Add parallel Print Page Options

Tsoka kwa Efereimu

28 Tsoka ufumu wonyada wa zidakwa za ku Efereimu.
    Tsoka kwa ulemerero wake wokongola umene ukufota ngati duwa
limene lili pa mutu pa anthu
    oledzera a mʼchigwa chachonde.
Taonani, ambuye ali naye wina wamphamvu ndi nyonga.
    Iye adzabwera ngati mkuntho wamatalala ndi namondwe wowononga,
ngati madzi amphamvu osefukira a mvula yamkuntho;
    ndipo adzawagwetsa pansi mwankhanza.
Ulamuliro wa atsogoleri oledzera
    a ku Efereimu adzawuthetsa.
Ndipo ulemerero wokongola wa mzinda umene uli ngati duwa
    lofota pamutu pa anthu oledzera a mʼchigwa chachonde uja,
udzakhala ngati nkhuyu yoyambirira kupsa
    imene munthu akangoyiona amayithyola
    nthawi yokolola isanakwane.

Tsiku limenelo Yehova Wamphamvuzonse
    adzakhala ngati nkhata yaufumu,
chipewa chokongola
    kwa anthu ake otsala.
Iye adzapereka mtima
    wachilungamo kwa oweruza,
adzakhala chilimbikitso kwa
    amene amabweza adani pa zipata za mzinda.

Nawonso awa ali dzandidzandi chifukwa cha vinyo
    ndipo akusochera chifukwa cha mowa:
ansembe ndi aneneri akudzandira chifukwa cha mowa
    ndipo akusokonezeka chifukwa cha vinyo;
akusochera chifukwa cha mowa,
    akudzandira pamene akuona masomphenya,
    kupunthwa pamene akupereka chigamulo.
Pa matebulo onse pali masanzi okhaokha
    ndipo palibenso malo wopanda zonyansa.

Iwo akuti, “Kodi munthu ameneyu akufuna aphunzitse ndani?
    Uthengawu akufuna kufotokozera yani?
Ndi kwa ana amene aleka kuyamwa,
    kwa makanda ongowachotsa kumene ku bere?
10 Akuyesa kumatiphunzitsa pangʼonopangʼono
    lemba ndi lemba, mzere ndi mzere,
    phunziro ndi phunziro.
    Zonsezi akungoti apa pangʼono apa pangʼono.”

11 Mulungu adzayankhula kwa anthu ake kudzera mwa anthu aziyankhulo zachilendo, ziyankhulo zosamveka bwino.
    Mulungu adzayankhula kwa anthu awa, amene
12 anakuwuzani kuti,
    “Malo opumulira ndi ano,
otopa apumule, malo owusira ndi ano.”
    Koma inu simunamvere.
13 Choncho Yehova adzakuphunzitsani
    pangʼonopangʼono lemba ndi lemba,
    mzere ndi mzere, phunziro ndi phunziro.
    Kotero mudzayenda ndi kugwa chambuyo,
adzapweteka ndi kukodwa mu msampha
    ndipo adzakutengani ku ukapolo.

14 Nʼchifukwa chake imvani mawu a Yehova,
    inu anthu achipongwe amene mumalamulira anthu awa mu Yerusalemu.
15 Inu mumayankhula monyada kuti, “Ife tinachita pangano ndi imfa,
    ife tachita mgwirizano ndi manda.
Pamene mliri woopsa ukadzafika
    sudzatikhudza ife,
chifukwa timadalira bodza ngati pothawirapo pathu
    ndi chinyengo ngati malo anthu obisalapo.”

16 Tsono zimene Ambuye Yehova akunena ndi izi:

“Taonani, ndikuyika mwala wovomerezeka ndi amisiri
    ngati maziko mu Ziyoni,
mwala wapangodya, wamtengowapatali wopanga maziko amphamvu;
    munthu amene awukhulupirira sadzagwedezeka.
17 Ntchito zolungama zidzakhala ngati chingwe choyezera maziko ake,
    ndipo chilungamo chidzakhala chowongolera mzere;
matalala adzawononga malo anu othawirapo, amene ndi mabodza,
    ndipo madzi adzamiza malo anu obisalako.
18 Pangano limene munachita ndi imfa lidzathetsedwa;
    mgwirizano wanu ndi manda udzachotsedwa.
Pakuti mliri woopsa udzafika,
    ndipo udzakugonjetsani.
19 Ndipo ukadzangofika udzakutengani.
    Udzafika mmawa uliwonse,
    usiku ndi usana.”

Anthu akadzamvetsetsa uthenga umenewu
    adzaopsedwa kwambiri.
20 Mudzakhala ngati munthu wogona pa bedi lalifupi kwambiri kuti sangathe kutambalitsapo miyendo;
    ndiponso mudzakhala ngati munthu amene wafunda bulangeti lochepa kwambiri kuti sangathe nʼkufunda komwe.
21 Yehova adzamenya nkhondo monga anachitira ku phiri la Perazimu
    adzakalipa monga anachitira ku chigwa cha Gibiyoni;
adzagwira ntchito yake yooneka ngati yachilendo,
    ndipo zimene ati adzachite zidzakhala ngati zodabwitsa.
22 Tsopano lekani kunyoza,
    mukapanda kutero maunyolo anu adzakuthinani kwambiri;
Ambuye, Yehova Wamphamvuzonse wandiwuza kuti,
    “Ndagamula kuti ndidzawononga dziko lapansi.”

23 Tcherani khutu ndipo mumve mawu anga;
    mvetserani ndipo mumve zimene ndikunena.
24 Kodi mlimi wofuna kudzala mbewu amangokhalira kutipula kokhakokha?
    Kodi amangokhalira kugawula ndi kugalawuza kokhakokha?
25 Pamene iye wasalaza mundawo,
    kodi samafesa mawere ndi chitowe?
Kodi suja samadzala tirigu
    ndi barele mʼmizere yake,
    nadzala mchewere mʼphepete mwa mundawo?
26 Mulungu wake amamulangiza
    ndi kumuphunzitsa njira yabwino.

27 Mawere sapunthira chopunthira cha galeta lopanda mikombero,
    kapena chitowe sapuntha popondetsapo mikombero ya galeta;
mawere amapuntha ndi ndodo
    ndipo chitowe amapuntha ndi kamtengo.
28 Tirigu ayenera kusinjidwa kuti apangire buledi,
    komabe munthu samangokhalira kupuntha tiriguyo osalekeza, kuopa kuti angatekedzeke.
Ngakhale kuti amapuntha tiriguyo poyendetsapo mikombero ya galeta,
    koma akavalo ake satekedza tiriguyo.
29 Izinso zimachokera kwa Yehova Wamphamvuzonse,
    wa uphungu wodabwitsa ndi wa nzeru zopambana.

Woe to the Leaders of Ephraim and Judah

28 Woe(A) to that wreath, the pride of Ephraim’s(B) drunkards,
    to the fading flower, his glorious beauty,
set on the head of a fertile valley(C)
    to that city, the pride of those laid low by wine!(D)
See, the Lord has one who is powerful(E) and strong.
    Like a hailstorm(F) and a destructive wind,(G)
like a driving rain and a flooding(H) downpour,
    he will throw it forcefully to the ground.
That wreath, the pride of Ephraim’s(I) drunkards,
    will be trampled(J) underfoot.
That fading flower, his glorious beauty,
    set on the head of a fertile valley,(K)
will be like figs(L) ripe before harvest—
    as soon as people see them and take them in hand,
    they swallow them.

In that day(M) the Lord Almighty
    will be a glorious(N) crown,(O)
a beautiful wreath
    for the remnant(P) of his people.
He will be a spirit of justice(Q)
    to the one who sits in judgment,(R)
a source of strength
    to those who turn back the battle(S) at the gate.

And these also stagger(T) from wine(U)
    and reel(V) from beer:
Priests(W) and prophets(X) stagger from beer
    and are befuddled with wine;
they reel from beer,
    they stagger when seeing visions,(Y)
    they stumble when rendering decisions.
All the tables are covered with vomit(Z)
    and there is not a spot without filth.

“Who is it he is trying to teach?(AA)
    To whom is he explaining his message?(AB)
To children weaned(AC) from their milk,(AD)
    to those just taken from the breast?
10 For it is:
    Do this, do that,
    a rule for this, a rule for that[a];
    a little here, a little there.(AE)

11 Very well then, with foreign lips and strange tongues(AF)
    God will speak to this people,(AG)
12 to whom he said,
    “This is the resting place, let the weary rest”;(AH)
and, “This is the place of repose”—
    but they would not listen.
13 So then, the word of the Lord to them will become:
    Do this, do that,
    a rule for this, a rule for that;
    a little here, a little there(AI)
so that as they go they will fall backward;
    they will be injured(AJ) and snared and captured.(AK)

14 Therefore hear the word of the Lord,(AL) you scoffers(AM)
    who rule this people in Jerusalem.
15 You boast, “We have entered into a covenant with death,(AN)
    with the realm of the dead we have made an agreement.
When an overwhelming scourge sweeps by,(AO)
    it cannot touch us,
for we have made a lie(AP) our refuge
    and falsehood[b] our hiding place.(AQ)

16 So this is what the Sovereign Lord says:

“See, I lay a stone in Zion,(AR) a tested stone,(AS)
    a precious cornerstone for a sure foundation;(AT)
the one who relies on it
    will never be stricken with panic.(AU)
17 I will make justice(AV) the measuring line
    and righteousness the plumb line;(AW)
hail(AX) will sweep away your refuge, the lie,
    and water will overflow(AY) your hiding place.
18 Your covenant with death will be annulled;
    your agreement with the realm of the dead will not stand.(AZ)
When the overwhelming scourge sweeps by,(BA)
    you will be beaten down(BB) by it.
19 As often as it comes it will carry you away;(BC)
    morning after morning,(BD) by day and by night,
    it will sweep through.”

The understanding of this message
    will bring sheer terror.(BE)
20 The bed is too short to stretch out on,
    the blanket too narrow to wrap around you.(BF)
21 The Lord will rise up as he did at Mount Perazim,(BG)
    he will rouse himself as in the Valley of Gibeon(BH)
to do his work,(BI) his strange work,
    and perform his task, his alien task.
22 Now stop your mocking,(BJ)
    or your chains will become heavier;
the Lord, the Lord Almighty, has told me
    of the destruction decreed(BK) against the whole land.(BL)

23 Listen(BM) and hear my voice;
    pay attention and hear what I say.
24 When a farmer plows for planting,(BN) does he plow continually?
    Does he keep on breaking up and working the soil?
25 When he has leveled the surface,
    does he not sow caraway and scatter cumin?(BO)
Does he not plant wheat in its place,[c]
    barley(BP) in its plot,[d]
    and spelt(BQ) in its field?
26 His God instructs him
    and teaches(BR) him the right way.

27 Caraway is not threshed(BS) with a sledge,(BT)
    nor is the wheel of a cart rolled over cumin;
caraway is beaten out with a rod,(BU)
    and cumin with a stick.
28 Grain must be ground to make bread;
    so one does not go on threshing it forever.
The wheels of a threshing cart(BV) may be rolled over it,
    but one does not use horses to grind grain.
29 All this also comes from the Lord Almighty,
    whose plan is wonderful,(BW)
    whose wisdom is magnificent.(BX)

Footnotes

  1. Isaiah 28:10 Hebrew / sav lasav sav lasav / kav lakav kav lakav (probably meaningless sounds mimicking the prophet’s words); also in verse 13
  2. Isaiah 28:15 Or false gods
  3. Isaiah 28:25 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  4. Isaiah 28:25 The meaning of the Hebrew for this word is uncertain.