Add parallel Print Page Options

Mawu a Yobu

19 Pamenepo Yobu anayankha kuti,

“Kodi mudzakhala mukundizunza mpaka liti,
    ndi kundilasa ndi mawu anuwo?
Inuyo mwandinyoza kwambiri;
    mwanditsutsa mopanda manyazi.
Ngati ndi zoona kuti ine ndasochera,
    cholakwachotu nʼchanga.
Ngati ndithudi mukudziyika nokha pamwamba panga,
    ndi kugwiritsa ntchito kunyozedwa kwanga polimbana nane,
pamenepa dziwani kuti Mulungu wandilakwira
    ndipo wandizinga ukonde wake.

“Ngakhale ndifuwule kuti, ‘Akundizunza!’ Palibe wondiyankha;
    ngakhale ndipemphe thandizo, palibe wondichitira zolungama.
Mulungu wanditsekera njira yanga kotero sindingathe kudutsa;
    waphimba njira zanga ndi mdima.
Iye wandilanda ulemu wanga
    ndipo wandivula chipewa chaufumu pamutu panga.
10 Wandiphwanyaphwanya mbali zonse ndipo ndatheratu;
    Iye wazula chiyembekezo changa ngati mtengo.
11 Wandikwiyira ndipo
    akundiyesa mmodzi mwa adani ake.
12 Ankhondo ake akubwera kwa ine mwamphamvu,
    akonzekera zodzalimbana nane
    ndipo azungulira nyumba yanga.

13 “Mulungu wandisiyanitsa ndi abale anga;
    wasandutsa odziwana nane kukhala achilendo kwa ine.
14 Abale anga andithawa;
    abwenzi anga andiyiwala.
15 Anthu odzacheza ku nyumba kwanga ndiponso antchito anga aakazi andisandutsa mlendo;
    ndasanduka mlendo mʼmaso mwawo.
16 Ndikayitana wa ntchito wanga, iye sandiyankha,
    ngakhale ndikapempha ndi pakamwa panga sandichitira kanthu.
17 Mpweya wanga umamunyansa mkazi wanga;
    ndine chinthu chonyansa kwa abale anga a mimba imodzi.
18 Inde, ngakhale ana amandinyoza;
    akandiona amandinyodola.
19 Anzanga onse apamtima amanyansidwa nane;
    iwo amene ndinkawakonda andiwukira.
20 Ndangotsala khungu ndi mafupa okhaokha;
    ndapulumuka lokumbakumba.

21 “Mvereni chisoni, inu abwenzi anga, mvereni chisoni,
    pakuti dzanja la Mulungu landikantha.
22 Chifukwa chiyani mukundilondola ngati Mulungu?
    Kodi simunatope nalo thupi langa?

23 “Aa, achikhala mawu anga analembedwa,
    achikhala analembedwa mʼbuku,
24 akanalembedwa pa mwala ndi chitsulo,
    akanalembedwa pa thanthwe kuti sangathe kufufutidwa!
25 Koma ndikudziwa kuti mpulumutsi wanga ali ndi moyo,
    ndipo pa nthawi yomaliza adzabwera kudzanditeteza.
26 Ndipo khungu langa litatha nʼkuwonongeka,
    mʼthupi langa lomweli ndidzamuona Mulungu.
27 Ine ndemwe ndidzamuona Iye
    ndi maso angawa, ineyo, osati wina ayi.
    Ndithu mtima wanga ukufunitsitsadi!

28 “Koma inu mukuti, ‘Haa! Tingamuzunze bwanji,
    popeza kuti zonsezi zaoneka chifukwa cha iye yemweyo?’
29 Inu muyenera kuopa lupanga;
    pakuti mkwiyo wake umalangadi ndi lupanga;
    zikadzatero muzadziwa kuti chiweruzo chilipo ndithu.”

Job

19 Then Job replied:

“How long will you torment(A) me
    and crush(B) me with words?
Ten times(C) now you have reproached(D) me;
    shamelessly you attack me.
If it is true that I have gone astray,
    my error(E) remains my concern alone.
If indeed you would exalt yourselves above me(F)
    and use my humiliation against me,
then know that God has wronged me(G)
    and drawn his net(H) around me.(I)

“Though I cry, ‘Violence!’ I get no response;(J)
    though I call for help,(K) there is no justice.(L)
He has blocked my way so I cannot pass;(M)
    he has shrouded my paths in darkness.(N)
He has stripped(O) me of my honor(P)
    and removed the crown from my head.(Q)
10 He tears me down(R) on every side till I am gone;
    he uproots my hope(S) like a tree.(T)
11 His anger(U) burns against me;
    he counts me among his enemies.(V)
12 His troops advance in force;(W)
    they build a siege ramp(X) against me
    and encamp around my tent.(Y)

13 “He has alienated my family(Z) from me;
    my acquaintances are completely estranged from me.(AA)
14 My relatives have gone away;
    my closest friends(AB) have forgotten me.
15 My guests(AC) and my female servants(AD) count me a foreigner;
    they look on me as on a stranger.
16 I summon my servant, but he does not answer,
    though I beg him with my own mouth.
17 My breath is offensive to my wife;
    I am loathsome(AE) to my own family.
18 Even the little boys(AF) scorn me;
    when I appear, they ridicule me.(AG)
19 All my intimate friends(AH) detest me;(AI)
    those I love have turned against me.(AJ)
20 I am nothing but skin and bones;(AK)
    I have escaped only by the skin of my teeth.[a]

21 “Have pity on me, my friends,(AL) have pity,
    for the hand of God has struck(AM) me.
22 Why do you pursue(AN) me as God does?(AO)
    Will you never get enough of my flesh?(AP)

23 “Oh, that my words were recorded,
    that they were written on a scroll,(AQ)
24 that they were inscribed with an iron tool(AR) on[b] lead,
    or engraved in rock forever!(AS)
25 I know that my redeemer[c](AT) lives,(AU)
    and that in the end he will stand on the earth.[d]
26 And after my skin has been destroyed,
    yet[e] in[f] my flesh I will see God;(AV)
27 I myself will see him
    with my own eyes(AW)—I, and not another.
    How my heart yearns(AX) within me!

28 “If you say, ‘How we will hound(AY) him,
    since the root of the trouble lies in him,[g]
29 you should fear the sword yourselves;
    for wrath will bring punishment by the sword,(AZ)
    and then you will know that there is judgment.[h](BA)

Footnotes

  1. Job 19:20 Or only by my gums
  2. Job 19:24 Or and
  3. Job 19:25 Or vindicator
  4. Job 19:25 Or on my grave
  5. Job 19:26 Or And after I awake, / though this body has been destroyed, / then
  6. Job 19:26 Or destroyed, / apart from
  7. Job 19:28 Many Hebrew manuscripts, Septuagint and Vulgate; most Hebrew manuscripts me
  8. Job 19:29 Or sword, / that you may come to know the Almighty