Yesaya 16
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
16 Anthu a ku Mowabu
atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa,
kuchokera ku Sela kudutsa chipululu
mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku
akazimwaza mʼchisa,
momwemonso akazi a ku Mowabu
akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti,
“Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite.
Inu mutiteteze kwa adani anthu.
Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo.
Mutibise,
musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu;
mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.”
Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso,
kuwononga kudzaleka;
waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi;
mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika.
Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo
ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri.
Kunyada kwawo
ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo,
zonse ndi zopanda phindu.
7 Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri;
iwo akulirira dziko lawo.
Akubuma momvetsa chisoni
chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 Minda ya ku Hesiboni yauma,
minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga.
Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda
minda ya mpesa wabwino,
imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri,
mpaka kutambalalira ku chipululu.
Mizu yake inakafika
mpaka ku tsidya la nyanja.
9 Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri,
chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima.
Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali,
ndikukunyowetsani ndi misozi!
Mwalephera kupeza zokolola,
chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso;
palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa;
palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa,
pakuti ndathetsa kufuwula.
11 Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu,
mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 Ngakhale anthu a ku Mowabu
apite ku malo awo achipembedzo
koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe
chifukwa sizidzatheka.
13 Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu. 14 Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”
Isaiah 16
New International Version
16 Send lambs(A) as tribute(B)
to the ruler of the land,
from Sela,(C) across the desert,
to the mount of Daughter Zion.(D)
2 Like fluttering birds
pushed from the nest,(E)
so are the women of Moab(F)
at the fords(G) of the Arnon.(H)
3 “Make up your mind,” Moab says.
“Render a decision.
Make your shadow like night—
at high noon.
Hide the fugitives,(I)
do not betray the refugees.
4 Let the Moabite fugitives stay with you;
be their shelter(J) from the destroyer.”
The oppressor(K) will come to an end,
and destruction will cease;(L)
the aggressor will vanish from the land.
5 In love a throne(M) will be established;(N)
in faithfulness a man will sit on it—
one from the house[a] of David(O)—
one who in judging seeks justice(P)
and speeds the cause of righteousness.
6 We have heard of Moab’s(Q) pride(R)—
how great is her arrogance!—
of her conceit, her pride and her insolence;
but her boasts are empty.
7 Therefore the Moabites wail,(S)
they wail together for Moab.
Lament and grieve
for the raisin cakes(T) of Kir Hareseth.(U)
8 The fields of Heshbon(V) wither,(W)
the vines of Sibmah(X) also.
The rulers of the nations
have trampled down the choicest vines,(Y)
which once reached Jazer(Z)
and spread toward the desert.
Their shoots spread out(AA)
and went as far as the sea.[b](AB)
9 So I weep,(AC) as Jazer weeps,
for the vines of Sibmah.
Heshbon and Elealeh,(AD)
I drench you with tears!(AE)
The shouts of joy(AF) over your ripened fruit
and over your harvests(AG) have been stilled.
10 Joy and gladness are taken away from the orchards;(AH)
no one sings or shouts(AI) in the vineyards;
no one treads(AJ) out wine at the presses,(AK)
for I have put an end to the shouting.
11 My heart laments for Moab(AL) like a harp,(AM)
my inmost being(AN) for Kir Hareseth.
12 When Moab appears at her high place,(AO)
she only wears herself out;
when she goes to her shrine(AP) to pray,
it is to no avail.(AQ)
13 This is the word the Lord has already spoken concerning Moab. 14 But now the Lord says: “Within three years,(AR) as a servant bound by contract(AS) would count them,(AT) Moab’s splendor and all her many people will be despised,(AU) and her survivors will be very few and feeble.”(AV)
Footnotes
- Isaiah 16:5 Hebrew tent
- Isaiah 16:8 Probably the Dead Sea
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.