalala
    akamalowa mʼmanda?
23 Chifuwa chiyani moyo umaperekedwa kwa munthu
    amene njira yake yabisika,
    amene Mulungu wamuzinga ponseponse?
24 Mʼmalo moti ndidye, ndimalira,
    ndi kubuwula kwanga nʼkosalekeza.
25 Chimene ndinkachiopa chandigwera;
    chimene ndinkachita nacho mantha chandichitikira.
26 Ndilibe mtendere kapena bata,
    ndilibe mpumulo, koma mavuto okhaokha.”

Job Speaks

After this, Job opened his mouth and cursed the day of his birth.(A) He said:

“May the day of my birth perish,
    and the night that said, ‘A boy is conceived!’(B)
That day—may it turn to darkness;
    may God above not care about it;
    may no light shine on it.
May gloom and utter darkness(C) claim it once more;
    may a cloud settle over it;
    may blackness overwhelm it.
That night—may thick darkness(D) seize it;
    may it not be included among the days of the year
    nor be entered in any of the months.
May that night be barren;
    may no shout of joy(E) be heard in it.
May those who curse days[a] curse that day,(F)
    those who are ready to rouse Leviathan.(G)
May its morning stars become dark;
    may it wait for daylight in vain
    and not see the first rays of dawn,(H)
10 for it did not shut the doors of the womb on me
    to hide trouble from my eyes.

11 “Why did I not perish at birth,
    and die as I came from the womb?(I)
12 Why were there knees to receive me(J)
    and breasts that I might be nursed?
13 For now I would be lying down(K) in peace;
    I would be asleep and at rest(L)
14 with kings and rulers of the earth,(M)
    who built for themselves places now lying in ruins,(N)
15 with princes(O) who had gold,
    who filled their houses with silver.(P)
16 Or why was I not hidden away in the ground like a stillborn child,(Q)
    like an infant who never saw the light of day?(R)
17 There the wicked cease from turmoil,(S)
    and there the weary are at rest.(T)
18 Captives(U) also enjoy their ease;
    they no longer hear the slave driver’s(V) shout.(W)
19 The small and the great are there,(X)
    and the slaves are freed from their owners.

20 “Why is light given to those in misery,
    and life to the bitter of soul,(Y)
21 to those who long for death that does not come,(Z)
    who search for it more than for hidden treasure,(AA)
22 who are filled with gladness
    and rejoice when they reach the grave?(AB)
23 Why is life given to a man
    whose way is hidden,(AC)
    whom God has hedged in?(AD)
24 For sighing(AE) has become my daily food;(AF)
    my groans(AG) pour out like water.(AH)
25 What I feared has come upon me;
    what I dreaded(AI) has happened to me.(AJ)
26 I have no peace,(AK) no quietness;
    I have no rest,(AL) but only turmoil.”(AM)

Footnotes

  1. Job 3:8 Or curse the sea