Add parallel Print Page Options

Kusala Kwenikweni

58 “Fuwula kwambiri, usaleke.
    Mawu ako amveke ngati lipenga.
Uwawuze anthu anga za kulakwa kwawo;
    uwuze nyumba ya Yakobo za machimo awo.
Pakuti tsiku ndi tsiku amafunafuna Ine;
    amaoneka ngati a chidwi chofuna kudziwa zimene ndimafuna,
kukhala ngati kuti ndi dziko limene limachita zolondola
    ndipo silinasiye zolamulira za Mulungu wake.
Amandipempha kuti ndigamule mlandu wawo mwachilungamo
    ndipo amaonetsa chidwi chofuna kukhala pafupi ndi Mulungu.
Anthu akufunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani ife tasala
    kudya pamene Inu simukulabadirapo?
Kodi ife tavutikiranji nʼkudzichepetsa
    pamene Inu simunasamalepo?’ ”

Yehova akuti, “Komatu tsiku lanu losala kudya, mumachita zinthu zokukondweretsani,
    ndipo mumazunza antchito anu onse.
Mumati uku mukusala kudya, uku mukukangana ndi kumenyana,
    mpaka kumenyana ndi nkhonya zopweteka.
Kusala kudya mukuchitiramu musayembekezere kuti mawu anu amveka kumwamba.
Kodi kusala kudya kumene ndimakufuna Ine nʼkumeneku,
    kungokhala tsiku loti munthu adzichepetse basi?
Kodi ndi tsiku loti munthu angowerama pansi ngati bango
    ndi kumayala ziguduli nʼkuthirapo phulusa nʼkugonapo?
Kodi ndiye mumati kusala kudya kumeneko,
    tsiku lokondweretsa Yehova?

“Kodi si uku kusala kudya kumene Ine ndimakufuna:
Kumasula maunyolo ozunzizira anthu
    ndi kumasula zingwe za goli,
kupereka ufulu kwa oponderezedwa
    ndi kuphwanya goli lililonse?
Anthu anjala kodi mwawagawira chakudya chanu?
    Osowa ndi ongoyendayenda,
kodi mwawapatsa malo ogona?
    Munthu wausiwa kodi mwamupatsa chovala?
Mukatero chipulumutso chanu chidzabwera ngati mʼbandakucha,
    ndipo mabala anu adzachira msangamsanga;
chilungamo chanu chidzakutsogolerani
    ndipo ulemerero wa Yehova udzakhala chokutchinjirizani kumbuyo kwanu.
Mukamadzapemphera Yehova adzakuyankhani;
    mukadzapempha thandizo, Iye adzati: Ine ndili pano.

“Ngati muleka kuzunza anzanu,
    ngati musiya kuloza chala ndiponso kunena zoyipa za anzanu.
10 Ndipo ngati mudyetsa anthu anjala,
    ndi kuthandiza anthu oponderezedwa,
pamenepo kuwala kwanu kudzaonekera mu mdima,
    ndipo usiku wanu udzakhala ngati usana.
11 Yehova adzakutsogolerani nthawi zonse;
    adzakwaniritsa zosowa zanu mʼdziko longʼalukangʼaluka dzuwa
    ndipo adzalimbitsa matupi anu.
Mudzakhala ngati dimba la madzi ambiri,
    ngati kasupe amene madzi ake saphwa.
12 Anthu ako adzamanganso nyumba zimene zakhala mabwinja nthawi yayitali,
    ndipo adzamanganso pa maziko akalekale;
inu mudzatchedwa okonza makoma opasuka.
    Anthu okonza misewu ndi nyumba zake.

13 “Muzisunga osaphwanya Sabata;
    musamachite zimene mukufuna pa masiku anga opatulika,
tsiku la Sabata lizikhala tsiku lachisangalalo.
    Tsiku lopatulika la Yehova muzililemekeza
posayenda mʼnjira zanu,
    kapena kuchita zimene mukufuna ndi kuyankhula zopandapake,
14 mukatero mudzapeza chimwemwe mwa Yehova,
    ndipo ndidzakukwezani ndi kukupambanitsani pa dziko lonse lapansi.
    Mudzadyerera dziko limene ndinapatsa Yakobo kholo lanu.”
            Yehova wayankhula ndi pakamwa pake.

True Fasting

58 “Shout it aloud,(A) do not hold back.
    Raise your voice like a trumpet.(B)
Declare to my people their rebellion(C)
    and to the descendants of Jacob their sins.(D)
For day after day they seek(E) me out;
    they seem eager to know my ways,
as if they were a nation that does what is right
    and has not forsaken(F) the commands of its God.
They ask me for just decisions
    and seem eager for God to come near(G) them.
‘Why have we fasted,’(H) they say,
    ‘and you have not seen it?
Why have we humbled(I) ourselves,
    and you have not noticed?’(J)

“Yet on the day of your fasting, you do as you please(K)
    and exploit all your workers.
Your fasting ends in quarreling and strife,(L)
    and in striking each other with wicked fists.
You cannot fast as you do today
    and expect your voice to be heard(M) on high.
Is this the kind of fast(N) I have chosen,
    only a day for people to humble(O) themselves?
Is it only for bowing one’s head like a reed(P)
    and for lying in sackcloth and ashes?(Q)
Is that what you call a fast,
    a day acceptable to the Lord?

“Is not this the kind of fasting(R) I have chosen:
to loose the chains of injustice(S)
    and untie the cords of the yoke,
to set the oppressed(T) free
    and break every yoke?(U)
Is it not to share your food with the hungry(V)
    and to provide the poor wanderer with shelter(W)
when you see the naked, to clothe(X) them,
    and not to turn away from your own flesh and blood?(Y)
Then your light will break forth like the dawn,(Z)
    and your healing(AA) will quickly appear;
then your righteousness[a](AB) will go before you,
    and the glory of the Lord will be your rear guard.(AC)
Then you will call,(AD) and the Lord will answer;(AE)
    you will cry for help, and he will say: Here am I.

“If you do away with the yoke of oppression,
    with the pointing finger(AF) and malicious talk,(AG)
10 and if you spend yourselves in behalf of the hungry
    and satisfy the needs of the oppressed,(AH)
then your light(AI) will rise in the darkness,
    and your night will become like the noonday.(AJ)
11 The Lord will guide(AK) you always;
    he will satisfy your needs(AL) in a sun-scorched land(AM)
    and will strengthen(AN) your frame.
You will be like a well-watered garden,(AO)
    like a spring(AP) whose waters never fail.
12 Your people will rebuild the ancient ruins(AQ)
    and will raise up the age-old foundations;(AR)
you will be called Repairer of Broken Walls,(AS)
    Restorer of Streets with Dwellings.

13 “If you keep your feet from breaking the Sabbath(AT)
    and from doing as you please on my holy day,
if you call the Sabbath a delight(AU)
    and the Lord’s holy day honorable,
and if you honor it by not going your own way
    and not doing as you please or speaking idle words,(AV)
14 then you will find your joy(AW) in the Lord,
    and I will cause you to ride in triumph on the heights(AX) of the land
    and to feast on the inheritance(AY) of your father Jacob.”
For the mouth of the Lord has spoken.(AZ)

Footnotes

  1. Isaiah 58:8 Or your righteous One