Add parallel Print Page Options

29 Yobu anapitiriza kuyankhula kwake:

“Aa! Ndikanakhala momwe ndinalili miyezi yapitayi,
    masiku amene Mulungu ankandiyangʼanira,
pamene nyale yake inkandiwunikira
    ndipo ndi kuwunika kwakeko ine ndinkatha kuyenda mu mdima!
Ndithu, masiku amene ndinali pabwino kwambiri,
    pamene ubwenzi wa Mulungu unkabweretsa madalitso pa nyumba yanga,
nthawi imene Wamphamvuzonse anali nane,
    ndipo ana anga anali atandizungulira mʼmbalimu,
pamene popondapo ine panali patakhathamira mafuta a mkaka,
    ndipo pa thanthwe pamatuluka mitsinje ya mafuta a olivi.

“Pamene ndinkapita pa chipata cha mzinda
    ndi kukhala pa mpando wanga pabwalo,
anyamata amati akandiona ankapatuka
    ndipo anthu akuluakulu ankayimirira;
atsogoleri ankakhala chete
    ndipo ankagwira pakamwa pawo;
10 anthu otchuka ankangoti duu,
    ndipo malilime awo anali atamatirira ku nkhama zawo.
11 Aliyense amene anamva za ine anayankhula zabwino zanga,
    ndipo iwo amene anandiona ankandiyamikira,
12 chifukwa ndinkapulumutsa mʼmphawi wofuna chithandizo,
    ndiponso mwana wamasiye amene analibe aliyense womuthandiza.
13 Munthu amene anali pafupi kufa ankandidalitsa;
    ndinkasangalatsanso mkazi wamasiye.
14 Chilungamo chinali ngati chovala changa;
    chiweruzo cholungama ndiye chinali mkanjo ndi nduwira yanga.
15 Ndinali ngati maso kwa anthu osapenya;
    ndinali ngati mapazi kwa anthu olumala.
16 Ndinali ngati abambo kwa anthu aumphawi;
    ndinkayimira mlendo pa mlandu wake.
17 Ndinkawononga mphamvu za anthu oyipa
    ndi kulanditsa amene anali atagwidwa.

18 “Ndinkaganiza kuti, ‘Ndidzafera mʼnyumba yanga,
    masiku a moyo wanga ali ochuluka ngati mchenga.
19 Mizu yanga idzatambalalira ku madzi,
    ndipo mame adzakhala pa nthambi zanga usiku wonse.
20 Ulemerero wanga udzakhala wosaguga mwa ine,
    ndipo uta wanga udzakhala watsopano nthawi zonse mʼdzanja langa.’

21 “Anthu ankamvetsera zimene ndinkanena mwachidwi,
    ankadikira atakhala chete kuti amve malangizo anga.
22 Ndikayankhula, iwo sankayankhulanso;
    mawu anga ankawagwira mtima.
23 Ankayembekezera ine monga momwe amayembekezera mvula
    ndipo ankalandira mawu anga ngati mvula ya mʼmalimwe.
24 Ndikawasekerera, iwo sankatha kukhulupirira;
    kuwala kwa nkhope yanga chinali chinthu chamtengowapatali kwa iwowo.
25 Ndinkawasankhira njira yawo ndipo ndinkawatsogolera ngati mfumu;
    ndinkakhala ngati mfumu pakati pa gulu lake lankhondo;
    ndinali ngati msangalatsi pakati pa anthu olira.”

Job’s Final Defense

29 Job continued his discourse:(A)

“How I long for the months gone by,(B)
    for the days when God watched over me,(C)
when his lamp shone on my head
    and by his light I walked through darkness!(D)
Oh, for the days when I was in my prime,
    when God’s intimate friendship(E) blessed my house,(F)
when the Almighty was still with me
    and my children(G) were around me,(H)
when my path was drenched with cream(I)
    and the rock(J) poured out for me streams of olive oil.(K)

“When I went to the gate(L) of the city
    and took my seat in the public square,
the young men saw me and stepped aside(M)
    and the old men rose to their feet;(N)
the chief men refrained from speaking(O)
    and covered their mouths with their hands;(P)
10 the voices of the nobles were hushed,(Q)
    and their tongues stuck to the roof of their mouths.(R)
11 Whoever heard me spoke well of me,
    and those who saw me commended me,(S)
12 because I rescued the poor(T) who cried for help,
    and the fatherless(U) who had none to assist them.(V)
13 The one who was dying blessed me;(W)
    I made the widow’s(X) heart sing.
14 I put on righteousness(Y) as my clothing;
    justice was my robe and my turban.(Z)
15 I was eyes(AA) to the blind
    and feet to the lame.(AB)
16 I was a father to the needy;(AC)
    I took up the case(AD) of the stranger.(AE)
17 I broke the fangs of the wicked
    and snatched the victims(AF) from their teeth.(AG)

18 “I thought, ‘I will die in my own house,
    my days as numerous as the grains of sand.(AH)
19 My roots will reach to the water,(AI)
    and the dew will lie all night on my branches.(AJ)
20 My glory will not fade;(AK)
    the bow(AL) will be ever new in my hand.’(AM)

21 “People listened to me expectantly,
    waiting in silence for my counsel.(AN)
22 After I had spoken, they spoke no more;(AO)
    my words fell gently on their ears.(AP)
23 They waited for me as for showers
    and drank in my words as the spring rain.(AQ)
24 When I smiled at them, they scarcely believed it;
    the light of my face(AR) was precious to them.[a](AS)
25 I chose the way for them and sat as their chief;(AT)
    I dwelt as a king(AU) among his troops;
    I was like one who comforts mourners.(AV)

Footnotes

  1. Job 29:24 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.