Add parallel Print Page Options

Hananiya Atsutsana ndi Yeremiya

28 Chaka chomwecho mwezi wachisanu wa chaka chachinayi, poyambirira pa ulamuliro wa Zedekiya mfumu ya Yuda, mneneri Hananiya mwana wa Azuri, amene amachokera ku Gibiyoni, anandiwuza ine mʼNyumba ya Yehova pamaso pa ansembe ndi anthu onse kuti, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akuti, ‘Ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni. Pasanathe zaka ziwiri ndidzabweretsa pa malo ano ziwiya zonse za ku Nyumba ya Yehova zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni anazichotsa pa malo pano ndi kupita nazo ku Babuloni. Ndidzabweretsanso pa malo pano Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda pamodzi ndi akapolo ena onse ochokera ku Yuda amene anapita ku Babuloni,’ akutero Yehova, ‘chifukwa ndidzathyola goli la mfumu ya ku Babuloni.’ ”

Pamenepo mneneri Yeremiya anayankha mneneri Hananiya pamaso pa ansembe ndi anthu onse amene anasonkhana mʼNyumba ya Yehova. Anati, “Ameni! Yehova achitedi zomwezo! Yehova akwaniritse mawu amene waloserawo. Iye abweretsenso pa malo pano ziwiya za mʼNyumba ya Yehova ndi akapolo onse kuchokera ku Babuloni. Komabe, tamvera zimene nditi ndikuwuze iweyo pamodzi ndi anthu onse: Kunali aneneri kalelo, ine ndi iwe tisanabadwe. Iwowa analosera za nkhondo, mavuto ndi mliri kuti zidzagwera mayiko ambiri ndi maufumu amphamvu. Koma mneneri amene amalosera zamtendere adzadziwika kuti ndi woona ndi kuti watumidwa ndi Yehova ngati zimene wanenera zachitikadi.”

10 Pamenepo mneneri Hananiya anachotsa goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya nalithyola, 11 ndipo anawuza anthu onse kuti, “Yehova akuti, ‘Umu ndi mmene ndidzathyolere goli la Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonse pasanathe zaka ziwiri.’ ” Zitatero, mneneri Yeremiya anachoka.

12 Patapita nthawi pangʼono, mneneri Hananiya atathyola goli mʼkhosi mwa mneneri Yeremiya, Yehova anawuza Yeremiya kuti, 13 “Pita, kawuze mneneri Hananiya kuti, ‘Yehova akuti: Iwe wathyola goli lamtengo, mʼmalo mwake Ine ndidzayika goli lachitsulo. 14 Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayika goli lachitsulo mʼkhosi mwa anthu a mitundu yonseyi kuti atumikire Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo iwo adzamutumikiradi. Ndipo ndamupatsanso ulamuliro ngakhale pa nyama zakuthengo.’ ”

15 Ndipo mneneri Yeremiya anawuza mneneri Hananiya kuti, “Tamvera, Hananiya! Iweyo Yehova sanakutume, koma iwe wanyenga anthuwa kuti akhulupirire zabodza. 16 Nʼchifukwa chake Yehova akuti, ‘Ndatsala pangʼono kukuchotsa pa dziko lapansi. Iwe ufa chaka chino chisanathe, chifukwa wakhala ukulalikira zowukira Yehova.’ ”

17 Mʼmwezi wachisanu ndi chiwiri wa chaka chomwecho, mneneri Hananiya anamwaliradi.

The False Prophet Hananiah

28 In the fifth month of that same year, the fourth year, early in the reign of Zedekiah(A) king of Judah, the prophet Hananiah son of Azzur, who was from Gibeon,(B) said to me in the house of the Lord in the presence of the priests and all the people: “This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: ‘I will break the yoke(C) of the king of Babylon. Within two years I will bring back to this place all the articles(D) of the Lord’s house that Nebuchadnezzar king of Babylon removed from here and took to Babylon. I will also bring back to this place Jehoiachin[a](E) son of Jehoiakim king of Judah and all the other exiles from Judah who went to Babylon,’ declares the Lord, ‘for I will break the yoke of the king of Babylon.’”(F)

Then the prophet Jeremiah replied to the prophet Hananiah before the priests and all the people who were standing in the house of the Lord. He said, “Amen! May the Lord do so! May the Lord fulfill the words you have prophesied by bringing the articles of the Lord’s house and all the exiles back to this place from Babylon.(G) Nevertheless, listen to what I have to say in your hearing and in the hearing of all the people: From early times the prophets who preceded you and me have prophesied war, disaster and plague(H) against many countries and great kingdoms. But the prophet who prophesies peace will be recognized as one truly sent by the Lord only if his prediction comes true.(I)

10 Then the prophet Hananiah took the yoke(J) off the neck of the prophet Jeremiah and broke it, 11 and he said(K) before all the people, “This is what the Lord says: ‘In the same way I will break the yoke of Nebuchadnezzar king of Babylon off the neck of all the nations within two years.’” At this, the prophet Jeremiah went on his way.

12 After the prophet Hananiah had broken the yoke off the neck of the prophet Jeremiah, the word of the Lord came to Jeremiah: 13 “Go and tell Hananiah, ‘This is what the Lord says: You have broken a wooden yoke, but in its place you will get a yoke of iron. 14 This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: I will put an iron yoke(L) on the necks of all these nations to make them serve(M) Nebuchadnezzar(N) king of Babylon, and they will serve him. I will even give him control over the wild animals.(O)’”

15 Then the prophet Jeremiah said to Hananiah the prophet, “Listen, Hananiah! The Lord has not sent(P) you, yet you have persuaded this nation to trust in lies.(Q) 16 Therefore this is what the Lord says: ‘I am about to remove you from the face of the earth.(R) This very year you are going to die,(S) because you have preached rebellion(T) against the Lord.’”

17 In the seventh month of that same year, Hananiah the prophet died.(U)

Footnotes

  1. Jeremiah 28:4 Hebrew Jeconiah, a variant of Jehoiachin