Add parallel Print Page Options

Mulungu Thandizo la Israeli

41 “Khalani chete pamaso panga, inu mayiko a mʼmbali mwa nyanja!
    Alekeni ayandikire ndi kuyankhula;
tiyeni tikhale pamodzi
    kuti atiweruze.

“Ndani anadzutsa wochokera kummawa
    uja amene ananka napambana kulikonse kumene ankapita?
Iye amapereka anthu a mitundu ina mʼmanja mwake
    ndipo ndi lupanga lake anagonjetsa
ndi kusandutsa mafumu kukhala ngati fumbi
    nawamwaza ngati mankhusu ndi uta wake.
Amawalondola namayenda mosavutika,
    mʼnjira imene mapazi ake sanayendemo kale.
Ndani anachita zimenezi ndi kuzitsiriza,
    si uja amene anayambitsa mitundu ya anthu?
Ine Yehova, ndine chiyambi
    ndipo potsiriza pake ndidzakhalapo.”

Mayiko amʼmbali mwa nyanja aona zimenezi ndipo akuopa;
    anthu a ku mathero a dziko lapansi akunjenjemera.
Akuyandikira pafupi, akubwera;
    aliyense akuthandiza mnzake
    ndipo akuwuza mʼbale wake kuti, “Limba mtima!”
Mʼmisiri wa matabwa amalimbikitsa mʼmisiri wa golide,
    ndipo iye amene amasalaza fano ndi nyundo
    amalimbikitsa amene amalisanja pa chipala.
Ponena za kuwotcherera iye amati, “Zili bwino.”
    Iye amalikhomerera fanolo ndi misomali kuti lisagwe.

“Koma Iwe Israeli mtumiki wanga,
    Yakobo amene ndakusankha,
    Ndiwe chidzukulu cha Abrahamu bwenzi langa.
Ndinakutengani kuchokera ku mapeto a dziko lapansi,
    ndinakuyitanani kuchokera ku mbali za kutali za dziko lapansi.
Ine ndinati, ‘Iwe ndiwe mtumiki wanga;’
    Ndinakusankha ndipo sindinakutaye.
10 Tsono usaope, pakuti Ine ndili nawe;
    usataye mtima chifukwa Ine ndine Mulungu wako.
Ndidzakupatsa mphamvu ndipo ndidzakuthandiza,
    ndidzakutchinjiriza ndi dzanja langa lamanja logonjetsa.

11 “Onse amene akupsera mtima
    adzachita manyazi ndithu ndi kunyazitsidwa;
onse amene akukangana nawe
    sadzakhalanso kanthu, adzawonongeka.
12 Udzafunafuna adani ako,
    koma sadzapezeka.
Iwo amene akuchita nawe nkhondo
    sadzakhalanso kanthu.
13 Pakuti Ine Yehova, ndine Mulungu wako,
    amene ndikukugwira dzanja lako lamanja
ndipo ndikuti, usaope;
    ndidzakuthandiza.
14 Usachite mantha, iwe Yakobo wofowoka ngati nyongolotsi,
    iwe wochepa mphamvu Israeli,
chifukwa Ine ndidzakuthandiza,”
    akutero Yehova Mpulumutsi wako, Woyerayo wa Israeli.
15 “Taona, ndidzakusandutsa ngati chipangizo chopunthira tirigu
    chatsopano, chakunthwa ndi cha mano ambiri.
Udzanyenya mapiri ndi kuwaphwanyaphwanya,
    ndipo zitunda adzazisandutsa ngati mankhusu.
16 Udzawapeta ndipo adzawuluka ndi mphepo komanso
    adzamwazika ndi kamvuluvulu.
Koma iwe udzakondwera chifukwa Ine ndine Mulungu wako,
    ndipo udzanyadira chifukwa cha Ine Woyerayo wa Israeli:

17 “Pamene amphawi ndi osauka akufunafuna madzi,
    koma sakuwapeza;
    ndipo kummero kwawo kwawuma ndi ludzu.
Ine Yehova ndidzayankha pemphero lawo;
    Ine, Mulungu wa Israeli, sindidzawasiya.
18 Ndidzayendetsa mitsinje mʼmalo owuma,
    ndi akasupe adzatumphuka mu zigwa.
Ndidzasandutsa chipululu kukhala dziwe la madzi
    ndipo dziko lowuma kukhala akasupe a madzi.
19 Mʼchipululu ndidzameretsa
    mkungudza, kasiya mchisu ndi mtengo wa Olivi.
Mʼdziko lowuma ndidzaza mitengo
    ya payini, ya mkuyu ndi ya mlombwa,
20 kuti anthu aone ndi kudziwa;
    inde, alingalire ndi kumvetsa,
kuti Yehova ndiye wachita zimenezi;
    kuti Woyera wa Israeli ndiye anakonza zimenezi.

21 “Yehova akuwuza milungu ina kuti, ‘Fotokozani mlandu wanu.’
    Mfumu ya Yakobo ikuti, ‘Perekani umboni wanu.’
22 Bwerani ndi milungu yanu kuti idzatiwuze
    zomwe zidzachitike mʼtsogolo.
Tifotokozereni zinthu zamakedzana
    tiziganizire
    ndi kudziwa zotsatira zake.
Kapena tiwuzeni zimene zidzachitike mʼtsogolo,
23     tiwuzeni kuti kutsogolo kuli zotani,
    ndipo ife tidziwa kuti ndinu milungu.
Chitani chinthu chabwino kapena choyipa,
    ndipo mutidabwitsa ndi kutichititsa mantha.
24 Koma inu sindinu kanthu
    ndipo zochita zanu nʼzopandapake;
    amene amapembedza inu ali ngati chinthu chokanidwa chifukwa ndi choyipa.

25 “Ndinawutsa munthu wina kumpoto ndipo anabwera,
    munthu wochokera kummawa amene ndinamuyitana.
Amapondaponda olamulira ngati matope,
    ngati ndi wowumba mbiya amene akuponda dongo.
26 Ndani anawululiratu zimenezi poyamba pomwe, kuti ife tidziwe,
    kapena kutiwuziratu zisanachitike kuti ife tinene kuti, ‘Analondola?’
Palibe amene ananena,
    palibe analengeza zimenezi,
    palibe anamva mawu anu.
27 Ine ndinali woyamba kumuwuza Ziyoni kuti, ‘Taona, si awa akubwera apawa!’
    Ndinatumiza mthenga wa nkhani yabwino ku Yerusalemu.
28 Koma ndikayangʼana palibe ndi mmodzi yemwe,
    palibe ndi mmodzi yemwe pakati pawo wotha kupereka uphungu,
    palibe woti ayankhe pamene ine ndawafunsa.
29 Taonani, milungu yonseyi ndi yachinyengo!
    Zochita zawo si kanthu konse;
    mafano awo ali ngati mphepo yachabechabe.

The Helper of Israel

41 “Be silent(A) before me, you islands!(B)
    Let the nations renew their strength!(C)
Let them come forward(D) and speak;
    let us meet together(E) at the place of judgment.

“Who has stirred(F) up one from the east,(G)
    calling him in righteousness(H) to his service[a]?(I)
He hands nations over to him
    and subdues kings before him.
He turns them to dust(J) with his sword,
    to windblown chaff(K) with his bow.(L)
He pursues them and moves on unscathed,(M)
    by a path his feet have not traveled before.
Who has done this and carried it through,
    calling(N) forth the generations from the beginning?(O)
I, the Lord—with the first of them
    and with the last(P)—I am he.(Q)

The islands(R) have seen it and fear;
    the ends of the earth(S) tremble.
They approach and come forward;
    they help each other
    and say to their companions, “Be strong!(T)
The metalworker(U) encourages the goldsmith,(V)
    and the one who smooths with the hammer
    spurs on the one who strikes the anvil.
One says of the welding, “It is good.”
    The other nails down the idol so it will not topple.(W)

“But you, Israel, my servant,(X)
    Jacob, whom I have chosen,(Y)
    you descendants of Abraham(Z) my friend,(AA)
I took you from the ends of the earth,(AB)
    from its farthest corners I called(AC) you.
I said, ‘You are my servant’;(AD)
    I have chosen(AE) you and have not rejected you.
10 So do not fear,(AF) for I am with you;(AG)
    do not be dismayed, for I am your God.
I will strengthen(AH) you and help(AI) you;
    I will uphold you(AJ) with my righteous right hand.(AK)

11 “All who rage(AL) against you
    will surely be ashamed and disgraced;(AM)
those who oppose(AN) you
    will be as nothing and perish.(AO)
12 Though you search for your enemies,
    you will not find them.(AP)
Those who wage war against you
    will be as nothing(AQ) at all.
13 For I am the Lord your God
    who takes hold of your right hand(AR)
and says to you, Do not fear;
    I will help(AS) you.
14 Do not be afraid,(AT) you worm(AU) Jacob,
    little Israel, do not fear,
for I myself will help(AV) you,” declares the Lord,
    your Redeemer,(AW) the Holy One(AX) of Israel.
15 “See, I will make you into a threshing sledge,(AY)
    new and sharp, with many teeth.
You will thresh the mountains(AZ) and crush them,
    and reduce the hills to chaff.(BA)
16 You will winnow(BB) them, the wind will pick them up,
    and a gale(BC) will blow them away.(BD)
But you will rejoice(BE) in the Lord
    and glory(BF) in the Holy One(BG) of Israel.

17 “The poor and needy search for water,(BH)
    but there is none;
    their tongues are parched with thirst.(BI)
But I the Lord will answer(BJ) them;
    I, the God of Israel, will not forsake(BK) them.
18 I will make rivers flow(BL) on barren heights,
    and springs within the valleys.
I will turn the desert(BM) into pools of water,(BN)
    and the parched ground into springs.(BO)
19 I will put in the desert(BP)
    the cedar and the acacia,(BQ) the myrtle and the olive.
I will set junipers(BR) in the wasteland,
    the fir and the cypress(BS) together,(BT)
20 so that people may see and know,(BU)
    may consider and understand,(BV)
that the hand(BW) of the Lord has done this,
    that the Holy One(BX) of Israel has created(BY) it.

21 “Present your case,(BZ)” says the Lord.
    “Set forth your arguments,” says Jacob’s King.(CA)
22 “Tell us, you idols,
    what is going to happen.(CB)
Tell us what the former things(CC) were,
    so that we may consider them
    and know their final outcome.
Or declare to us the things to come,(CD)
23     tell us what the future holds,
    so we may know(CE) that you are gods.
Do something, whether good or bad,(CF)
    so that we will be dismayed(CG) and filled with fear.
24 But you are less than nothing(CH)
    and your works are utterly worthless;(CI)
    whoever chooses you is detestable.(CJ)

25 “I have stirred(CK) up one from the north,(CL) and he comes—
    one from the rising sun who calls on my name.
He treads(CM) on rulers as if they were mortar,
    as if he were a potter treading the clay.
26 Who told of this from the beginning,(CN) so we could know,
    or beforehand, so we could say, ‘He was right’?
No one told of this,
    no one foretold(CO) it,
    no one heard any words(CP) from you.
27 I was the first to tell(CQ) Zion, ‘Look, here they are!’
    I gave to Jerusalem a messenger of good news.(CR)
28 I look but there is no one(CS)
    no one among the gods to give counsel,(CT)
    no one to give answer(CU) when I ask them.
29 See, they are all false!
    Their deeds amount to nothing;(CV)
    their images(CW) are but wind(CX) and confusion.

Footnotes

  1. Isaiah 41:2 Or east, / whom victory meets at every step