Add parallel Print Page Options

Nyimbo ya Matamando

26 Tsiku limenelo anthu a mʼdziko la Yuda adzayimba nyimbo iyi.

Tili ndi mzinda wolimba.
    Mulungu amawuteteza ndi zipupa
    ndi malinga.
Tsekulani zipata za mzinda
    kuti mtundu wolungama
    ndi wokhulupirika ulowemo.
Inu mudzamupatsa munthu
    wa mtima wokhazikika
    mtendere weniweni.
Mudalireni Yehova mpaka muyaya,
    chifukwa Yehova Mulungu ndiye Thanthwe losatha.
Iye amatsitsa anthu amene amadziyika pamwamba,
    iye amagwetsa pansi mzinda wodzitukumula,
amagumula makoma ake
    ndi kuwagwetsa pansi pa fumbi penipeni.
Mapazi a anthu akuwupondereza,
    mapazi a anthu oponderezedwa,
    mapazi anthu osauka.

Njira ya munthu wolungama ndi yosalaza,
    Inu Wolungamayo, mumasalaza njira ya wolungama.
Inde Yehova, timayenda mʼnjira zanu zolungama,
    ife timayembekezera Inu;
mitima yathu imakhumba kukumbukira
    ndi kulemekeza dzina lanu.
Moyo wanga umalakalaka Inu usiku wonse;
    nthawi yammawa ndimafunafuna Inu.
Pamene muweruza dziko lapansi
    anthu amaphunzira kuchita chilungamo.
10 Ngakhale mukomere mtima anthu oyipa,
    saphunzira chilungamo.
Amachita zoyipa mʼdziko la chilungamo,
    ndipo sazindikira ululu wa Yehova.
11 Inu Yehova, mwatukula dzanja lanu kuti muwalange,
    koma iwo sakuliona dzanjalo.
Aloleni anthu aone ndi kuchita manyazi poona mmene mukondera anthu anu;
    ndipo moto umene mwasonkhera adani anu uwapsereze.

12 Yehova, mumatipatsa mtendere;
    ndipo zonse zimene ife tinazichita munatichitira ndinu.
13 Inu Yehova Mulungu wathu, ngakhale takhala tikulamulidwa ndi ena mʼmalo mwanu,
    koma ife timalemekeza dzina lanu lokha.
14 Iwo tsopano sadzadzukanso;
    mizimu yawo sidzabwera kudzativutitsa
pakuti mwawalanga ndipo mwawawononga;
    palibenso amene amawakumbukira.
15 Inu Yehova, mwaukulitsa mtundu wathu;
    mwauchulukitsa ndithu
ndipo mwalandirapo ulemu;
    mwaukuza mbali zonse za dziko.

16 Yehova, anthu anu anabwera kwa Inu pamene anali mʼmasautso;
    pamene munawalanga,
    iwo anapemphera kwa Inu.
17 Monga mayi woyembekezera pamene nthawi yake yobereka yayandikira
    amamva kupweteka ndipo amalira ndi ululu,
    ifenso tinali chimodzimodzi pamaso panu, Inu Yehova.
18 Ife chimodzimodzi tinamva ululu, ngati mayi pa nthawi yobala mwana,
    koma sitinapindulepo kanthu,
kapena kupulumutsa dziko lapansi;
    sitinabadwitse anthu atsopano pa dziko pano.

19 Koma anthu anu amene anafa adzakhalanso ndi moyo;
    matupi awo adzadzuka.
Iwo amene ali ku fumbi tsopano
    adzadzuka ndi kuyimba mosangalala.
Monga mame amafewetsa pansi kutsitsimutsa zomera,
    momwenso Yehova adzaukitsa anthu amene anafa kale.

20 Abale anga, pitani mukalowe mʼnyumba zanu
    ndipo mukadzitsekere;
mukabisale kwa kanthawi kochepa
    mpaka ukali wake utatha.
21 Taonani, Yehova akubwera kuchokera kumene amakhala;
    akubwera kudzalanga anthu a dziko lapansi chifukwa cha machimo awo.
Dziko lapansi lidzawulula magazi amene anakhetsedwa pa dzikolo;
    dziko lapansi silidzabisanso mitembo ya anthu ophedwa.

A Song of Praise

26 In that day(A) this song will be sung(B) in the land of Judah:

We have a strong city;(C)
    God makes salvation
    its walls(D) and ramparts.(E)
Open the gates(F)
    that the righteous(G) nation may enter,
    the nation that keeps faith.
You will keep in perfect peace(H)
    those whose minds are steadfast,
    because they trust(I) in you.
Trust(J) in the Lord forever,(K)
    for the Lord, the Lord himself, is the Rock(L) eternal.
He humbles those who dwell on high,
    he lays the lofty city low;
he levels it to the ground(M)
    and casts it down to the dust.(N)
Feet trample(O) it down—
    the feet of the oppressed,(P)
    the footsteps of the poor.(Q)

The path of the righteous is level;(R)
    you, the Upright One,(S) make the way of the righteous smooth.(T)
Yes, Lord, walking in the way of your laws,[a](U)
    we wait(V) for you;
your name(W) and renown
    are the desire of our hearts.
My soul yearns for you in the night;(X)
    in the morning my spirit longs(Y) for you.
When your judgments(Z) come upon the earth,
    the people of the world learn righteousness.(AA)
10 But when grace is shown to the wicked,(AB)
    they do not learn righteousness;
even in a land of uprightness they go on doing evil(AC)
    and do not regard(AD) the majesty of the Lord.
11 Lord, your hand is lifted high,(AE)
    but they do not see(AF) it.
Let them see your zeal(AG) for your people and be put to shame;(AH)
    let the fire(AI) reserved for your enemies consume them.

12 Lord, you establish peace(AJ) for us;
    all that we have accomplished you have done(AK) for us.
13 Lord our God, other lords(AL) besides you have ruled over us,
    but your name(AM) alone do we honor.(AN)
14 They are now dead,(AO) they live no more;
    their spirits(AP) do not rise.
You punished them and brought them to ruin;(AQ)
    you wiped out all memory of them.(AR)
15 You have enlarged the nation, Lord;
    you have enlarged the nation.(AS)
You have gained glory for yourself;
    you have extended all the borders(AT) of the land.

16 Lord, they came to you in their distress;(AU)
    when you disciplined(AV) them,
    they could barely whisper(AW) a prayer.[b]
17 As a pregnant woman about to give birth(AX)
    writhes and cries out in her pain,
    so were we in your presence, Lord.
18 We were with child, we writhed in labor,
    but we gave birth(AY) to wind.
We have not brought salvation(AZ) to the earth,
    and the people of the world have not come to life.(BA)

19 But your dead(BB) will live, Lord;
    their bodies will rise—
let those who dwell in the dust(BC)
    wake up and shout for joy—
your dew(BD) is like the dew of the morning;
    the earth will give birth to her dead.(BE)

20 Go, my people, enter your rooms
    and shut the doors(BF) behind you;
hide(BG) yourselves for a little while
    until his wrath(BH) has passed by.(BI)
21 See, the Lord is coming(BJ) out of his dwelling(BK)
    to punish(BL) the people of the earth for their sins.
The earth will disclose the blood(BM) shed on it;
    the earth will conceal its slain no longer.

Footnotes

  1. Isaiah 26:8 Or judgments
  2. Isaiah 26:16 The meaning of the Hebrew for this clause is uncertain.