Add parallel Print Page Options

Chimwemwe cha Opulumutsidwa

35 Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala;
    dziko lowuma lidzakondwa
ndi kuchita maluwa. Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka
    lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe.
Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni,
    maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni.

Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova,
    ukulu wa Mulungu wathu.
Limbitsani manja ofowoka,
    limbitsani mawondo agwedegwede;
nenani kwa a mitima yamantha kuti;
    “Limbani mtima, musachite mantha;
Mulungu wanu akubwera,
    akubwera kudzalipsira;
ndi kudzabwezera chilango adani anu;
    akubwera kudzakupulumutsani.”

Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso
    ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala,
    ndipo osayankhula adzayimba mokondwera.
Akasupe adzatumphuka mʼchipululu
    ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
mchenga wotentha udzasanduka dziwe,
    nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe.
Pamene panali mbuto ya ankhandwe
    padzamera udzu ndi bango.

Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu;
    ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika.
Anthu odetsedwa
    sadzayendamo mʼmenemo;
    zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
Kumeneko sikudzakhala mkango,
    ngakhale nyama yolusa sidzafikako;
    sidzapezeka konse kumeneko.
Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10     Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera.
Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba;
    kumeneko adzakondwa mpaka muyaya.
Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe,
    ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.

Joy of the Redeemed

35 The desert(A) and the parched land will be glad;
    the wilderness will rejoice and blossom.(B)
Like the crocus,(C) it will burst into bloom;
    it will rejoice greatly and shout for joy.(D)
The glory of Lebanon(E) will be given to it,
    the splendor of Carmel(F) and Sharon;(G)
they will see the glory(H) of the Lord,
    the splendor of our God.(I)

Strengthen the feeble hands,
    steady the knees(J) that give way;
say(K) to those with fearful hearts,(L)
    “Be strong, do not fear;(M)
your God will come,(N)
    he will come with vengeance;(O)
with divine retribution
    he will come to save(P) you.”

Then will the eyes of the blind be opened(Q)
    and the ears of the deaf(R) unstopped.
Then will the lame(S) leap like a deer,(T)
    and the mute tongue(U) shout for joy.(V)
Water will gush forth in the wilderness
    and streams(W) in the desert.
The burning sand will become a pool,
    the thirsty ground(X) bubbling springs.(Y)
In the haunts where jackals(Z) once lay,
    grass and reeds(AA) and papyrus will grow.

And a highway(AB) will be there;
    it will be called the Way of Holiness;(AC)
    it will be for those who walk on that Way.
The unclean(AD) will not journey on it;
    wicked fools will not go about on it.
No lion(AE) will be there,
    nor any ravenous beast;(AF)
    they will not be found there.
But only the redeemed(AG) will walk there,
10     and those the Lord has rescued(AH) will return.
They will enter Zion with singing;(AI)
    everlasting joy(AJ) will crown their heads.
Gladness(AK) and joy will overtake them,
    and sorrow and sighing will flee away.(AL)