Add parallel Print Page Options

43 Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze, Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’ Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”

Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda. Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako. Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya. Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.

Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti, “Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona. 10 Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi. 11 Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga. 12 Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere. 13 Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’ ”

43 When Jeremiah had finished telling the people all the words of the Lord their God—everything the Lord had sent him to tell them(A) Azariah son of Hoshaiah(B) and Johanan(C) son of Kareah and all the arrogant(D) men said to Jeremiah, “You are lying!(E) The Lord our God has not sent you to say, ‘You must not go to Egypt to settle there.’(F) But Baruch(G) son of Neriah is inciting you against us to hand us over to the Babylonians,[a] so they may kill us or carry us into exile to Babylon.”(H)

So Johanan son of Kareah and all the army officers and all the people(I) disobeyed the Lord’s command(J) to stay in the land of Judah.(K) Instead, Johanan son of Kareah and all the army officers led away all the remnant of Judah who had come back to live in the land of Judah from all the nations where they had been scattered.(L) They also led away all those whom Nebuzaradan commander of the imperial guard had left with Gedaliah son of Ahikam, the son of Shaphan—the men, the women,(M) the children and the king’s daughters. And they took Jeremiah the prophet and Baruch(N) son of Neriah along with them. So they entered Egypt(O) in disobedience to the Lord and went as far as Tahpanhes.(P)

In Tahpanhes(Q) the word of the Lord came to Jeremiah: “While the Jews are watching, take some large stones(R) with you and bury them in clay in the brick(S) pavement at the entrance to Pharaoh’s palace(T) in Tahpanhes. 10 Then say to them, ‘This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: I will send for my servant(U) Nebuchadnezzar(V) king of Babylon, and I will set his throne(W) over these stones I have buried here; he will spread his royal canopy(X) above them. 11 He will come and attack Egypt,(Y) bringing death(Z) to those destined(AA) for death, captivity to those destined for captivity,(AB) and the sword to those destined for the sword.(AC) 12 He will set fire(AD) to the temples(AE) of the gods(AF) of Egypt; he will burn their temples and take their gods captive.(AG) As a shepherd picks(AH) his garment clean of lice, so he will pick Egypt clean and depart. 13 There in the temple of the sun[b](AI) in Egypt he will demolish the sacred pillars(AJ) and will burn down the temples of the gods of Egypt.’”

Footnotes

  1. Jeremiah 43:3 Or Chaldeans
  2. Jeremiah 43:13 Or in Heliopolis