Add parallel Print Page Options

Kugwa kwa Babuloni

47 “Tsika, ndi kukhala pa fumbi,
    iwe namwali, Babuloni;
khala pansi wopanda mpando waufumu,
    iwe namwali, Kaldeya
pakuti sadzakutchulanso wanthete kapena woyenera
    kumugwira mosamala.
Tenga mphero ndipo upere ufa;
    chotsa nsalu yako yophimba nkhope
kwinya chovala chako mpaka ntchafu
    ndipo woloka mitsinje.
Maliseche ako adzakhala poyera
    ndipo udzachita manyazi.
Ndidzabwezera chilango
    ndipo palibe amene adzandiletse.”

Woyerayo wa Israeli ndiye Mpulumutsi wathu,
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.

“Khala chete, ndipo lowa mu mdima,
    iwe namwali, Kaldeya;
chifukwa sadzakutchulanso
    mfumukazi ya maufumu.
Ndinawakwiyira anthu anga,
    osawasamalanso.
Ndinawapereka manja mwako,
    ndipo iwe sunawachitire chifundo.
Iwe unachitira nkhanza
    ngakhale nkhalamba.
Iwe unati, ‘Ine ndidzakhalapo nthawi zonse
    ngati mfumukazi.’
Koma sunaganizire zinthu izi
    kapena kusinkhasinkha za mmene ziti zidzathere.

“Ndipo tsopano, tamvera, iwe wongokonda zokondweretsawe,
    amene ukukhala mosatekesekawe,
umaganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndi Ine, ndipo kupatula ine palibenso wina.
Sindidzakhala konse mkazi wamasiye,
    ndipo ana anga sadzamwalira.’
Koma mʼkamphindi, ndiponso tsiku limodzi,
    zinthu ziwiri izi zidzakuchitikira:
    ana ako kukufera komanso kukhala mkazi wamasiye.
Zimenezi zidzakuchitikira kwathunthu
    ngakhale ali ndi amatsenga ambiri
    ndi mawula amphamvu.
10 Iwe unkadalira kuyipa kwako
    ndipo unati, ‘Palibe amene akundiona.’
Kuchenjera ndi nzeru zako zidzakusokoneza,
    choncho ukuganiza mu mtima mwako kuti,
    ‘Ine ndine basi, ndipo kupatula ine palibenso wina.’
11 Ngozi yayikulu idzakugwera
    ndipo sudzadziwa momwe ungayipewere ndi matsenga ako.
Mavuto adzakugwera
    ndipo sudzatha kuwachotsa;
chipasupasu chimene iwe sukuchidziwa
    chidzakugwera mwadzidzidzi.

12 “Pitiriza tsono kukhala ndi matsenga ako,
    pamodzi ndi nyanga zako zochulukazo,
    wakhala ukuzigwiritsa ntchito kuyambira ubwana wako.
Mwina udzatha kupambana
    kapena kuopsezera nazo adani ako.
13 Malangizo onse amene unalandira angokutopetsa basi!
    Abwere patsogolopa anthu amene amatanthauzira za kumwamba kuti adzakupulumutseni.
Abwere amene amayangʼana nyenyezi, ndi kumalosera mwezi ndi mwezi
    zimene ziti zidzakuchitikire.
14 Ndithudi, anthuwo ali ngati phesi;
    adzapsa ndi moto.
Sangathe kudzipulumutsa okha
    ku mphamvu ya malawi a moto.
Awa si makala a moto woti wina nʼkuwotha;
    kapena moto woti wina nʼkuwukhalira pafupi.
15 Umu ndi mmene adzachitire amatsenga,
    anthu amene wakhala ukugwira nawo ntchito
    ndi kuchita nawo malonda chiyambire cha ubwana wako.
Onse adzamwazika ndi mantha,
    sipadzakhala ndi mmodzi yemwe wokupulumutsa.”

The Fall of Babylon

47 “Go down, sit in the dust,(A)
    Virgin Daughter(B) Babylon;
sit on the ground without a throne,
    queen city of the Babylonians.[a](C)
No more will you be called
    tender or delicate.(D)
Take millstones(E) and grind(F) flour;
    take off your veil.(G)
Lift up your skirts,(H) bare your legs,
    and wade through the streams.
Your nakedness(I) will be exposed
    and your shame(J) uncovered.
I will take vengeance;(K)
    I will spare no one.(L)

Our Redeemer(M)—the Lord Almighty(N) is his name(O)
    is the Holy One(P) of Israel.

“Sit in silence,(Q) go into darkness,(R)
    queen city of the Babylonians;(S)
no more will you be called
    queen(T) of kingdoms.(U)
I was angry(V) with my people
    and desecrated my inheritance;(W)
I gave them into your hand,(X)
    and you showed them no mercy.(Y)
Even on the aged
    you laid a very heavy yoke.
You said, ‘I am forever(Z)
    the eternal queen!’(AA)
But you did not consider these things
    or reflect(AB) on what might happen.(AC)

“Now then, listen, you lover of pleasure,
    lounging in your security(AD)
and saying to yourself,
    ‘I am, and there is none besides me.(AE)
I will never be a widow(AF)
    or suffer the loss of children.’
Both of these will overtake you
    in a moment,(AG) on a single day:
    loss of children(AH) and widowhood.(AI)
They will come upon you in full measure,
    in spite of your many sorceries(AJ)
    and all your potent spells.(AK)
10 You have trusted(AL) in your wickedness
    and have said, ‘No one sees me.’(AM)
Your wisdom(AN) and knowledge mislead(AO) you
    when you say to yourself,
    ‘I am, and there is none besides me.’
11 Disaster(AP) will come upon you,
    and you will not know how to conjure it away.
A calamity will fall upon you
    that you cannot ward off with a ransom;
a catastrophe you cannot foresee
    will suddenly(AQ) come upon you.

12 “Keep on, then, with your magic spells
    and with your many sorceries,(AR)
    which you have labored at since childhood.
Perhaps you will succeed,
    perhaps you will cause terror.
13 All the counsel you have received has only worn you out!(AS)
    Let your astrologers(AT) come forward,
those stargazers who make predictions month by month,
    let them save(AU) you from what is coming upon you.
14 Surely they are like stubble;(AV)
    the fire(AW) will burn them up.
They cannot even save themselves
    from the power of the flame.(AX)
These are not coals for warmth;
    this is not a fire to sit by.
15 That is all they are to you—
    these you have dealt with
    and labored(AY) with since childhood.
All of them go on in their error;
    there is not one that can save(AZ) you.

Footnotes

  1. Isaiah 47:1 Or Chaldeans; also in verse 5