Add parallel Print Page Options

Mawu a Elifazi

22 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,

“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu?
    Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama?
    Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?

“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula,
    kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu?
    Kodi machimo ako si opanda malire?
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa;
    umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
Sunawapatse madzi anthu otopa,
    ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake,
    munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu,
    ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira,
    nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu,
    nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.

12 “Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba?
    Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani?
    Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona
    pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale
    imene anthu oyipa ankayendamo?
16 Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane,
    maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni!
    Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino,
    choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.

19 “Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera;
    anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka
    ndipo moto wawononga chuma chawo!’

21 “Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere;
    ukatero udzaona zabwino.
22 Landira malangizo a pakamwa pake
    ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa;
    ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi,
    golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako,
    siliva wako wamtengowapatali.
26 Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse
    ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Udzamupempha ndipo adzakumvera,
    ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi,
    kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’
    Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa,
    ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”

22 Then Eliphaz the Temanite answered and said,

Can a man be profitable unto God, as he that is wise may be profitable unto himself?

Is it any pleasure to the Almighty, that thou art righteous? or is it gain to him, that thou makest thy ways perfect?

Will he reprove thee for fear of thee? will he enter with thee into judgment?

Is not thy wickedness great? and thine iniquities infinite?

For thou hast taken a pledge from thy brother for nought, and stripped the naked of their clothing.

Thou hast not given water to the weary to drink, and thou hast withholden bread from the hungry.

But as for the mighty man, he had the earth; and the honourable man dwelt in it.

Thou hast sent widows away empty, and the arms of the fatherless have been broken.

10 Therefore snares are round about thee, and sudden fear troubleth thee;

11 Or darkness, that thou canst not see; and abundance of waters cover thee.

12 Is not God in the height of heaven? and behold the height of the stars, how high they are!

13 And thou sayest, How doth God know? can he judge through the dark cloud?

14 Thick clouds are a covering to him, that he seeth not; and he walketh in the circuit of heaven.

15 Hast thou marked the old way which wicked men have trodden?

16 Which were cut down out of time, whose foundation was overflown with a flood:

17 Which said unto God, Depart from us: and what can the Almighty do for them?

18 Yet he filled their houses with good things: but the counsel of the wicked is far from me.

19 The righteous see it, and are glad: and the innocent laugh them to scorn.

20 Whereas our substance is not cut down, but the remnant of them the fire consumeth.

21 Acquaint now thyself with him, and be at peace: thereby good shall come unto thee.

22 Receive, I pray thee, the law from his mouth, and lay up his words in thine heart.

23 If thou return to the Almighty, thou shalt be built up, thou shalt put away iniquity far from thy tabernacles.

24 Then shalt thou lay up gold as dust, and the gold of Ophir as the stones of the brooks.

25 Yea, the Almighty shall be thy defence, and thou shalt have plenty of silver.

26 For then shalt thou have thy delight in the Almighty, and shalt lift up thy face unto God.

27 Thou shalt make thy prayer unto him, and he shall hear thee, and thou shalt pay thy vows.

28 Thou shalt also decree a thing, and it shall be established unto thee: and the light shall shine upon thy ways.

29 When men are cast down, then thou shalt say, There is lifting up; and he shall save the humble person.

30 He shall deliver the island of the innocent: and it is delivered by the pureness of thine hands.