Add parallel Print Page Options

Chiweruzo ndi Chipulumutso

65 “Ndinali wokonzeka kumva mapemphero a amene sankandipempha kanthu;
    ndipo ndinalola kuti anthu amene ankandifunafuna kuti andipeze.
Kwa mtundu wa anthu umene sunkapempha chithandizo kwa Ine,
    ndinati, ‘Ine ndili pano, Ine ndili pano.’
Tsiku lonse ndatambasulira manja anga
    anthu owukira aja,
amene amachita zoyipa,
    natsatira zokhumba zawo.
Ndatambasulira manja anga anthu aja amene nthawi zonse amandikwiyitsa
    mopanda manyazi.
Iwo amapereka nsembe mʼminda
    ndi kufukiza lubani pa maguwa ansembe a njerwa.
Amakatandala ku manda
    ndipo amakachezera usiku wonse kumalo obisika.
Amadya nyama ya nkhumba,
    ndipo mʼmiphika mwawo muli msunzi wa nyama yodetsedwa.
Amawuza ena kuti, ‘Khala patali usandiyandikire,
    chifukwa ungatengere kupatulika kwanga!’
Ukali wanga pa anthu otere uli ngati utsi mphuno zanga,
    ngati moto umene umayaka tsiku lonse.

“Taonani, ndatsimikiza kale mlandu ndi chilango chawo;
    sindidzakhala chete koma ndidzawalanga kwathunthu
    chifukwa cha machimo awo
ndi a makolo awo,”
    akutero Yehova.
“Chifukwa anapereka nsembe zopsereza pa mapiri
    ndi kundinyoza Ine pa zitunda zawo,
Ine ndidzawalanga kwathunthu potsata
    zimene anachita kale.”

Yehova akuti,

“Pamene madzi akanapezeka mu phava la mphesa
    ndipo anthu amati, ‘Musawononge phavalo,
    popeza madzi ena abwino akanalimobe mʼphavalo,’
Inenso chifukwa cha mtumiki wanga;
    sindidzawononga onse.
Ndidzatulutsa zidzukulu mʼbanja la Yakobo,
    ndipo a banja la Yuda adzalandira mapiri anga ngati cholowa chawo.
Anthu anga osankhidwa adzalandira zimenezi,
    ndipo atumiki anga adzakhala kumeneko.
10 Chigwa cha Saroni chidzakhala kodyetserako nkhosa,
    ndipo chigwa cha Akori chidzakhala malo opumirako ngʼombe
    kwa anthu anga ondifunafuna Ine.

11 “Koma inu amene mumasiya Yehova
    ndi kuyiwala phiri langa lopatulika,
amene munamukonzera Gadi chakudya
    ndi kuthirira Meni chakumwa,
12 ndidzakuperekani ku lupanga ngati nsembe,
    ndipo nonse mudzaphedwa;
chifukwa simunayankhe pamene ndinakuyitanani,
    ndinayankhula koma simunamvere.
Munachita zoyipa pamaso panga
    ndipo munasankha kuchita zoyipa zomwe sindikondwera nazo.”

13 Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti,

“Atumiki anga adzadya,
    koma inu mudzakhala ndi njala;
atumiki anga adzamwa,
    koma inu mudzakhala ndi ludzu;
atumiki anga adzakondwa,
    koma inu mudzakhala ndi manyazi.
14 Atumiki anga adzayimba
    mosangalala,
koma inu mudzalira kwambiri
    chifukwa chovutika mu mtima
    ndipo mudzalira mofuwula chifukwa mudzamva kuwawa mu mtima.
15 Anthu anga osankhidwa
    adzatchula dzina lanu potemberera.
Ambuye Yehova adzakuphani,
    koma atumiki ake adzawapatsa dzina lina.
16 Aliyense wopempha dalitso mʼdzikomo
    adzachita zimenezo kwa Mulungu woona;
ndipo aliyense wochita malumbiro mʼdzikomo
    adzalumbira mwa Mulungu woona.
Pakuti mavuto akale adzayiwalika
    ndipo adzachotsedwa pamaso panga.

Chilengedwe Chatsopano

17 “Taonani, ndikulenga
    mlengalenga mwatsopano ndi dziko lapansi latsopano.
Zinthu zakale sizidzakumbukika,
    zidzayiwalika kotheratu.
18 Koma inu mukhale osangalala ndi okondwa mpaka muyaya
    chifukwa cha zimene ndikulenga,
pakuti ndikulenga Yerusalemu kukhala malo wosangalatsa
    ndipo anthu ake adzakhala achimwemwe.
19 Ine ndidzakondwa chifuwa cha Yerusalemu
    ndipo ndidzasangalala chifukwa cha anthu anga.
Kumeneko sikudzamvekanso kulira
    ndi mfuwu wodandaula.

20 “Ana sadzafa ali akhanda
    ndipo nkhalamba zonse zidzakwaniritsa zaka zawo zonse.
    Wamngʼono mwa iwo
adzafa ali ndi zaka 100.
    Amene adzalephere kufika zaka 100
adzatengedwa kukhala
    wotembereredwa.
21 Anthu adzamanga nyumba ndi kukhalamo,
    adzadzala mpesa ndipo adzadya zipatso zake.
22 Sadzamanganso nyumba anthu ena nʼkukhalamo,
    kapena kudzala ndi ena nʼkudya.
Pakuti anthu anga adzakhala ndi moyo
    wautali ngati mitengo.
Osankhidwa anga adzakondwera ndi ntchito
    ya manja awo nthawi yayitali.
23 Sadzagwira ntchito pachabe
    kapena kubereka ana kuti aone tsoka;
chifukwa adzakhala anthu odalitsidwa ndi Yehova,
    iwowo pamodzi ndi adzukulu awo omwe.
24 Ndidzawayankha ngakhale asanathe nʼkupempha komwe.
    Pamene akuyankhula kumene Ine ndidzakhala nditamva kale.
25 Mʼmbulu ndi mwana wankhosa wamkazi zidzadyera pamodzi.
    Mkango udzadya udzu monga ngʼombe,
    koma fumbi ndiye chidzakhale chakudya cha njoka.
Pa phiri langa lopatulika sipadzakhala
    chinthu chopweteka kapena chowononga,”
            akutero Yehova.

Judgment and Salvation

65 “I revealed myself to those who did not ask for me;
    I was found by those who did not seek me.(A)
To a nation(B) that did not call on my name,(C)
    I said, ‘Here am I, here am I.’
All day long I have held out my hands
    to an obstinate people,(D)
who walk in ways not good,
    pursuing their own imaginations(E)
a people who continually provoke me
    to my very face,(F)
offering sacrifices in gardens(G)
    and burning incense(H) on altars of brick;
who sit among the graves(I)
    and spend their nights keeping secret vigil;
who eat the flesh of pigs,(J)
    and whose pots hold broth of impure meat;
who say, ‘Keep away; don’t come near me,
    for I am too sacred(K) for you!’
Such people are smoke(L) in my nostrils,
    a fire that keeps burning all day.

“See, it stands written before me:
    I will not keep silent(M) but will pay back(N) in full;
    I will pay it back into their laps(O)
both your sins(P) and the sins of your ancestors,”(Q)
    says the Lord.
“Because they burned sacrifices on the mountains
    and defied me on the hills,(R)
I will measure into their laps
    the full payment(S) for their former deeds.”

This is what the Lord says:

“As when juice is still found in a cluster of grapes(T)
    and people say, ‘Don’t destroy it,
    there is still a blessing in it,’
so will I do in behalf of my servants;(U)
    I will not destroy them all.
I will bring forth descendants(V) from Jacob,
    and from Judah those who will possess(W) my mountains;
my chosen(X) people will inherit them,
    and there will my servants live.(Y)
10 Sharon(Z) will become a pasture for flocks,(AA)
    and the Valley of Achor(AB) a resting place for herds,
    for my people who seek(AC) me.

11 “But as for you who forsake(AD) the Lord
    and forget my holy mountain,(AE)
who spread a table for Fortune
    and fill bowls of mixed wine(AF) for Destiny,
12 I will destine you for the sword,(AG)
    and all of you will fall in the slaughter;(AH)
for I called but you did not answer,(AI)
    I spoke but you did not listen.(AJ)
You did evil in my sight
    and chose what displeases me.”(AK)

13 Therefore this is what the Sovereign Lord says:

“My servants will eat,(AL)
    but you will go hungry;(AM)
my servants will drink,(AN)
    but you will go thirsty;(AO)
my servants will rejoice,(AP)
    but you will be put to shame.(AQ)
14 My servants will sing(AR)
    out of the joy of their hearts,
but you will cry out(AS)
    from anguish of heart
    and wail in brokenness of spirit.
15 You will leave your name
    for my chosen ones to use in their curses;(AT)
the Sovereign Lord will put you to death,
    but to his servants he will give another name.(AU)
16 Whoever invokes a blessing(AV) in the land
    will do so by the one true God;(AW)
whoever takes an oath in the land
    will swear(AX) by the one true God.
For the past troubles(AY) will be forgotten
    and hidden from my eyes.

New Heavens and a New Earth

17 “See, I will create
    new heavens and a new earth.(AZ)
The former things will not be remembered,(BA)
    nor will they come to mind.
18 But be glad and rejoice(BB) forever
    in what I will create,
for I will create Jerusalem(BC) to be a delight
    and its people a joy.
19 I will rejoice(BD) over Jerusalem
    and take delight(BE) in my people;
the sound of weeping and of crying(BF)
    will be heard in it no more.

20 “Never again will there be in it
    an infant(BG) who lives but a few days,
    or an old man who does not live out his years;(BH)
the one who dies at a hundred
    will be thought a mere child;
the one who fails to reach[a] a hundred
    will be considered accursed.
21 They will build houses(BI) and dwell in them;
    they will plant vineyards and eat their fruit.(BJ)
22 No longer will they build houses and others live in them,(BK)
    or plant and others eat.
For as the days of a tree,(BL)
    so will be the days(BM) of my people;
my chosen(BN) ones will long enjoy
    the work of their hands.
23 They will not labor in vain,(BO)
    nor will they bear children doomed to misfortune;(BP)
for they will be a people blessed(BQ) by the Lord,
    they and their descendants(BR) with them.
24 Before they call(BS) I will answer;(BT)
    while they are still speaking(BU) I will hear.
25 The wolf and the lamb(BV) will feed together,
    and the lion will eat straw like the ox,(BW)
    and dust will be the serpent’s(BX) food.
They will neither harm nor destroy
    on all my holy mountain,”(BY)
says the Lord.

Footnotes

  1. Isaiah 65:20 Or the sinner who reaches