Add parallel Print Page Options

57 Anthu olungama amafa,
    ndipo palibe amene amalingalira mu mtima mwake;
anthu odzipereka amatengedwa,
    ndipo palibe amene amamvetsa chifukwa chake.
Anthu olungama amatengedwa
    kuti tsoka lisawagwere.
Iwo amene amakhala moyo wolungama
    amafa mwamtendere;
    amapeza mpumulo pamene agona mu imfa.

“Bwerani kuno, anthu ochita zoyipa,
    inu muli ngati zidzukulu za mkazi wachigololo ndi wadama!
Kodi inu mukuseka yani?
    Kodi mukumunena ndani
    ndi kupotoza pakamwa panu?
Kodi inu si ana owukira,
    zidzukulu za anthu abodza?
Inu mumapembedza mafano pamene mumalobodoka ndi zilakolako zanu pakati pa mitengo ya thundu,
    ndiponso pa tsinde pa mtengo uliwonse wa nthambi zambiri.
Mumapereka ana anu ngati nsembe mu zigwa
    ndiponso mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.
Mafano a pakati pa miyala yosalala ya mu zigwa ndiye chuma chanu. Inde, ndiye gawo lanu.
    Mumapereka chopereka cha chakumwa kwa mafanowo,
ndipo mumaperekanso chopereka cha chakudya.
    Kodi zimenezi
    zingandichititse kuti ndikukomereni mtima?
Inu munayiwala bedi lanu pa phiri lalitali ndi looneka kutali.
    Mumapita kumeneko kukapereka nsembe zanu.
Mʼnyumba mwanu mwayika
    mafano kuseri kwa zitseko ndiponso pa mphuthu.
Mwandisiya Ine, mwavula zovala zanu.
    Bedi lanu mwalikulitsa ndipo mwakwera ndi zibwenzi zanu,
ndiye mwazilipira kuti mugone nazo.
    Kumene mwakwaniritsa zilakolako zanu zoyipa.
Mumapita kukapembedza fano la Moleki mutatenga mafuta
    ndi zonunkhira zochuluka.
Munachita kutumiza akazembe anu kutali;
    inu ngakhale munapita ku manda kwenikweniko!
10 Inu mumatopa ndi maulendo anu,
    koma simunathe kunena kuti, ‘Nʼzopanda phindu.’
Munapezako kumeneko zokhumba zanu
    nʼchifukwa chake simunalefuke.

11 “Kodi ndani amene mwachita naye mantha ndi kumuopa,
    kotero kuti mwakhala mukundinamiza,
ndipo Ine simundikumbukira nʼkomwe,
    kapena kuganizirapo mʼmitima yanu za Ine?
Kodi mwaleka kundiopa chifukwa choti
    ndakhala chete nthawi yayitali?
12 Koma ndaonetsa poyera ntchito zanu zomwe mumati nʼzolungama,
    ndi mafano anu kuti nʼzosathandiza.
13 Pamene mufuwula kupempha thandizo,
    mafano anu amene munasonkhanitsawo ndiyetu akupulumutseni!
Mphepo idzanyamula mafano anu onsewo,
    mpweya chabe udzawulutsa mafanowo.
Koma munthu amene amadalira ine
    adzalandira dziko lokhalamo.
    Phiri langa lopatulika lidzakhala lakelake.”

Mpumulo kwa Anthu Osweka Mtima

14 Ndipo panamveka mawu akuti,

“Undani, undani, konzani msewu!
    Chotsani zotchinga pa njira yoyendamo anthu anga.”
15 Pakuti Iye amene ali Wamkulu ndi Wopambanazonse,
    amene alipo nthawi zonse, amene dzina lake ndi Woyerayo,
akunena kuti, “Ndimakhala pamalo aulemu ndi opatulika,
    koma ndimakhalanso ndi munthu wodzichepetsa ndi wosweka mtima
kuti odzichepetsawo ndiwalimbitse
    ndi kuwachotsa mantha osweka mtima.
16 Sindidzawatsutsa anthu mpaka muyaya
    kapena kuwapsera mtima nthawi zonse,
popeza kuti ndinalenga anthu anga
    ndi kuwapatsa mpweya wamoyo.
17 Ine ndinakwiya kwambiri chifukwa cha tchimo lawo ladyera;
    ndinawalanga ndi kuwafulatira mokwiya,
    koma iwo anapitirirabe kuchita ntchito zawo zoyipa.
18 Ndaona zochita zawo, komabe ndidzawachiritsa;
    kuwapumulitsa ndi kuwapatsa mtendere,
19     anthu olira a mu Israeli adzanditamanda ndi milomo yawo.
Anthu amene ali kutali ndi apafupi pomwe ndidzawapatsa mtendere,”
    “Ndipo ndidzawachiritsa.”
            Akutero Yehova.
20 Koma anthu oyipa ali ngati nyanja yowinduka,
    yosatha kukhala bata,
    mafunde ake amaponya matope ndi ndere.
21 “Palibe mtendere kwa oyipa,” akutero Mulungu wanga.

57 The righteous perish,(A)
    and no one takes it to heart;(B)
the devout are taken away,
    and no one understands
that the righteous are taken away
    to be spared from evil.(C)
Those who walk uprightly(D)
    enter into peace;
    they find rest(E) as they lie in death.

“But you—come here, you children of a sorceress,(F)
    you offspring of adulterers(G) and prostitutes!(H)
Who are you mocking?
    At whom do you sneer
    and stick out your tongue?
Are you not a brood of rebels,(I)
    the offspring of liars?
You burn with lust among the oaks(J)
    and under every spreading tree;(K)
you sacrifice your children(L) in the ravines
    and under the overhanging crags.
The idols(M) among the smooth stones of the ravines are your portion;
    indeed, they are your lot.
Yes, to them you have poured out drink offerings(N)
    and offered grain offerings.
    In view of all this, should I relent?(O)
You have made your bed on a high and lofty hill;(P)
    there you went up to offer your sacrifices.(Q)
Behind your doors and your doorposts
    you have put your pagan symbols.
Forsaking me, you uncovered your bed,
    you climbed into it and opened it wide;
you made a pact with those whose beds you love,(R)
    and you looked with lust on their naked bodies.(S)
You went to Molek[a](T) with olive oil
    and increased your perfumes.(U)
You sent your ambassadors[b](V) far away;
    you descended to the very realm of the dead!(W)
10 You wearied(X) yourself by such going about,
    but you would not say, ‘It is hopeless.’(Y)
You found renewal of your strength,(Z)
    and so you did not faint.

11 “Whom have you so dreaded and feared(AA)
    that you have not been true to me,
and have neither remembered(AB) me
    nor taken this to heart?(AC)
Is it not because I have long been silent(AD)
    that you do not fear me?
12 I will expose your righteousness and your works,(AE)
    and they will not benefit you.
13 When you cry out(AF) for help,
    let your collection of idols save(AG) you!
The wind will carry all of them off,
    a mere breath will blow(AH) them away.
But whoever takes refuge(AI) in me
    will inherit the land(AJ)
    and possess my holy mountain.”(AK)

Comfort for the Contrite

14 And it will be said:

“Build up, build up, prepare the road!(AL)
    Remove the obstacles out of the way of my people.”(AM)
15 For this is what the high and exalted(AN) One says—
    he who lives forever,(AO) whose name is holy:
“I live in a high(AP) and holy place,
    but also with the one who is contrite(AQ) and lowly in spirit,(AR)
to revive the spirit of the lowly
    and to revive the heart of the contrite.(AS)
16 I will not accuse(AT) them forever,
    nor will I always be angry,(AU)
for then they would faint away because of me—
    the very people(AV) I have created.
17 I was enraged by their sinful greed;(AW)
    I punished them, and hid(AX) my face in anger,
    yet they kept on in their willful ways.(AY)
18 I have seen their ways, but I will heal(AZ) them;
    I will guide(BA) them and restore comfort(BB) to Israel’s mourners,
19     creating praise on their lips.(BC)
Peace, peace,(BD) to those far and near,”(BE)
    says the Lord. “And I will heal them.”
20 But the wicked(BF) are like the tossing sea,(BG)
    which cannot rest,
    whose waves cast up mire(BH) and mud.
21 “There is no peace,”(BI) says my God, “for the wicked.”(BJ)

Footnotes

  1. Isaiah 57:9 Or to the king
  2. Isaiah 57:9 Or idols