Add parallel Print Page Options

Uthenga kwa Baruki

45 Uwu ndi uthenga umene mneneri Yeremiya anawuza Baruki mwana wa Neriya mʼchaka cha chinayi cha Yehoyakimu mwana wa mwana ya Yosiya kuti alembe mʼbuku. “Yehova Mulungu wa Israeli, akunena kwa iwe Baruki kuti: Iwe unati, ‘Kalanga ine! Yehova wawonjezera chisoni pa mavuto anga. Ine ndatopa ndi kubuwula ndipo sindikupeza mpumulo.’ ”

Koma Yehova akukuwuza kuti, “Ndidzagwetsa chimene ndinamanga ndipo ndidzazula chimene ndinadzala. Ndidzachita zimenezi mʼdziko lonse. Kodi tsono ukudzifunira wekha zinthu zazikulu? Usadzifunire. Pakuti ndidzagwetsa mavuto pa anthu onse, koma ndidzasunga moyo wako kulikonse kumene ungadzapite.”

A Message to Baruch

45 When Baruch(A) son of Neriah(B) wrote on a scroll(C) the words Jeremiah the prophet dictated in the fourth year of Jehoiakim(D) son of Josiah king of Judah, Jeremiah said this to Baruch: “This is what the Lord, the God of Israel, says to you, Baruch: You said, ‘Woe(E) to me! The Lord has added sorrow(F) to my pain;(G) I am worn out with groaning(H) and find no rest.’(I) But the Lord has told me to say to you, ‘This is what the Lord says: I will overthrow what I have built and uproot(J) what I have planted,(K) throughout the earth.(L) Should you then seek great(M) things for yourself? Do not seek them.(N) For I will bring disaster(O) on all people,(P) declares the Lord, but wherever you go I will let you escape(Q) with your life.’”(R)