Add parallel Print Page Options

Tsiku limenelo akazi asanu ndi awiri
    adzagwira mwamuna mmodzi,
nʼkunena kuti, “Ife tizidya chakudya chathuchathu,
    ndi kuvala zovala zathu;
inu mungotilola kuti tidziyitanidwa ndi dzina lanu.
    Tichotseni manyazi aumbeta!”

Nthambi ya Yehova

Tsiku limenelo Nthambi ya Yehova idzakhala yokongola ndi yaulemerero, ndipo chipatso cha mʼdziko chidzakhala chonyaditsa ndi chopereka ulemerero kwa onse opulumuka mu Israeli. Iwo amene adzatsale mu Ziyoni, amene adzatsalire mu Yerusalemu, adzatchedwa oyera, onse amene mayina awo alembedwa pakati pa anthu amoyo okhala mu Yerusalemu. Ambuye adzasambitsa akazi a Ziyoni ndi kuchotsa zonyansa zawo. Adzatsuka magazi amene anakhetsedwa mu Yerusalemu ndi mzimu wachiweruzo ndiponso mzimu wamoto. Tsono Yehova adzayika mtambo wake pamwamba ponse pa phiri la Ziyoni, ndipo pa onse amene asonkhana masana padzakhala mtambo wa utsi ndipo usiku padzakhala malawi amoto. Pamwamba pa zonse padzakhala ulemerero wa Yehova. Ulemerero wake udzakhala mthunzi wothawiramo kutentha kwa masana, udzakhala malo opeweramo mphepo ndi owusiramo mvula.

In that day(A) seven women
    will take hold of one man(B)
and say, “We will eat our own food(C)
    and provide our own clothes;
only let us be called by your name.
    Take away our disgrace!”(D)

The Branch of the Lord

In that day(E) the Branch of the Lord(F) will be beautiful(G) and glorious, and the fruit(H) of the land will be the pride and glory(I) of the survivors(J) in Israel. Those who are left in Zion,(K) who remain(L) in Jerusalem, will be called holy,(M) all who are recorded(N) among the living in Jerusalem. The Lord will wash away the filth(O) of the women of Zion;(P) he will cleanse(Q) the bloodstains(R) from Jerusalem by a spirit[a] of judgment(S) and a spirit[b] of fire.(T) Then the Lord will create(U) over all of Mount Zion(V) and over those who assemble there a cloud of smoke by day and a glow of flaming fire by night;(W) over everything the glory[c](X) will be a canopy.(Y) It will be a shelter(Z) and shade from the heat of the day, and a refuge(AA) and hiding place from the storm(AB) and rain.

Footnotes

  1. Isaiah 4:4 Or the Spirit
  2. Isaiah 4:4 Or the Spirit
  3. Isaiah 4:5 Or over all the glory there