Add parallel Print Page Options

Mawu a Zofari

11 Pamenepo Zofari wa ku Naama anayankha kuti,

“Kodi mawu ambirimbiriwa nʼkukhala osayankhidwa?
    Kodi munthu woyankhulayankhulayu nʼkulungamitsidwa?
Kodi anthu nʼkukhala chete atamva kubwebweta kwakoku?
    Kodi palibe wina amene adzakudzudzule pamene ukuyankhula zonyoza?
Iwe ukunena kwa Mulungu kuti, ‘Zikhulupiriro zanga ndi zopanda zolakwika
    ndipo ndine wangwiro pamaso panu.’
Aa, nʼkanakonda Mulungu akanayankhula
    kuti Iye atsekule pakamwa pake kutsutsana nawe
ndi kukuwululira chinsinsi cha nzeru yake,
    pakuti nzeru yeniyeni ili ndi mbali ziwiri.
    Dziwa izi: Mulungu wayiwala machimo ako ena.

“Kodi iwe ungathe kumvetsa zinsinsi za Mulungu?
    Kodi ungafufuze malire a nzeru za Wamphamvuzonse?
Zili kutali kupambana mayiko akumwamba, nanga ungachite chiyani?
    Ndi zakuya kupambana kuya kwa manda, nanga ungadziwe chiyani?
Muyeso wa nzeru zake ndi wautali kupambana dziko lapansi
    ndipo ndi wopingasa kupambana nyanja.

10 “Ngati Iye atabwera ndi kukutsekera mʼndende
    nakutengera ku bwalo la milandu, ndani angathe kumuletsa?
11 Ndithudi, Mulungu amazindikira anthu achinyengo;
    akaona choyipa, kodi sachizindikira?
12 Munthu wopanda nzeru sizingatheke kukhala wanzeru
    monganso mwana wa bulu wakuthengo sangasanduke munthu.

13 “Koma ngati upereka mtima wako kwa Iye
    ndi kutambasulira manja ako kwa Iyeyo,
14 ngati utaya tchimo limene lili mʼdzanja lako
    ndi kusalola choyipa kuti chikhale mʼmoyo mwako,
15 udzatukula mutu wako wosachita manyazi;
    udzayima chilili ndipo sudzachita mantha.
16 Udzayiwala ndithu zowawa zako,
    zidzakhala ngati madzi amene apita kale.
17 Moyo wako udzawala kupambana usana,
    ndipo mdima udzakhala ngati mmawa.
18 Udzalimba mtima popeza pali chiyembekezo;
    ndipo udzayangʼana mbali zonse ndi kugona mosatekeseka.
19 Udzagona pansi, popanda wina wokuopseza
    ndipo ambiri adzakupempha kuti uwachitire chifundo.
20 Koma anthu oyipa adzafuna thandizo osalipeza,
    ndipo adzasowa njira yothawirapo;
    chiyembekezo chawo chidzakhala imfa basi.”

Zophar

11 Then Zophar the Naamathite(A) replied:

“Are all these words to go unanswered?(B)
    Is this talker to be vindicated?(C)
Will your idle talk(D) reduce others to silence?
    Will no one rebuke you when you mock?(E)
You say to God, ‘My beliefs are flawless(F)
    and I am pure(G) in your sight.’
Oh, how I wish that God would speak,(H)
    that he would open his lips against you
and disclose to you the secrets of wisdom,(I)
    for true wisdom has two sides.
    Know this: God has even forgotten some of your sin.(J)

“Can you fathom(K) the mysteries of God?
    Can you probe the limits of the Almighty?
They are higher(L) than the heavens(M) above—what can you do?
    They are deeper than the depths below(N)—what can you know?(O)
Their measure(P) is longer than the earth
    and wider than the sea.(Q)

10 “If he comes along and confines you in prison
    and convenes a court, who can oppose him?(R)
11 Surely he recognizes deceivers;
    and when he sees evil, does he not take note?(S)
12 But the witless can no more become wise
    than a wild donkey’s colt(T) can be born human.[a](U)

13 “Yet if you devote your heart(V) to him
    and stretch out your hands(W) to him,(X)
14 if you put away(Y) the sin that is in your hand
    and allow no evil(Z) to dwell in your tent,(AA)
15 then, free of fault, you will lift up your face;(AB)
    you will stand firm(AC) and without fear.(AD)
16 You will surely forget your trouble,(AE)
    recalling it only as waters gone by.(AF)
17 Life will be brighter than noonday,(AG)
    and darkness will become like morning.(AH)
18 You will be secure, because there is hope;
    you will look about you and take your rest(AI) in safety.(AJ)
19 You will lie down, with no one to make you afraid,(AK)
    and many will court your favor.(AL)
20 But the eyes of the wicked will fail,(AM)
    and escape will elude them;(AN)
    their hope will become a dying gasp.”(AO)

Footnotes

  1. Job 11:12 Or wild donkey can be born tame