Add parallel Print Page Options

Za Munda Wamphesa wa Yehova

27 Tsiku limenelo,

Yehova ndi lupanga lake
    lakuthwa, lalikulu ndi lamphamvu,
adzalanga Leviyatani chinjoka chothawa chija,
    Leviyatani chinjoka chodzikulunga;
adzapha chirombo choopsa cha mʼnyanja.

Tsiku limenelo Yehova adzati,

“Tidzayimba nyimbo ya munda wamphesa wobereka bwino:
    Ine, Yehova, ndimawuyangʼanira;
    ndimawuthirira nthawi zonse.
Ndimawulondera usana ndi usiku
    kuti wina angawononge.
    Ine sindinakwiye.
Ngati mkandankhuku ndi minga zikanaoneka ndikanalimbana nazo!
    Ndikachita nazo nkhondo;
    ndikanazitentha zonse ndi moto.
Koma ngati apo ayi, abweretu kwa Ine adani angawo kuti ndidzawateteze;
    apangane nane za mtendere,
    ndithu, apangane nane za mtendere.”

Masiku akubwerawo Yakobo adzazika mizu,
    Israeli adzaphukira ndi kuchita maluwa,
    ndipo adzadzaza dziko lonse lapansi ndi zipatso.

Kodi Yehova anakantha Israeli
    ngati momwe anakanthira anthu amene anazunza Israeli?
Kapena kodi Yehova anapha Israeli
    ngati mmene anthu ena anaphera Israeli?
Yehova mwawalanga powapirikitsa ndi kuwatumiza ku ukapolo,
    mwawachotsa ndi mpweya wanu woopsa,
    monga zimachitikira pa tsiku la mkuntho wochokera kummawa.
Yehova adzakhululuka kulakwa kwa Yakobo.
    Iwo adzaonetsa kuti alapadi pamene adzaphwanya miyala yonse ya guwa lachikunja,
ngati mmene anthu amaphwanyira miyala yanjereza
    mpaka kukhala ngati fumbi lokhalokha.
Sipadzapezekanso mafano a Asera
    kapena maguwa ofukiza lubani.
10 Mzinda wamalinga uja wasanduka bwinja,
    wasanduka malo osiyidwa, ndi kutayidwa ngati chipululu;
kumeneko amadyetselako ana angʼombe
    kumeneko zimapumulako ziweto
    ndi kumwetula nthambi za mitengo kotheratu.
11 Pamene nthambi za mitengoyo zauma, zimathyoka
    ndipo amayi amabwera nazitola ndi kuzisandutsa nkhuni.
Pakuti awa ndi anthu opanda nzeru;
    kotero Mulungu amene anawapanga sadzachitira chisoni,
    ndipo Mlengi wawo sawakomera mtima.

12 Tsiku limenelo Yehova adzasonkhanitsa pamodzi anthu ake mmodzimmodzi kumalo opunthira tirigu, kuchokera ku mtsinje wa Yufurate mpaka ku mtsinje wa ku Igupto. 13 Ndipo tsiku limenelo lipenga lalikulu lidzalira. Amene akuzunzika ku Asiriya iwo amene ali ku ukapolo ku Igupto adzabwera ndi kudzalambira Yehova pa phiri lopatulika mu Yerusalemu.

Deliverance of Israel

27 In that day,(A)

the Lord will punish with his sword(B)
    his fierce, great and powerful sword—
Leviathan(C) the gliding serpent,(D)
    Leviathan the coiling serpent;
he will slay the monster(E) of the sea.

In that day(F)

“Sing(G) about a fruitful vineyard:(H)
    I, the Lord, watch over it;
    I water(I) it continually.
I guard(J) it day and night
    so that no one may harm(K) it.
    I am not angry.
If only there were briers and thorns confronting me!
    I would march against them in battle;
    I would set them all on fire.(L)
Or else let them come to me for refuge;(M)
    let them make peace(N) with me,
    yes, let them make peace with me.”

In days to come Jacob will take root,(O)
    Israel will bud and blossom(P)
    and fill all the world with fruit.(Q)

Has the Lord struck her
    as he struck(R) down those who struck her?
Has she been killed
    as those were killed who killed her?
By warfare[a] and exile(S) you contend with her—
    with his fierce blast he drives her out,
    as on a day the east wind(T) blows.
By this, then, will Jacob’s guilt be atoned(U) for,
    and this will be the full fruit of the removal of his sin:(V)
When he makes all the altar stones(W)
    to be like limestone crushed to pieces,
no Asherah poles[b](X) or incense altars(Y)
    will be left standing.
10 The fortified city stands desolate,(Z)
    an abandoned settlement, forsaken(AA) like the wilderness;
there the calves graze,(AB)
    there they lie down;(AC)
    they strip its branches bare.
11 When its twigs are dry, they are broken off(AD)
    and women come and make fires(AE) with them.
For this is a people without understanding;(AF)
    so their Maker has no compassion on them,
    and their Creator(AG) shows them no favor.(AH)

12 In that day the Lord will thresh(AI) from the flowing Euphrates to the Wadi of Egypt,(AJ) and you, Israel, will be gathered(AK) up one by one. 13 And in that day(AL) a great trumpet(AM) will sound. Those who were perishing in Assyria and those who were exiled(AN) in Egypt(AO) will come and worship(AP) the Lord on the holy mountain(AQ) in Jerusalem.

Footnotes

  1. Isaiah 27:8 See Septuagint; the meaning of the Hebrew for this word is uncertain.
  2. Isaiah 27:9 That is, wooden symbols of the goddess Asherah