Add parallel Print Page Options

Mawu a Elifazi

22 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?
    Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?
    Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?

“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,
    kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?
    Kodi machimo ako si opanda malire?
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;
    umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Sunawapatse madzi anthu otopa,
    ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,
    munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,
    ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,
    nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,
    nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.

12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?
    Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?
    Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona
    pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale
    imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,
    maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!
    Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,
    choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.

19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;
    anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka
    ndipo moto wawononga chuma chawo!’

21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;
    ukatero udzaona zabwino.
22 Landira malangizo a pakamwa pake
    ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;
    ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,
    golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,
    siliva wako wamtengowapatali.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse
    ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera,
    ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,
    kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’
    Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,
    ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

Eliphaz

22 Then Eliphaz the Temanite(A) replied:

“Can a man be of benefit to God?(B)
    Can even a wise person benefit him?(C)
What pleasure(D) would it give the Almighty if you were righteous?(E)
    What would he gain if your ways were blameless?(F)

“Is it for your piety that he rebukes you
    and brings charges against you?(G)
Is not your wickedness great?
    Are not your sins(H) endless?(I)
You demanded security(J) from your relatives for no reason;(K)
    you stripped people of their clothing, leaving them naked.(L)
You gave no water(M) to the weary
    and you withheld food from the hungry,(N)
though you were a powerful man, owning land(O)
    an honored man,(P) living on it.(Q)
And you sent widows(R) away empty-handed(S)
    and broke the strength of the fatherless.(T)
10 That is why snares(U) are all around you,(V)
    why sudden peril terrifies you,(W)
11 why it is so dark(X) you cannot see,
    and why a flood of water covers you.(Y)

12 “Is not God in the heights of heaven?(Z)
    And see how lofty are the highest stars!
13 Yet you say, ‘What does God know?(AA)
    Does he judge through such darkness?(AB)
14 Thick clouds(AC) veil him, so he does not see us(AD)
    as he goes about in the vaulted heavens.’(AE)
15 Will you keep to the old path
    that the wicked(AF) have trod?(AG)
16 They were carried off before their time,(AH)
    their foundations(AI) washed away by a flood.(AJ)
17 They said to God, ‘Leave us alone!
    What can the Almighty do to us?’(AK)
18 Yet it was he who filled their houses with good things,(AL)
    so I stand aloof from the plans of the wicked.(AM)
19 The righteous see their ruin and rejoice;(AN)
    the innocent mock(AO) them, saying,
20 ‘Surely our foes are destroyed,(AP)
    and fire(AQ) devours their wealth.’

21 “Submit to God and be at peace(AR) with him;(AS)
    in this way prosperity will come to you.(AT)
22 Accept instruction from his mouth(AU)
    and lay up his words(AV) in your heart.(AW)
23 If you return(AX) to the Almighty, you will be restored:(AY)
    If you remove wickedness far from your tent(AZ)
24 and assign your nuggets(BA) to the dust,
    your gold(BB) of Ophir(BC) to the rocks in the ravines,(BD)
25 then the Almighty will be your gold,(BE)
    the choicest silver for you.(BF)
26 Surely then you will find delight in the Almighty(BG)
    and will lift up your face(BH) to God.(BI)
27 You will pray to him,(BJ) and he will hear you,(BK)
    and you will fulfill your vows.(BL)
28 What you decide on will be done,(BM)
    and light(BN) will shine on your ways.(BO)
29 When people are brought low(BP) and you say, ‘Lift them up!’
    then he will save the downcast.(BQ)
30 He will deliver even one who is not innocent,(BR)
    who will be delivered through the cleanness of your hands.”(BS)