Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

21 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Mvetserani bwino mawu anga;
    ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
Ndiloleni ndiyankhule
    ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.

“Kodi ine ndikudandaulira munthu?
    Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
Ndipenyeni ndipo mudabwe;
    mugwire dzanja pakamwa.
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri;
    thupi langa limanjenjemera.
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo,
    amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo,
    zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha;
    mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa;
    ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa;
    makanda awo amavinavina pabwalo.
12 Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze;
    amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero
    ndipo amatsikira ku manda mwamtendere.
14 Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’
    Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire?
    Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo,
    koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.

17 “Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa?
    Nʼkangati kamene tsoka limawagwera?
    Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo,
    ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’
    Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 Mulole kuti adzionere yekha chilango chake,
    kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo,
    pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?

22 “Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru,
    poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse,
    ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 thupi lake lili lonenepa,
    mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima,
    wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda
    ndipo onse amatuluka mphutsi.

27 “Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza,
    ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti,
    matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo?
    Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka,
    kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo?
    Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Iye amanyamulidwa kupita ku manda
    ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Dothi la ku chigwa limamukomera;
    anthu onse amatsatira mtembo wake,
    ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.

34 “Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo
    palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”