Add parallel Print Page Options

Yehova Yekha Mpulumutsi wa Israeli

43 Koma tsopano, Yehova
    amene anakulenga, iwe Yakobo,
    amene anakuwumba, iwe Israeli akuti,
“Usaope, pakuti ndakuwombola;
    Ndinakuyitanitsa mokutchula dzina lako, ndiwe wanga.
Pamene ukuwoloka nyanja,
    ndidzakhala nawe;
ndipo pamene ukuwoloka mitsinje,
    sidzakukokolola.
Pamene ukudutsa pa moto,
    sudzapsa;
    lawi la moto silidzakutentha.
Chifukwa Ine Yehova, Mulungu wako,
    Woyera wa Israeli, ndine Mpulumutsi wako.
Ndinapereka Igupto pofuna kuti ndiwombole iwe,
    ndinapereka Kusi ndi Seba mʼmalo mwa iwe.
Popeza kuti ndiwe wamtengowapatali wolemekezeka ndi wapamtima panga,
    ndipo chifukwa ndimakukonda,
ndidzapereka anthu mʼmalo mwa iwe,
    ndidzapereka mitundu ya anthu pofuna kuwombola moyo wako.
Usachite mantha, pakuti Ine ndili nawe;
    ndidzabweretsa ana ako kuchokera kummawa,
    ndipo ndidzakusonkhanitsani kuchokera kumadzulo.
Ndidzawuza a kumpoto kuti, ‘Amasuleni,’
    ndidzawuza akummwera kuti, ‘Musawagwire.’
Bweretsani ana anga aamuna kuchokera ku mayiko akutali,
    ana anga a akazi kuchokera kumalekezero a dziko lapansi;
onsewo amadziwika ndi dzina langa;
    ndinawalenga chifukwa cha ulemerero wanga,
    ndinawawumba, inde ndinawapanga.”
Tulutsa anthu amene ali nawo maso koma sakupenya,
    anthu amene ali nawo makutu koma sakumva.
Mitundu yonse ya anthu isonkhane pamodzi,
    anthu a mitundu ina akhale pamodzi pabwalo la milandu.
Ndani wa iwo amene ananeneratu zimenezi?
    Ndani wa iwo anatifotokozerapo zinthu zakalekale?
Abweretu ndi mboni zawo kuti adzatsimikizire kuti ananena zoona,
    kuti anthu ena amve ndi kunena kuti, “Ndi zoona.”
10 Yehova akunena kuti, “Inu Aisraeli ndinu mboni zanga,
    ndi mtumiki wanga amene ndinakusankha,
kuti mundidziwe ndi kundikhulupirira, ndipo mudzamvetsa kuti Mulungu ndine ndekha.
    Patsogolo panga sipanapangidwepo mulungu wina,
ngakhale pambuyo panga
    sipadzakhalaponso wina.”
11 Akutero Yehova, “Ine, Inetu ndine Yehova,
    ndipo palibe Mpulumutsi wina koma Ine ndekha.
12 Ndine amene ndinaneneratu, amene ndinakupulumutsa;
    ndine, osati mulungu wina wachilendo pakati panu amene ndinalengezeratu.
Inu ndinu mboni zanga, kuti Ine ndine Mulungu,” akutero Yehova.
13     “Ine ndine Mulungu kuyambira nthawi yamakedzana, ndipo ndidzakhalabe Mulungu ku nthawi zonse.
Palibe amene angathe kuthawa mʼmanja mwanga,
    ndipo chimene ndachita palibe angathe kuchisintha.”

Chifundo cha Mulungu ndi Kusakhulupirika kwa Israeli

14 Yehova akuti,
    Mpulumutsi wanu, Woyerayo wa Israeli akuti,
“Chifukwa cha inu ndidzatuma gulu lankhondo kukalimbana ndi Babuloni
    ndi kukupulumutsani.
    Ndidzagwetsa zitseko zonse za mzindawo, ndipo kukondwa kwa anthu ake kudzasanduka kulira.
15 Ine ndine Yehova, Woyera wanu uja,
    Mlengi wa Israeli. Ine ndine Mfumu yanu.”

16 Yehova
    anapanga njira pa nyanja,
    anapanga njira pakati pa madzi amphamvu.
17 Iye anasonkhanitsa magaleta, akavalo,
    gulu lankhondo ndi asilikali amphamvu,
ndipo onse anagwa pamenepo, osadzukanso
    anazimitsidwa kutheratu ngati chingwe cha nyale. Yehova ameneyu akuti,
18 “Iwalani zinthu zakale;
    ndipo musaganizirenso zinthu zimene zinachitika kale.
19 Taonani, Ine ndikuchita zinthu zatsopano!
    Tsopano zayamba kale kuoneka; kodi simukuziona?
Ine ndikulambula msewu mʼchipululu
    ndi kupanga mitsinje mʼdziko lowuma.
20 Nyama zakuthengo, nkhandwe ndi akadzidzi
    zinandilemekeza.
Ndidzayendetsa mitsinje mʼdziko lowuma
    kuti ndiwapatse madzi anthu anga
osankhidwa.
21     Anthu amene ndinadziwumbira ndekha
    kuti aziyimba nyimbo yotamanda Ine.

22 “Komatu simunapemphera kwa Ine, Inu a mʼbanja la Yakobo,
    munatopa nane, Inu Aisraeli.
23 Simunabweretse kwa Ine nkhosa za nsembe zopsereza,
    kapena kundilemekeza ndi nsembe zanu.
Ine sindinakulemetseni pomakupemphani zopereka za chakudya
    kapena kukutopetsani pomakupemphani nsembe zofukiza.
24 Simunandigulire bango lonunkhira
    kapena kundipatsa Ine mafuta okwanira a nsembe zanu.
Koma inu mwandilemetsa Ine ndi machimo anu
    ndipo mwanditopetsa Ine ndi zolakwa zanu.

25 “Ine, Inetu, ndi amene ndimafafaniza
    zolakwa zanu, chifukwa cha Ine mwini,
    ndipo sindidzakumbukiranso machimo anu.
26 Mundikumbutse zakale,
    ndipo titsutsane nkhaniyi pamodzi;
    fotokozani mlandu wanu kuti muonetse kuti ndinu osalakwa.
27 Kholo lanu loyamba linachimwa;
    ndipo Atsogoleri anu achipembedzo anandiwukira.
28 Chifukwa chake Ine ndidzanyazitsa akuluakulu a Nyumba yanu ya mapemphero,
    ndipo ndidzapereka Yakobo kuti awonongedwe
    ndi Israeli kuti achitidwe chipongwe.”

Israel’s Only Savior

43 But now, this is what the Lord says—
    he who created(A) you, Jacob,
    he who formed(B) you, Israel:(C)
“Do not fear, for I have redeemed(D) you;
    I have summoned you by name;(E) you are mine.(F)
When you pass through the waters,(G)
    I will be with you;(H)
and when you pass through the rivers,
    they will not sweep over you.
When you walk through the fire,(I)
    you will not be burned;
    the flames will not set you ablaze.(J)
For I am the Lord your God,(K)
    the Holy One(L) of Israel, your Savior;(M)
I give Egypt(N) for your ransom,
    Cush[a](O) and Seba(P) in your stead.(Q)
Since you are precious and honored(R) in my sight,
    and because I love(S) you,
I will give people in exchange for you,
    nations in exchange for your life.
Do not be afraid,(T) for I am with you;(U)
    I will bring your children(V) from the east
    and gather(W) you from the west.(X)
I will say to the north, ‘Give them up!’
    and to the south,(Y) ‘Do not hold them back.’
Bring my sons from afar
    and my daughters(Z) from the ends of the earth(AA)
everyone who is called by my name,(AB)
    whom I created(AC) for my glory,(AD)
    whom I formed and made.(AE)

Lead out those who have eyes but are blind,(AF)
    who have ears but are deaf.(AG)
All the nations gather together(AH)
    and the peoples assemble.
Which of their gods foretold(AI) this
    and proclaimed to us the former things?
Let them bring in their witnesses to prove they were right,
    so that others may hear and say, “It is true.”
10 “You are my witnesses,(AJ)” declares the Lord,
    “and my servant(AK) whom I have chosen,
so that you may know(AL) and believe me
    and understand that I am he.
Before me no god(AM) was formed,
    nor will there be one after me.(AN)
11 I, even I, am the Lord,(AO)
    and apart from me there is no savior.(AP)
12 I have revealed and saved and proclaimed—
    I, and not some foreign god(AQ) among you.
You are my witnesses,(AR)” declares the Lord, “that I am God.
13     Yes, and from ancient days(AS) I am he.(AT)
No one can deliver out of my hand.
    When I act, who can reverse it?”(AU)

God’s Mercy and Israel’s Unfaithfulness

14 This is what the Lord says—
    your Redeemer,(AV) the Holy One(AW) of Israel:
“For your sake I will send to Babylon
    and bring down as fugitives(AX) all the Babylonians,[b](AY)
    in the ships in which they took pride.
15 I am the Lord,(AZ) your Holy One,
    Israel’s Creator,(BA) your King.(BB)

16 This is what the Lord says—
    he who made a way through the sea,
    a path through the mighty waters,(BC)
17 who drew out(BD) the chariots and horses,(BE)
    the army and reinforcements together,(BF)
and they lay(BG) there, never to rise again,
    extinguished, snuffed out like a wick:(BH)
18 “Forget the former things;(BI)
    do not dwell on the past.
19 See, I am doing a new thing!(BJ)
    Now it springs up; do you not perceive it?
I am making a way in the wilderness(BK)
    and streams in the wasteland.(BL)
20 The wild animals(BM) honor me,
    the jackals(BN) and the owls,
because I provide water(BO) in the wilderness
    and streams in the wasteland,
to give drink to my people, my chosen,
21     the people I formed(BP) for myself(BQ)
    that they may proclaim my praise.(BR)

22 “Yet you have not called on me, Jacob,
    you have not wearied(BS) yourselves for[c] me, Israel.(BT)
23 You have not brought me sheep for burnt offerings,(BU)
    nor honored(BV) me with your sacrifices.(BW)
I have not burdened(BX) you with grain offerings
    nor wearied you with demands(BY) for incense.(BZ)
24 You have not bought any fragrant calamus(CA) for me,
    or lavished on me the fat(CB) of your sacrifices.
But you have burdened me with your sins
    and wearied(CC) me with your offenses.(CD)

25 “I, even I, am he who blots out
    your transgressions,(CE) for my own sake,(CF)
    and remembers your sins(CG) no more.(CH)
26 Review the past for me,
    let us argue the matter together;(CI)
    state the case(CJ) for your innocence.
27 Your first father(CK) sinned;
    those I sent to teach(CL) you rebelled(CM) against me.
28 So I disgraced the dignitaries of your temple;
    I consigned Jacob to destruction[d](CN)
    and Israel to scorn.(CO)

Footnotes

  1. Isaiah 43:3 That is, the upper Nile region
  2. Isaiah 43:14 Or Chaldeans
  3. Isaiah 43:22 Or Jacob; / surely you have grown weary of
  4. Isaiah 43:28 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.