Add parallel Print Page Options

Uthenga Wonena za Babuloni

50 Uthenga umene Yehova anayankhula ndi mneneri Yeremiya wonena za mzinda wa Babuloni ndi anthu ake ndi uwu:

“Lengeza ndi kulalika pakati pa anthu a mitundu ina,
    kweza mbendera ndipo ulengeze;
    usabise kanthu, koma uwawuze kuti,
‘Babuloni wagwa;
    mulungu wawo Beli wachititsidwa manyazi,
    nayenso Mariduku wagwidwa ndi mantha.
Milungu yake yagwidwa ndi mantha
    ndipo mafano ake adzagwidwa ndi mantha.’
Mtundu wa anthu wochokera kumpoto wadzathira nkhondo Babuloni
    ndi kusandutsa bwinja dziko lake.
Kumeneko sikudzakhalanso
    munthu kapena nyama.

“Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
    akutero Yehova,
“anthu a ku Israeli ndi anthu a ku Yuda
    onse pamodzi adzabwera akulira. Adzafunitsitsa kuchita zimene Yehova Mulungu wawo akufuna.
Adzafunsa njira ya ku Ziyoni
    ndi kuyamba ulendo wopita kumeneko.
Iwo adzadzipereka kwa Yehova
    pochita naye pangano lamuyaya
    limene silidzayiwalika.

“Anthu anga ali ngati nkhosa zotayika;
    abusa awo
    anawasocheretsa mʼmapiri.
Iwo anayendayenda mʼmapiri ndi mʼzitunda
    mpaka kuyiwala kwawo.
Aliyense amene anawapeza anawawononga;
    adani awo anati, ‘Ife si olakwa,
chifukwa iwo anachimwira Yehova, amene ali mpumulo wawo weniweni
    ndi amene makolo awo anamukhulupirira.’

“Thawaniko ku Babuloni;
    chokani mʼdziko la Ababuloni.
    Muyambe inu kutuluka ngati atonde amene amatsogolera ziweto.
Taonani, ndidzaukitsa gulu lankhondo lamphamvu la mitundu ina
    ndi kubwera nalo kuchokera kumpoto
kudzamenyana ndi Babuloni.
    Iwo adzandandalika ankhondo awo ndi kugonjetsa Babuloni.
Mivi yawo ili ngati ya ankhondo aluso,
    yosapita padera.
10 Motero Ababuloni adzafunkhidwa;
    ndipo onse omufunkha adzakhuta,”
            akutero Yehova.

11 “Inu Ababuloni, munawononga anthu anga osankhika.
    Ndiye pano mukukondwa, mukusangalala.
Mukulumphalumpha mokondwa ngati mwana wangʼombe wopuntha tirigu
    ndiponso mukulira monyada ngati ngʼombe zazimuna.
12 Koma mzinda wanu udzachititsidwa manyazi kwambiri.
    Mzinda umene uli ngati mayi wanu udzanyazitsidwa.
Babuloni adzasanduka chitsirizira cha anthu onse.
    Mzinda wawo udzakhala ngati thengo, ngati dziko lowuma lachipululu.
13 Chifukwa cha mkwiyo wa Yehova Babuloni adzakhala wopanda anthu
    ndipo adzakhala chipululu chokhachokha.
Onse odutsa kumeneko adzachita mantha ndipo azidzangotsonya
    chifukwa cha chiwonongeko chake chachikulu.

14 “Inu okoka uta,
    konzekani kuti muthire nkhondo mzinda wa Babuloni mbali zonse.
Muponyereni mivi yanu yonse
    chifukwa anachimwira Yehova.
15 Mufuwulireni mbali zonse pakuti wagonja.
    Nsanja zake zagwa.
    Malinga ake agwetsedwa.
Kumeneku ndiko kulipsira kwa Yehova.
    Mulipsireni,
    mumuchite zomwe iye anachitira anthu ena.
16 Chotsani ku Babuloni munthu wofesa mbewu aliyense,
    ndiponso wodula tirigu ndi chikwakwa chake pa nthawi yokolola.
Poona lupanga la ozunza anzawo,
    aliyense adzabwerera kwa anthu ake;
    adzathawira ku dziko la kwawo.

17 “Aisraeli ali ngati nkhosa zomwe zabalalika
    pothamangitsidwa ndi mikango.
Mfumu ya ku Asiriya ndiye inayamba kuwapha Aisraeliwo.
    Wotsiriza anali Nebukadinezara
mfumu ya ku Babuloni
    amene anachita ngati kuphwanya mafupa ake.”

18 Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti,

“Ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi dziko lake
    monga momwe ndinalangira mfumu ya ku Asiriya.
19 Koma ndidzabwezera Israeli ku msipu wake
    ndipo adzadya mʼminda ya ku Karimeli ndi Basani;
adzadya nakhuta ku mapiri
    a ku Efereimu ndi Giliyadi.
20 Masiku amenewo, nthawi imeneyo,”
    akutero Yehova,
“anthu adzafunafuna zolakwa za Israeli
    koma sadzapeza nʼchimodzi chomwe,
ndipo adzafufuza machimo a Yuda,
    koma sadzapeza ndi limodzi lomwe,
    chifukwa otsala amene ndawasiya ndidzawakhululukira.

21 “Lithireni nkhondo dziko la Merataimu
    ndi anthu okhala ku Pekodi.
Muwaphe ndi lupanga ndi kuwawonongeratu,”
            akutero Yehova.
    “Chitani zonse monga momwe ndakulamulani.
22 Mʼdziko muli phokoso la nkhondo,
    phokoso la chiwonongeko chachikulu!
23 Taonani mʼmene waphwanyikira ndi kuwonongekera
    uja amati ndi nyundo ya dziko lonse lapansi.
Mzinda wa Babuloni wasanduka chinthu chochititsa mantha
    pakati pa mitundu ina!
24 Ndinakutchera msampha, iwe Babuloni,
    ndipo wakodwamo iwe wosazindikira kanthu;
unapezeka ndiponso unakodwa
    chifukwa unalimbana ndi Yehova.
25 Yehova watsekula nyumba ya zida zake
    ndipo watulutsa zida za ukali wake,
pakuti Ambuye Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ntchito yoti agwire
    mʼdziko la Ababuloni.
26 Mumenyane naye Babuloni mbali zonse.
    Anthu ake muwawunjike
    ngati milu ya tirigu.
Muwawononge kotheratu
    ndipo pasakhale wopulumuka ndi mmodzi yemwe.
27 Iphani ankhondo ake onse.
    Onse aphedwe ndithu.
Tsoka lawagwera
    pakuti tsiku lawo lachilango lafika.
28 Tikumva anthu othawa nkhondo ochokera ku Babuloni
    akulengeza mu Yerusalemu
za kulipsira kwa Yehova Mulungu wathu.
    Iye akulipsira chifukwa chowononga Nyumba yake.

29 “Itanani anthu oponya mivi kudzathira nkhondo Babuloni.
    Muyitanenso onse amene amakoka mauta.
Mangani misasa ya nkhondo momuzungulira;
    musalole munthu aliyense kuthawa.
Muchiteni monga momwe
    iye anachitira anthu ena.
Iyeyu ananyoza
    Yehova, Woyera wa Israeli.
30 Nʼchifukwa chake, anyamata ake adzaphedwa mʼmabwalo ake;
    ankhondo ake onse adzaphedwa tsiku limenelo,”
            akutero Yehova.
31 “Taona, ndikukuthira nkhondo, iwe wodzikuzawe,”
    akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse,
“chifukwa tsiku lako lafika,
    nthawi yoti ndikulange yakwana.
32 Wodzikuzawe udzapunthwa nʼkugwa
    ndipo palibe amene adzakudzutse;
ndidzayatsa moto mʼmizinda yake
    umene udzanyeketsa onse amene amuzungulira.”

33 Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Anthu a ku Israeli akuzunzidwa,
    pamodzi ndi anthu a ku Yuda,
ndipo onse amene anawagwira ukapolo awagwiritsitsa,
    akukana kuwamasula.
34 Koma Mpulumutsi wawo ndi wamphamvu;
    dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
Iye adzawateteza molimba pa mlandu wawo
    nʼcholinga choti abweretse mtendere mʼdziko lawo,
    koma adzavutitsa okhala ku Babuloni.”

35 Yehova akuti,
    “Imfa yalunjika pa Ababuloni,
pa akuluakulu ake
    ndi pa anthu ake a nzeru!
36 Imfa yalunjika pa aneneri abodza
    kuti asanduke zitsiru.
Imfa yalunjika pa ankhondo ake
    kuti agwidwe ndi mantha aakulu.
37 Imfa ilunjike pa akavalo ake ndi magaleta ake.
    Ilunjikanso pa magulu ankhondo achilendo amene ali pakati pawo
    kuti asanduke ngati akazi.
Chiwonongeko chilunjikenso pa chuma chake
    kuti chidzafunkhidwe.
38 Chilala chilunjike pa madzi ake
    kuti aphwe.
Babuloni ndi dziko la mafano,
    ndipo anthu afika poyaluka nawo mafanowo.

39 “Nʼchifukwa chake nyama zakuthengo ndi afisi zidzakhala kumeneko
    ndipo kudzakhalanso akadzidzi.
Kumeneko sikudzapezekako anthu,
    ndithu anthu sadzakhalako pa mibado yonse.
40 Monga momwe Mulungu anawonongera Sodomu ndi Gomora
    pamodzi ndi mizinda yonse yozungulira,”
            akutero Yehova,
“momwemonso palibe amene adzakhale kumeneko;
    anthu sadzayendanso mʼmenemo.

41 “Taonani! Gulu lankhondo likubwera kuchokera kumpoto;
    mtundu wa anthu amphamvu pamodzi ndi mafumu ambiri,
    wanyamuka kuchokera kumathero a dziko lapansi.
42 Atenga mauta ndi mikondo;
    ndi anthu ankhanza ndipo alibe chifundo.
Phokoso lawo likumveka ngati mkokomo wa nyanja.
    Akwera pa akavalo awo,
ndipo akonzekera kudzakuthira nkhondo
    iwe Babuloni.
43 Mfumu ya ku Babuloni yamva za mbiri yawo,
    ndipo yalobodokeratu.
Ikuda nkhawa,
    ikumva ululu ngati wa mayi pa nthawi yake yochira.
44 Taonani, monga mkango wochokera ku nkhalango ya ku Yorodani
    kupita ku msipu wobiriwira,
momwemonso ine ndidzapirikitsa Babuloni mʼdziko lake mwadzidzidzi.
    Pambuyo pake ndidzawayikira wowalamulira amene ndamufuna Ine.
Wofanana nane ndani ndipo ndani amene angalimbane nane?
    Ndi mtsogoleri wa dziko uti amene anganditengere ku bwalo la milandu?”
45 Nʼchifukwa chake imvani.
    Izi ndi zimene Ine Yehova ndakonza zolangira anthu a ku Babuloni.
Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo
    ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
46 Akadzagwa Babuloni padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera,
    ndipo kulira kwawo kudzamveka pakati pa mitundu yonse ya anthu.

A Message About Babylon(A)

50 This is the word the Lord spoke through Jeremiah the prophet concerning Babylon(B) and the land of the Babylonians[a]:

“Announce and proclaim(C) among the nations,
    lift up a banner(D) and proclaim it;
    keep nothing back, but say,
‘Babylon will be captured;(E)
    Bel(F) will be put to shame,(G)
    Marduk(H) filled with terror.
Her images will be put to shame
    and her idols(I) filled with terror.’
A nation from the north(J) will attack her
    and lay waste her land.
No one will live(K) in it;
    both people and animals(L) will flee away.

“In those days, at that time,”
    declares the Lord,
“the people of Israel and the people of Judah together(M)
    will go in tears(N) to seek(O) the Lord their God.
They will ask the way(P) to Zion
    and turn their faces toward it.
They will come(Q) and bind themselves to the Lord
    in an everlasting covenant(R)
    that will not be forgotten.

“My people have been lost sheep;(S)
    their shepherds(T) have led them astray(U)
    and caused them to roam on the mountains.
They wandered over mountain and hill(V)
    and forgot their own resting place.(W)
Whoever found them devoured(X) them;
    their enemies said, ‘We are not guilty,(Y)
for they sinned against the Lord, their verdant pasture,
    the Lord, the hope(Z) of their ancestors.’

“Flee(AA) out of Babylon;(AB)
    leave the land of the Babylonians,
    and be like the goats that lead the flock.
For I will stir(AC) up and bring against Babylon
    an alliance of great nations(AD) from the land of the north.(AE)
They will take up their positions against her,
    and from the north she will be captured.(AF)
Their arrows(AG) will be like skilled warriors
    who do not return empty-handed.
10 So Babylonia[b] will be plundered;(AH)
    all who plunder her will have their fill,”
declares the Lord.

11 “Because you rejoice and are glad,
    you who pillage my inheritance,(AI)
because you frolic like a heifer(AJ) threshing grain
    and neigh like stallions,
12 your mother will be greatly ashamed;
    she who gave you birth will be disgraced.(AK)
She will be the least of the nations—
    a wilderness, a dry land, a desert.(AL)
13 Because of the Lord’s anger she will not be inhabited
    but will be completely desolate.(AM)
All who pass Babylon will be appalled;(AN)
    they will scoff(AO) because of all her wounds.(AP)

14 “Take up your positions around Babylon,
    all you who draw the bow.(AQ)
Shoot at her! Spare no arrows,(AR)
    for she has sinned against the Lord.
15 Shout(AS) against her on every side!
    She surrenders, her towers fall,
    her walls(AT) are torn down.
Since this is the vengeance(AU) of the Lord,
    take vengeance on her;
    do to her(AV) as she has done to others.(AW)
16 Cut off from Babylon the sower,
    and the reaper with his sickle at harvest.
Because of the sword(AX) of the oppressor
    let everyone return to their own people,(AY)
    let everyone flee to their own land.(AZ)

17 “Israel is a scattered flock(BA)
    that lions(BB) have chased away.
The first to devour(BC) them
    was the king(BD) of Assyria;
the last to crush their bones(BE)
    was Nebuchadnezzar(BF) king(BG) of Babylon.”

18 Therefore this is what the Lord Almighty, the God of Israel, says:

“I will punish the king of Babylon and his land
    as I punished the king(BH) of Assyria.(BI)
19 But I will bring(BJ) Israel back to their own pasture,
    and they will graze on Carmel and Bashan;
their appetite will be satisfied(BK)
    on the hills(BL) of Ephraim and Gilead.(BM)
20 In those days, at that time,”
    declares the Lord,
“search will be made for Israel’s guilt,
    but there will be none,(BN)
and for the sins(BO) of Judah,
    but none will be found,
    for I will forgive(BP) the remnant(BQ) I spare.

21 “Attack the land of Merathaim
    and those who live in Pekod.(BR)
Pursue, kill and completely destroy[c] them,”
declares the Lord.
    “Do everything I have commanded you.
22 The noise(BS) of battle is in the land,
    the noise of great destruction!
23 How broken and shattered
    is the hammer(BT) of the whole earth!(BU)
How desolate(BV) is Babylon
    among the nations!
24 I set a trap(BW) for you, Babylon,
    and you were caught before you knew it;
you were found and captured(BX)
    because you opposed(BY) the Lord.
25 The Lord has opened his arsenal
    and brought out the weapons(BZ) of his wrath,
for the Sovereign Lord Almighty has work to do
    in the land of the Babylonians.(CA)
26 Come against her from afar.(CB)
    Break open her granaries;
    pile her up like heaps of grain.(CC)
Completely destroy(CD) her
    and leave her no remnant.
27 Kill all her young bulls;(CE)
    let them go down to the slaughter!(CF)
Woe to them! For their day(CG) has come,
    the time(CH) for them to be punished.
28 Listen to the fugitives(CI) and refugees from Babylon
    declaring in Zion(CJ)
how the Lord our God has taken vengeance,(CK)
    vengeance for his temple.(CL)

29 “Summon archers against Babylon,
    all those who draw the bow.(CM)
Encamp all around her;
    let no one escape.(CN)
Repay(CO) her for her deeds;(CP)
    do to her as she has done.
For she has defied(CQ) the Lord,
    the Holy One(CR) of Israel.
30 Therefore, her young men(CS) will fall in the streets;
    all her soldiers will be silenced in that day,”
declares the Lord.
31 “See, I am against(CT) you, you arrogant one,”
    declares the Lord, the Lord Almighty,
“for your day(CU) has come,
    the time for you to be punished.
32 The arrogant(CV) one will stumble and fall(CW)
    and no one will help her up;(CX)
I will kindle a fire(CY) in her towns
    that will consume all who are around her.”

33 This is what the Lord Almighty says:

“The people of Israel are oppressed,(CZ)
    and the people of Judah as well.
All their captors hold them fast,
    refusing to let them go.(DA)
34 Yet their Redeemer(DB) is strong;
    the Lord Almighty(DC) is his name.
He will vigorously defend their cause(DD)
    so that he may bring rest(DE) to their land,
    but unrest to those who live in Babylon.

35 “A sword(DF) against the Babylonians!”(DG)
    declares the Lord
“against those who live in Babylon
    and against her officials and wise(DH) men!
36 A sword against her false prophets!
    They will become fools.
A sword against her warriors!(DI)
    They will be filled with terror.(DJ)
37 A sword against her horses and chariots(DK)
    and all the foreigners in her ranks!
    They will become weaklings.(DL)
A sword against her treasures!(DM)
    They will be plundered.
38 A drought on[d] her waters!(DN)
    They will dry(DO) up.
For it is a land of idols,(DP)
    idols that will go mad with terror.

39 “So desert creatures(DQ) and hyenas will live there,
    and there the owl will dwell.
It will never again be inhabited
    or lived in from generation to generation.(DR)
40 As I overthrew Sodom and Gomorrah(DS)
    along with their neighboring towns,”
declares the Lord,
“so no one will live there;
    no people will dwell in it.(DT)

41 “Look! An army is coming from the north;(DU)
    a great nation and many kings
    are being stirred(DV) up from the ends of the earth.(DW)
42 They are armed with bows(DX) and spears;
    they are cruel(DY) and without mercy.(DZ)
They sound like the roaring sea(EA)
    as they ride on their horses;
they come like men in battle formation
    to attack you, Daughter Babylon.(EB)
43 The king of Babylon has heard reports about them,
    and his hands hang limp.(EC)
Anguish has gripped him,
    pain like that of a woman in labor.(ED)
44 Like a lion coming up from Jordan’s thickets(EE)
    to a rich pastureland,
I will chase Babylon from its land in an instant.
    Who is the chosen(EF) one I will appoint for this?
Who is like me and who can challenge me?(EG)
    And what shepherd can stand against me?”

45 Therefore, hear what the Lord has planned against Babylon,
    what he has purposed(EH) against the land of the Babylonians:(EI)
The young of the flock will be dragged away;
    their pasture will be appalled at their fate.
46 At the sound of Babylon’s capture the earth will tremble;(EJ)
    its cry(EK) will resound among the nations.

Footnotes

  1. Jeremiah 50:1 Or Chaldeans; also in verses 8, 25, 35 and 45
  2. Jeremiah 50:10 Or Chaldea
  3. Jeremiah 50:21 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them; also in verse 26.
  4. Jeremiah 50:38 Or A sword against