Add parallel Print Page Options

Lonjezo la Kubwezeretsedwa

33 Yeremiya akanali mʼndende mʼbwalo la alonda, Yehova anayankhula nayenso kachiwiri nati: “Yehova amene analenga dziko lapansi, kuliwumba ndi kulikhazikitsa; amene dzina lake ndi Yehova, akuti, ‘Unditame mopemba ndipo ndidzakuyankha. Ndidzakuwuza zinsinsi zazikulu zimene suzidziwa.’ Yehova Mulungu wa Israeli akunenapo pa za nyumba za mu mzinda muno ndiponso pa za nyumba za mafumu a Yuda. Zidzagwetsedwa, ndipo palibe chifukwa cholimbana ndi mitumbira ya nkhondo ya Ababuloni. Ababuloni akubwera kudzawuthira nkhondo mzindawu ndipo nyumba zake zidzadzaza ndi mitembo ya anthu amene ndidzawapha mokwiya ndi mwaukali. Ndawufulatira mzinda uno chifukwa cha zoyipa zake zonse.

“ ‘Pambuyo pake mzindawu ndidzawupatsanso moyo ndi kuwuchiritsa; ndidzachiritsa anthu anga ndi kuwapatsa chitetezo ndi mtendere weniweni. Ndidzawakhazikanso Ayuda ndi Aisraeli ku dziko lawo, ndipo ndidzawabwezera monga mmene analili poyamba. Ndidzawayeretsa pochotsa zoyipa zonse zimene anandichitira, ndiponso ndidzawakhululukira machimo onse amene anachita pondiwukira. Mzinda wa Yerusalemu udzandipatsa chimwemwe, chiyamiko ndi ulemerero. Anthu a mitundu yonse adzanditamanda akadzamva za zabwino zonse zimene ndawuchitira mzindawu. Iwo adzachita mantha ndi kunjenjemera poona madalitso ochuluka ndi mtendere zimene ndapereka kwa mzinda umenewu.’

10 “Yehova akuti, ‘Inu mumanena za malo ano kuti ndi bwinja,’ malo opandamo anthu kapena nyama. Komatu mizinda ya Yuda ndi mʼmisewu ya mu Yerusalemu mʼmene tsopano muli zii mudzamvekanso 11 mfuwu wachimwemwe ndi mawu achisangalalo, mawu a mkwatibwi ndi mkwati. Mʼnyumba ya Mulungu mudzamvekanso nyimbo za anthu amene akudzapereka nsembe zothokoza Yehova. Azidzati,

“Yamikani Yehova Wamphamvuzonse,
    popeza Iye ndi wabwino;
    pakuti chifundo chake nʼchamuyaya.”

Pakuti ndidzabwezeretsa zinthu zabwino za dziko lino monga zinalili poyamba, akutero Yehova.

12 “Yehova Wamphamvuzonse akuti, ‘Malo ano, a chipululu ndi wopanda anthu kapena nyama, mʼmizinda yake yonse mudzakhala msipu umene abusa adzadyetserako nkhosa zawo. 13 Ku mizinda ya kumapiri, ya kuchigwa, ya ku Negevi, ya ku dera la Benjamini, ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi ku mizinda ya Yuda, nkhosa zidzadutsanso pamaso pa munthu woziwerenga,’ akutero Yehova.

14 “ ‘Taonani masiku akubwera,’ akutero Yehova, ‘pamene ndidzachitadi zokoma zimene ndinalonjeza Aisraeli ndi nyumba ya Yuda.

15 “ ‘Mʼmasiku amenewo ndi pa nthawi imeneyo
    ndidzaphukitsa Nthambi yolungama kuchokera ku banja la Davide;
    munthuyo adzachita zolungama ndi zabwino mʼdziko.
16 Mʼmasiku amenewo Yuda adzapulumuka
    ndipo Yerusalemu adzakhala mwamtendere.
Dzina limene mzindawu udzadziwike nalo ndi ili:
    Yehova Chilungamo Chathu.’

17 Yehova akunena kuti, ‘Davide sadzasowa mdzukulu wolowa mʼmalo mwake pa mpando waufumu wa Israeli, 18 ngakhale ansembe, amene ndi Alevi, sadzasowanso munthu woyima pamaso panga nthawi zonse wopereka nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi nsembe zina.’ ”

19 Yehova anawuza Yeremiya kuti: 20 Mawu anga ndi awa. Ine ndinachita pangano ndi usana ndi usiku kuti zizibwera pa nthawi yake. Pangano limeneli inu simungaliphwanye. 21 Ndinachitanso pangano ndi Davide, mtumiki wanga kuti nthawi zonse adzakhala ndi mdzukulu wodzakhala pa mpando wake waufumu. Ndinachitanso pangano ndi Alevi kuti iwonso adzanditumikira nthawi zonse. Mapangano amenewa sadzaphwanyidwa nthawi zonse. 22 Ndidzachulukitsa ngati nyenyezi zamlengalenga ndiponso ngati mchenga wa mʼmbali mwa nyanja zidzukulu za mtumiki wanga Davide ndiponso za Alevi amene amanditumikira Ine.

23 Yehova anafunsa Yeremiya kuti, 24 “Kodi sunamve mmene anthu ena akumanenera kuti, ‘Yehova wakana maufumu awiriwa amene Iye anawasankha.’ Kotero anthuwo akunyoza anthu anga ndipo sakuwayesanso mtundu wa anthu. 25 ‘Koma Ine Yehova ndinachita pangano ndi usana ndi usiku. Ndinakhazikitsanso malamulo oyendetsa dziko lakumwamba ndi dziko lapansi, 26 monga ndachita zimenezi motsimikiza, choncho ndidzasunga pangano limene ndinachita ndi zidzukulu za Yakobo ndi Davide mtumiki wanga. Ndidzasankha mmodzi mwa ana a Davide kuti alamulire zidzukulu za Abrahamu, Isake ndi Yakobo. Komatu ndidzawamvera chifundo ndi kuwakhazikanso pabwino.’ ”

Promise of Restoration

33 While Jeremiah was still confined(A) in the courtyard(B) of the guard, the word of the Lord came to him a second time:(C) “This is what the Lord says, he who made the earth,(D) the Lord who formed it and established it—the Lord is his name:(E) ‘Call(F) to me and I will answer you and tell you great and unsearchable(G) things you do not know.’ For this is what the Lord, the God of Israel, says about the houses in this city and the royal palaces of Judah that have been torn down to be used against the siege(H) ramps(I) and the sword in the fight with the Babylonians[a]: ‘They will be filled with the dead bodies of the people I will slay in my anger and wrath.(J) I will hide my face(K) from this city because of all its wickedness.

“‘Nevertheless, I will bring health and healing to it; I will heal(L) my people and will let them enjoy abundant peace(M) and security. I will bring Judah(N) and Israel back from captivity[b](O) and will rebuild(P) them as they were before.(Q) I will cleanse(R) them from all the sin they have committed against me and will forgive(S) all their sins of rebellion against me. Then this city will bring me renown,(T) joy, praise(U) and honor(V) before all nations on earth that hear of all the good things I do for it; and they will be in awe and will tremble(W) at the abundant prosperity and peace I provide for it.’

10 “This is what the Lord says: ‘You say about this place, “It is a desolate waste, without people or animals.”(X) Yet in the towns of Judah and the streets of Jerusalem that are deserted,(Y) inhabited by neither people nor animals, there will be heard once more 11 the sounds of joy and gladness,(Z) the voices of bride and bridegroom, and the voices of those who bring thank offerings(AA) to the house of the Lord, saying,

“Give thanks to the Lord Almighty,
    for the Lord is good;(AB)
    his love endures forever.”(AC)

For I will restore the fortunes(AD) of the land as they were before,(AE)’ says the Lord.

12 “This is what the Lord Almighty says: ‘In this place, desolate(AF) and without people or animals(AG)—in all its towns there will again be pastures for shepherds to rest their flocks.(AH) 13 In the towns of the hill(AI) country, of the western foothills and of the Negev,(AJ) in the territory of Benjamin, in the villages around Jerusalem and in the towns of Judah, flocks will again pass under the hand(AK) of the one who counts them,’ says the Lord.

14 “‘The days are coming,’ declares the Lord, ‘when I will fulfill the good promise(AL) I made to the people of Israel and Judah.

15 “‘In those days and at that time
    I will make a righteous(AM) Branch(AN) sprout from David’s line;(AO)
    he will do what is just and right in the land.
16 In those days Judah will be saved(AP)
    and Jerusalem will live in safety.(AQ)
This is the name by which it[c] will be called:(AR)
    The Lord Our Righteous Savior.’(AS)

17 For this is what the Lord says: ‘David will never fail(AT) to have a man to sit on the throne of Israel, 18 nor will the Levitical(AU) priests(AV) ever fail to have a man to stand before me continually to offer burnt offerings, to burn grain offerings and to present sacrifices.(AW)’”

19 The word of the Lord came to Jeremiah: 20 “This is what the Lord says: ‘If you can break my covenant with the day(AX) and my covenant with the night, so that day and night no longer come at their appointed time,(AY) 21 then my covenant(AZ) with David my servant—and my covenant with the Levites(BA) who are priests ministering before me—can be broken and David will no longer have a descendant to reign on his throne.(BB) 22 I will make the descendants of David my servant and the Levites who minister before me as countless(BC) as the stars in the sky and as measureless as the sand on the seashore.’”

23 The word of the Lord came to Jeremiah: 24 “Have you not noticed that these people are saying, ‘The Lord has rejected the two kingdoms[d](BD) he chose’? So they despise(BE) my people and no longer regard them as a nation.(BF) 25 This is what the Lord says: ‘If I have not made my covenant with day and night(BG) and established the laws(BH) of heaven and earth,(BI) 26 then I will reject(BJ) the descendants of Jacob(BK) and David my servant and will not choose one of his sons to rule over the descendants of Abraham, Isaac and Jacob. For I will restore their fortunes[e](BL) and have compassion(BM) on them.’”

Footnotes

  1. Jeremiah 33:5 Or Chaldeans
  2. Jeremiah 33:7 Or will restore the fortunes of Judah and Israel
  3. Jeremiah 33:16 Or he
  4. Jeremiah 33:24 Or families
  5. Jeremiah 33:26 Or will bring them back from captivity