Add parallel Print Page Options

14 “Munthu wobadwa mwa amayi
    amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota;
    amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa?
    Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa?
    Palibe ndi mmodzi yemwe!
Masiku a munthu ndi odziwikiratu;
    munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake
    ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule
    kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.

“Mtengo uli nacho chiyembekezo:
    ngati wadulidwa, udzaphukiranso
    ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka
    ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira
    ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda,
    amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja
    kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso;
    mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka
    kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.

13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda
    ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita!
Achikhala munandiyikira nthawi,
    kuti pambuyo pake mundikumbukirenso.
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo?
    Masiku anga onse a moyo wovutikawu
    ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani;
    inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga
    koma simudzalondola tchimo langa.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba;
    inu mudzaphimba tchimo langa.

18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka
    ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala
    ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka,
    momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu;
    Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo;
    akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake
    ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”

14 “Mortals, born of woman,(A)
    are of few days(B) and full of trouble.(C)
They spring up like flowers(D) and wither away;(E)
    like fleeting shadows,(F) they do not endure.(G)
Do you fix your eye on them?(H)
    Will you bring them[a] before you for judgment?(I)
Who can bring what is pure(J) from the impure?(K)
    No one!(L)
A person’s days are determined;(M)
    you have decreed the number of his months(N)
    and have set limits he cannot exceed.(O)
So look away from him and let him alone,(P)
    till he has put in his time like a hired laborer.(Q)

“At least there is hope for a tree:(R)
    If it is cut down, it will sprout again,
    and its new shoots(S) will not fail.(T)
Its roots may grow old in the ground
    and its stump(U) die in the soil,
yet at the scent of water(V) it will bud
    and put forth shoots like a plant.(W)
10 But a man dies and is laid low;(X)
    he breathes his last and is no more.(Y)
11 As the water of a lake dries up
    or a riverbed becomes parched and dry,(Z)
12 so he lies down and does not rise;(AA)
    till the heavens are no more,(AB) people will not awake
    or be roused from their sleep.(AC)

13 “If only you would hide me in the grave(AD)
    and conceal me till your anger has passed!(AE)
If only you would set me a time
    and then remember(AF) me!(AG)
14 If someone dies, will they live again?
    All the days of my hard service(AH)
    I will wait for my renewal[b](AI) to come.
15 You will call and I will answer you;(AJ)
    you will long for the creature your hands have made.(AK)
16 Surely then you will count my steps(AL)
    but not keep track of my sin.(AM)
17 My offenses will be sealed(AN) up in a bag;(AO)
    you will cover over my sin.(AP)

18 “But as a mountain erodes and crumbles(AQ)
    and as a rock is moved from its place,(AR)
19 as water wears away stones
    and torrents(AS) wash away the soil,(AT)
    so you destroy a person’s hope.(AU)
20 You overpower them once for all, and they are gone;(AV)
    you change their countenance and send them away.(AW)
21 If their children are honored, they do not know it;
    if their offspring are brought low, they do not see it.(AX)
22 They feel but the pain of their own bodies(AY)
    and mourn only for themselves.(AZ)

Footnotes

  1. Job 14:3 Septuagint, Vulgate and Syriac; Hebrew me
  2. Job 14:14 Or release