Add parallel Print Page Options

Israeli ndi Nkhutukumve

48 “Mverani izi, inu nyumba ya Yakobo,
    inu amene amakutchani dzina lanu Israeli,
    ndinu a fuko la Yuda,
inu mumalumbira mʼdzina la Yehova,
    ndi kupemphera kwa Mulungu wa Israeli,
    ngakhale osati mʼchoonadi kapena mʼchilungamo.
Komabe inu mumadzitcha nzika za mzinda wopatulika
    ndipo mumadalira Mulungu wa Israeli,
    amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse:
Zimene zinachitika poyamba ndinalosera kalekale,
    zinatuluka mʼkamwa mwanga ndipo ndinazilengeza;
    tsono mwadzidzidzi ndinachitapo kanthu ndipo zinachitikadi.
Pakuti Ine ndinadziwa kuti iwe ndiwe nkhutukumve
    wa nkhongo gwaa,
    wa mutu wowuma.
Ine ndinakuwuziratu zinthu izi kalekale lomwe;
    zisanachitike ndinazilengezeratu kwa iwe
kuti unganene kuti,
    ‘Fano langa ndilo lachita zimenezi,
    kapena kuti fano langa losema ndi kamulungu kanga kachitsulo ndiwo analamula kuti zimenezi zichitike.’
Inu munamva zinthu zimenezi.
    Kodi inu simungazivomereze?

“Kuyambira tsopano mpaka mʼtsogolo ndidzakuwuzani zinthu zatsopano
    zinthu zobisika zimene simunazidziwe konse.
Zinthu zimenezi zikulengedwa tsopano lino, osati kalekale;
    munali musanazimve mpaka lero lino.
Choncho inu simunganene kuti,
    ‘Zimenezi ndiye ayi, ndinazidziwa kale.’
Inu simunazimvepo kapena kuzidziwa;
    makutu anu sanali otsekuka.
Tsono Ine ndinadziwa bwino kuti ndinu anthu achiwembu ndi kuti
    chiyambire ubwana wanu munatchedwa owukira.
Ine ndikuchedwetsa mkwiyo wanga chifukwa cha dzina langa.
    Ndikukulezerani ukali wanga kuti anthu andilemekeze.
    Sindidzakuwonongani kotheratu.
10 Taonani, ndinakuyeretsani ngati siliva;
    ndinakuyesani mʼngʼanjo yamasautso.
11 Chifukwa cha ulemu wanga, chifukwa cha ulemu wanga Ine ndikuchita zimenezi.
    Ndingalole bwanji kuti ndinyozeke?
    Ulemerero wanga sindidzawupereka kwa wina.

Kumasulidwa kwa Israeli

12 “Tamvera Ine, iwe Yakobo,
    Israeli, amene ndinakuyitana:
Mulungu uja Woyamba
    ndi Wotsiriza ndine.
13 Inde dzanja langa linamanga maziko a dziko lapansi,
    dzanja langa lamanja linafunyulula mlengalenga.
Ndi mawu anga ndinalenga kumwamba
    ndi dziko lapansi.

14 “Sonkhanani pamodzi inu nonse ndipo mvetserani:
    Ndani mwa mafano anu amene analoseratu za zinthu izi?
Wokondedwa wa Yehova uja adzachita
    zomwe Iye anakonzera Babuloni;
    dzanja lake lidzalimbana ndi Kaldeya.
15 Ine, Inetu, ndayankhula;
    ndi kumuyitana
ndidzamubweretsa ndine
    ndipo adzakwaniritsa zolinga zake.

16 “Bwerani pafupi ndipo mvetserani izi:

“Kuyambira pachiyambi sindinayankhule mobisa;
    pa nthawi imene zinkachitika zimenezi Ine ndinali pomwepo.”

Ndipo tsopano Ambuye Yehova wandipatsa Mzimu wake
    ndi kundituma.

17 Yehova, Mpulumutsi wanu,
    Woyerayo wa Israeli akuti,
“Ine ndine Yehova Mulungu wanu,
    amene ndimakuphunzitsa kuti upindule,
    ndimakutsogolera pa njira yoyenera kuyitsata.
18 Ngati iwe ukanangosamalira zolamulira zanga,
    bwenzi mtendere wako ukanakhala ngati mtsinje,
    ndi chipulumutso chako ngati mafunde a pa nyanja.
19 Zidzukulu zako zikanachuluka ngati mchenga,
    ana ako akanachuluka ngati fumbi;
dzina lawo silikanachotsedwa pamaso panga
    ndipo silikanafafanizidwa konse.”

20 Tulukani mʼdziko la Babuloni!
    Thawani dziko la Kaldeya!
Lengezani zimenezi ndi mawu a chisangalalo
    ndipo muzilalikire
mpaka kumathero a dziko lapansi;
    muzinena kuti, “Yehova wawombola Yakobo mtumiki wake.”
21 Iwo sanamve ludzu pamene Yehova ankawatsogolera mʼchipululu;
    anawapatsa madzi otuluka mʼthanthwe;
anangʼamba thanthwelo ndipo
    munatuluka madzi.

22 “Palibe mtendere kwa anthu ochimwa,” akutero Yehova.