Add parallel Print Page Options

Uthenga Wonena za Aamoni

49 Yehova ananena izi:

Amoni,

“Kodi Israeli alibe ana aamuna?
    Kapena alibe mlowamʼmalo?
Tsono nʼchifukwa chiyani anthu opembedza Moleki alanda dziko la Gadi?
    Nʼchifukwa chiyani anthu ake akukhala mʼmizinda ya Gadi?
Koma nthawi ikubwera,”
    akutero Yehova,
“pamene ndidzamveketse mfuwu wankhondo
    ku Raba, likulu la Amoni;
ndipo malo awo opembedzera milungu yawo
    adzatenthedwa ndi moto.
Choncho Aisraeli adzalandanso dziko lawo
    kuchokera kwa amene anawalanda poyamba dzikolo,”
            akutero Yehova.
“Lirani, inu anthu a ku Hesiboni chifukwa wowononga uja wafika!
    Fuwulani, inu anthu okhala ku Raba!
Valani ziguduli ndi kulira mwamphamvu;
    thamangani uku ndi uku mʼkati mwa malinga,
chifukwa mulungu wanu Moleki adzapita ku ukapolo,
    pamodzi ndi ansembe ake ndiponso akuluakulu ake.
Chifukwa chiyani mukunyadira
    chigwa chanu,
inu anthu osakhulupirika
    amene munadalira chuma chanu nʼkumati:
    ‘Ndani angandithire nkhondo?’
Ndidzabweretsa zoopsa pa iwe
    zochokera kwa onse amene akuzungulira,”
            akutero Ambuye, Mulungu Wamphamvuzonse.
“Mudzathawa, ndipo aliyense adzathawitsa moyo wake.
    Sipadzapezeka munthu wosonkhanitsanso othawawo.

“Komabe pambuyo pake, ndidzabwezera kwawo Aamoni,”
            akutero Yehova.

Uthenga Wonena za Edomu

Yehova Wamphamvuzonse ananena izi za Edomu:

“Kodi nzeru sizikupezekanso ku Temani?
    Kodi anzeru analeka kupereka uphungu?
    Kodi nzeru zawo zinatheratu?
Inu anthu a ku Dedani, thawani,
    bwererani ndi kukabisala ku makwalala
chifukwa ndidzagwetsa mavuto pa zidzukulu za Esau
    popeza nthawi yawo ya chiweruzo yafika.
Kodi anthu othyola mphesa akanafika kwa inu
    akanakusiyiraniko mphesa pangʼono pokha?
Anthu akuba akanafika usiku
    akanangotengako zimene akuzifuna zokha?
10 Koma ine ndazivula zidzukulu za Esau.
    Ndaonetsa poyera malo awo obisalamo,
    kotero kuti sadzathanso kubisala.
Ana ake, abale ake pamodzi ndi anansi ake awonongeka.
    Palibe wonena kuti,
11 ‘Siyani ana anu amasiye; Ine ndidzawateteza.
    Amayi anu amasiye akhoza kudalira Ine.’ ”

12 Yehova akuti, “Ngati iwo amene sanali oyenera kulangidwa adzamwa chikho cha chiweruzo, ndiye muyesa kuti inuyo simudzalangidwa? Ayi ndithu simudzakhala osalangidwa. Mudzamwa ndithu chikhocho. 13 Ine ndikulumbira, akutero Yehova, kuti mzinda wa Bozira udzasanduka bwinja, chinthu chochititsa mantha, chomachiseka ndiponso chotembereredwa. Mizinda yake yonse idzakhala mabwinja mpaka muyaya.”

14 Ndamva uthenga wochokera kwa Yehova:
    Nthumwi yatumidwa kupita kwa anthu a mitundu ina kukanena kuti,
“Sonkhanani pamodzi kuti muthire nkhondo Edomu!
    Konzekerani nkhondo!”

15 “Ndidzakuchepetsani pakati pa anthu a mitundu ina.
    Mudzakhala anthu onyozeka pakati pa anthu.
16 Kuopseza kwako kwakunyenga;
    kudzikuza kwa mtima wako kwakusocheretsa,
iwe amene umakhala mʼmapanga
    a mʼmatanthwe ndi mʼmapiri.
Ngakhale utamanga chisa chako pamwamba kwambiri ngati chiwombankhanga,
    ndidzakutsitsa pansi kuchokera kumeneko,”
            akutero Yehova.
17 “Dziko la Edomu lidzasanduka chinthu chochititsa mantha.
    Onse odutsamo adzadabwa ndi kupukusa mitu yawo
    chifukwa cha kuwonongeka kwake.
18 Monga momwe anawonongekera Sodomu ndi Gomora,
    pamodzi ndi mizinda yake yozungulira,”
            akutero Yehova,
“motero palibe munthu
    amene adzakhala mu Edomu.

19 “Monga mkango wotuluka ku nkhalango za ku Yorodani
    kupita ku malo a msipu wobiriwira,
Ine ndidzapirikitsa anthu a ku Edomu mwadzidzidzi kuchoka mʼdziko lawo.
    Pambuyo pake ndidzawayikira owalamulira amene ndamufuna Ine.
Kodi ndani wofanana nane, ndipo angatsutsane nane ndani?
    Ndipo ndi mʼbusa uti amene angalimbane nane?”
20 Nʼchifukwa chake imvani. Izi ndi zimene Ine Yehova
    ndakonza zolangira anthu a ku Edomu ndi a ku Temani.
Ngakhale ana omwe adzatengedwa ukapolo
    ndipo aliyense adzachita mantha chifukwa cha iwo.
21 Akadzagwa Edomu padzakhala mfuwu waukulu ndipo dziko lapansi lidzanjenjemera;
    kulira kwawo kudzamveka mpaka ku Nyanja Yofiira.
22 Taonani, mtundu wina udzachita kuwuluka
    nʼkudzatera pa Bozira ngati chiwombankhanga chimene chatambalitsa mapiko ake.
Pa tsiku limenelo mitima ya ankhondo a ku Edomu
    idzagunda ngati mtima wa mayi pa nthawi yake yochira.

Uthenga Wonena za Damasiko

23 Mawu a Yehova onena za Damasiko ndi awa:

“Anthu a ku Hamati ndi a ku Aripadi akuchita mantha
    chifukwa amva nkhani yoyipa.
Mitima yawo yagwidwa ndi mantha
    ndipo ali ngati muja ichitira nyanja yosakhazikika.
24 Anthu a ku Damasiko alefuka.
    Abwerera mʼmbuyo kufuna kuthawa
    chifukwa agwidwa ndi mantha aakulu.
Ali ndi nkhawa komanso mantha
    ngati za mayi pa nthawi yake yochira.
25 Mzinda wotchuka
    ndi wachikondwerero uja wasiyidwa!
26 Nʼchifukwa chake anyamata ake adzagwa mʼmisewu ndi kufa;
    ankhondo ake onse adzawonongedwa tsiku limenelo,”
            akutero Yehova Wamphamvuzonse.
27 “Ndidzatentha malinga a Damasiko;
    moto udzanyeketsa nyumba zaufumu za Beni-Hadadi.”

Uthenga Wonena za Kedara ndi Hazori

28 Mawu a Yehova onena za Kedara ndi maufumu a ku Hazori, amene Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anawagonjetsa ndi awa:

“Nyamukani mukathire nkhondo ku Kedara.
    Kawonongeni anthu a kummawako.
29 Landani matenti awo ndi nkhosa zawo,
    ndiye kuti, mutenge nsalu zawo ndi katundu wawo.
    Mutengenso ngamira zawo.
Anthu adzafuwula kwa iwo kuti,
    ‘Kuli zoopsa mbali zonse!’

30 “Thawani mofulumira!
    Kabisaleni mʼmakhwawa, inu anthu ku Hazori,”
            akutero Yehova.
“Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni wakukonzerani chiwembu;
    wakonzekera zoti alimbane nanu.

31 “Nyamukani kathireni nkhondo mtundu wa anthu umene uli pamtendere,
    umene ukukhala mosatekeseka,”
            akutero Yehova,
“mzindawo ulibe zipata ngakhalenso mipiringidzo;
    anthu ake amakhala pa okha.
32 Ngamira zawo zidzafunkhidwa,
    ndipo makola a ngʼombe zawo adzalandidwa.
Ndidzabalalitsira ku mphepo zinayi onse amene amameta tsitsi lawo chamʼmbali.
    Ndidzawagwetsera mavuto kuchokera ku mbali zonse,”
            akutero Yehova.
33 “Hazori adzasanduka bwinja,
    malo okhalamo nkhandwe
mpaka muyaya.
    Palibe munthu amene adzayendemo.”

Uthenga Wonena za Elamu

34 Uthenga umene Yehova anapatsa mneneri Yeremiya wonena za Elamu, Zedekiya mfumu ya Yuda atangoyamba kulamulira ndi uwu:

35 Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani, ndidzathyola uta wa Elamu,
    umene uli chida chawo champhamvu.
36 Ndidzabweretsa mphepo zinayi pa Elamu
    kuchokera ku zigawo zinayi zamlengalenga;
ndidzawabalalitsira ku mphepo zinayi,
    ndipo sipadzakhala dziko
    limene anthu a ku Elamu sadzafikako.
37 A ku Elamuwo ndidzachititsa mantha pamaso pa adani awo
    komanso pamaso pa iwo amene akufuna kuwononga moyo wawo.
Ndidzawagwetsera mkwiyo wanga
    ndipo adzakhala pa mavuto,”
            akutero Yehova.
“Ndidzawapirikitsa ndi lupanga
    mpaka nditawatheratu.
38 Ndidzakhazika mpando wanga waufumu ku Elamu
    ndipo ndidzawononga mfumu yake pamodzi ndi akuluakulu ake,”
            akutero Yehova.

39 “Komabe mʼtsogolomo ndidzabwezera
    anthu a ku Elamu dziko lawo,”
            akutero Yehova.

A Message About Ammon

49 Concerning the Ammonites:(A)

This is what the Lord says:

“Has Israel no sons?
    Has Israel no heir?
Why then has Molek[a](B) taken possession of Gad?(C)
    Why do his people live in its towns?
But the days are coming,”
    declares the Lord,
“when I will sound the battle cry(D)
    against Rabbah(E) of the Ammonites;
it will become a mound of ruins,(F)
    and its surrounding villages will be set on fire.
Then Israel will drive out
    those who drove her out,(G)
says the Lord.
“Wail, Heshbon,(H) for Ai(I) is destroyed!
    Cry out, you inhabitants of Rabbah!
Put on sackcloth(J) and mourn;
    rush here and there inside the walls,
for Molek(K) will go into exile,(L)
    together with his priests and officials.
Why do you boast of your valleys,
    boast of your valleys so fruitful?
Unfaithful Daughter Ammon,(M)
    you trust in your riches(N) and say,
    ‘Who will attack me?’(O)
I will bring terror on you
    from all those around you,”
declares the Lord, the Lord Almighty.
“Every one of you will be driven away,
    and no one will gather the fugitives.(P)

“Yet afterward, I will restore(Q) the fortunes of the Ammonites,”
declares the Lord.

A Message About Edom(R)(S)

Concerning Edom:(T)

This is what the Lord Almighty says:

“Is there no longer wisdom in Teman?(U)
    Has counsel perished from the prudent?
    Has their wisdom decayed?
Turn and flee, hide in deep caves,(V)
    you who live in Dedan,(W)
for I will bring disaster on Esau
    at the time when I punish him.
If grape pickers came to you,
    would they not leave a few grapes?
If thieves came during the night,
    would they not steal only as much as they wanted?
10 But I will strip Esau bare;
    I will uncover his hiding places,(X)
    so that he cannot conceal himself.
His armed men are destroyed,
    also his allies and neighbors,
    so there is no one(Y) to say,
11 ‘Leave your fatherless children;(Z) I will keep them alive.
    Your widows(AA) too can depend on me.’”

12 This is what the Lord says: “If those who do not deserve to drink the cup(AB) must drink it, why should you go unpunished?(AC) You will not go unpunished, but must drink it. 13 I swear(AD) by myself,” declares the Lord, “that Bozrah(AE) will become a ruin and a curse,[b] an object of horror(AF) and reproach;(AG) and all its towns will be in ruins forever.”(AH)

14 I have heard a message from the Lord;
    an envoy was sent to the nations to say,
“Assemble yourselves to attack it!
    Rise up for battle!”

15 “Now I will make you small among the nations,
    despised by mankind.
16 The terror you inspire
    and the pride(AI) of your heart have deceived you,
you who live in the clefts of the rocks,(AJ)
    who occupy the heights of the hill.
Though you build your nest(AK) as high as the eagle’s,
    from there I will bring you down,”
declares the Lord.
17 “Edom will become an object of horror;(AL)
    all who pass by will be appalled and will scoff
    because of all its wounds.(AM)
18 As Sodom(AN) and Gomorrah(AO) were overthrown,
    along with their neighboring towns,”
says the Lord,
“so no one will live there;
    no people will dwell(AP) in it.

19 “Like a lion(AQ) coming up from Jordan’s thickets(AR)
    to a rich pastureland,
I will chase Edom from its land in an instant.
    Who is the chosen one I will appoint for this?
Who is like(AS) me and who can challenge me?(AT)
    And what shepherd(AU) can stand against me?”

20 Therefore, hear what the Lord has planned against Edom,(AV)
    what he has purposed(AW) against those who live in Teman:(AX)
The young of the flock(AY) will be dragged away;
    their pasture will be appalled at their fate.(AZ)
21 At the sound of their fall the earth will tremble;(BA)
    their cry(BB) will resound to the Red Sea.[c]
22 Look! An eagle will soar and swoop(BC) down,
    spreading its wings over Bozrah.(BD)
In that day the hearts of Edom’s warriors(BE)
    will be like the heart of a woman in labor.(BF)

A Message About Damascus

23 Concerning Damascus:(BG)

“Hamath(BH) and Arpad(BI) are dismayed,
    for they have heard bad news.
They are disheartened,
    troubled like[d] the restless sea.(BJ)
24 Damascus has become feeble,
    she has turned to flee
    and panic has gripped her;
anguish and pain have seized her,
    pain like that of a woman in labor.(BK)
25 Why has the city of renown not been abandoned,
    the town in which I delight?
26 Surely, her young men(BL) will fall in the streets;
    all her soldiers will be silenced(BM) in that day,”
declares the Lord Almighty.
27 “I will set fire(BN) to the walls of Damascus;(BO)
    it will consume(BP) the fortresses of Ben-Hadad.(BQ)

A Message About Kedar and Hazor

28 Concerning Kedar(BR) and the kingdoms of Hazor,(BS) which Nebuchadnezzar(BT) king of Babylon attacked:

This is what the Lord says:

“Arise, and attack Kedar
    and destroy the people of the East.(BU)
29 Their tents and their flocks(BV) will be taken;
    their shelters will be carried off
    with all their goods and camels.
People will shout to them,
    ‘Terror(BW) on every side!’

30 “Flee quickly away!
    Stay in deep caves,(BX) you who live in Hazor,(BY)
declares the Lord.
“Nebuchadnezzar(BZ) king of Babylon has plotted against you;
    he has devised a plan against you.

31 “Arise and attack a nation at ease,
    which lives in confidence,”
declares the Lord,
“a nation that has neither gates nor bars;(CA)
    its people live far from danger.
32 Their camels(CB) will become plunder,
    and their large herds(CC) will be spoils of war.
I will scatter to the winds(CD) those who are in distant places[e](CE)
    and will bring disaster on them from every side,”
declares the Lord.
33 “Hazor(CF) will become a haunt of jackals,(CG)
    a desolate(CH) place forever.
No one will live there;
    no people will dwell(CI) in it.”

A Message About Elam

34 This is the word of the Lord that came to Jeremiah the prophet concerning Elam,(CJ) early in the reign of Zedekiah(CK) king of Judah:

35 This is what the Lord Almighty says:

“See, I will break the bow(CL) of Elam,
    the mainstay of their might.
36 I will bring against Elam the four winds(CM)
    from the four quarters of heaven;(CN)
I will scatter them to the four winds,
    and there will not be a nation
    where Elam’s exiles do not go.
37 I will shatter Elam before their foes,
    before those who want to kill them;
I will bring disaster on them,
    even my fierce anger,”(CO)
declares the Lord.
“I will pursue them with the sword(CP)
    until I have made an end of them.
38 I will set my throne in Elam
    and destroy her king and officials,”
declares the Lord.

39 “Yet I will restore(CQ) the fortunes of Elam
    in days to come,”
declares the Lord.

Footnotes

  1. Jeremiah 49:1 Or their king; also in verse 3
  2. Jeremiah 49:13 That is, its name will be used in cursing (see 29:22); or, others will see that it is cursed.
  3. Jeremiah 49:21 Or the Sea of Reeds
  4. Jeremiah 49:23 Hebrew on or by
  5. Jeremiah 49:32 Or who clip the hair by their foreheads