Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

21 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Mvetserani bwino mawu anga;
    ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Ndiloleni ndiyankhule
    ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.

“Kodi ine ndikudandaulira munthu?
    Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Ndipenyeni ndipo mudabwe;
    mugwire dzanja pakamwa.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri;
    thupi langa limanjenjemera.
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo,
    amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo,
    zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha;
    mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa;
    ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa;
    makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze;
    amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero
    ndipo amatsikira ku manda mwamtendere.
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’
    Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire?
    Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo,
    koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.

17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa?
    Nʼkangati kamene tsoka limawagwera?
    Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo,
    ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’
    Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake,
    kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo,
    pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?

22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru,
    poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse,
    ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 thupi lake lili lonenepa,
    mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima,
    wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda
    ndipo onse amatuluka mphutsi.

27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,
    ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti,
    matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo?
    Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka,
    kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo?
    Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda
    ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera;
    anthu onse amatsatira mtembo wake,
    ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.

34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo
    palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

Job

21 Then Job replied:

“Listen carefully to my words;(A)
    let this be the consolation you give me.(B)
Bear with me while I speak,
    and after I have spoken, mock on.(C)

“Is my complaint(D) directed to a human being?
    Why should I not be impatient?(E)
Look at me and be appalled;
    clap your hand over your mouth.(F)
When I think about this, I am terrified;(G)
    trembling seizes my body.(H)
Why do the wicked live on,
    growing old and increasing in power?(I)
They see their children established around them,
    their offspring before their eyes.(J)
Their homes are safe and free from fear;(K)
    the rod of God is not on them.(L)
10 Their bulls never fail to breed;
    their cows calve and do not miscarry.(M)
11 They send forth their children as a flock;(N)
    their little ones dance about.
12 They sing to the music of timbrel and lyre;(O)
    they make merry to the sound of the pipe.(P)
13 They spend their years in prosperity(Q)
    and go down to the grave(R) in peace.[a](S)
14 Yet they say to God, ‘Leave us alone!(T)
    We have no desire to know your ways.(U)
15 Who is the Almighty, that we should serve him?
    What would we gain by praying to him?’(V)
16 But their prosperity is not in their own hands,
    so I stand aloof from the plans of the wicked.(W)

17 “Yet how often is the lamp of the wicked snuffed out?(X)
    How often does calamity(Y) come upon them,
    the fate God allots in his anger?(Z)
18 How often are they like straw before the wind,
    like chaff(AA) swept away(AB) by a gale?(AC)
19 It is said, ‘God stores up the punishment of the wicked for their children.’(AD)
    Let him repay the wicked, so that they themselves will experience it!(AE)
20 Let their own eyes see their destruction;(AF)
    let them drink(AG) the cup of the wrath of the Almighty.(AH)
21 For what do they care about the families they leave behind(AI)
    when their allotted months(AJ) come to an end?(AK)

22 “Can anyone teach knowledge to God,(AL)
    since he judges even the highest?(AM)
23 One person dies in full vigor,(AN)
    completely secure and at ease,(AO)
24 well nourished(AP) in body,[b]
    bones(AQ) rich with marrow.(AR)
25 Another dies in bitterness of soul,(AS)
    never having enjoyed anything good.
26 Side by side they lie in the dust,(AT)
    and worms(AU) cover them both.(AV)

27 “I know full well what you are thinking,
    the schemes by which you would wrong me.
28 You say, ‘Where now is the house of the great,(AW)
    the tents where the wicked lived?’(AX)
29 Have you never questioned those who travel?
    Have you paid no regard to their accounts—
30 that the wicked are spared from the day of calamity,(AY)
    that they are delivered from[c] the day of wrath?(AZ)
31 Who denounces their conduct to their face?
    Who repays them for what they have done?(BA)
32 They are carried to the grave,
    and watch is kept over their tombs.(BB)
33 The soil in the valley is sweet to them;(BC)
    everyone follows after them,
    and a countless throng goes[d] before them.(BD)

34 “So how can you console me(BE) with your nonsense?
    Nothing is left of your answers but falsehood!”(BF)

Footnotes

  1. Job 21:13 Or in an instant
  2. Job 21:24 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  3. Job 21:30 Or wicked are reserved for the day of calamity, / that they are brought forth to
  4. Job 21:33 Or them, / as a countless throng went