Add parallel Print Page Options

Yuda Adzatumikira Nebukadinezara

27 Zedekiya mwana wa Yosiya, mfumu ya ku Yuda, atangoyamba kulamulira, Yehova anawuza Yeremiya kuti, “Tenga zingwe zomangira ndi mitengo ya goli ndipo uzimangirire mʼkhosi mwako. Tsono utumize uthenga kwa mafumu a Edomu, Mowabu, Amoni, Turo ndi Sidoni kudzera mwa amithenga amene abwera ku Yerusalemu kwa Zedekiya, mfumu ya Yuda. Uwapatse uthenga wokapereka kwa ambuye awo ndipo uwawuze kuti: Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Mukawuze ambuye anu kuti: Ndi mphamvu zanga ndi dzanja langa lamphamvu ndinalenga dziko lapansi ndi anthu ake onse pamodzi ndi nyama zili mʼmenemo, ndipo ndimalipereka kwa aliyense amene ndikufuna. Tsopano ndidzapereka mayiko anu onse kwa mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Ndamupatsanso nyama zakuthengo zonse kuti zimutumikire. Anthu a mitundu yonse adzamutumikira iyeyo, mwana wake ndi chidzukulu chake mpaka nthawi itakwana yoti dziko lake liwonongedwe. Pamenepo mitundu yambiri ndi mafumu amphamvu adzamugonjetsa.

“ ‘Koma ngati anthu a mtundu wina uliwonse kapena ufumu wina uliwonse adzakana kutumikira Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni kapena kusenza goli lake, Ine ndidzalanga mtundu umenewo ndi lupanga, ndi njala ndi mliri, akutero Yehova, mpaka nditawapereka mʼmanja mwake kotheratu. Choncho musamvere aneneri anu, owombeza anu, otanthauza maloto anu, amawula anu kapena amatsenga anu akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni.’ 10 Iwo akukuloserani zabodza kotero kuti adani adzakuchotsani mʼdziko lanu nʼkupita nanu ku dziko lakutali. Ndidzakupirikitsani ndi kukuwonongani kotheratu. 11 Koma ngati mtundu wina uliwonse udzagonjera mfumu ya ku Babuloni ndi kuyitumukira, ndidzawusiya kuti ukhale mʼdziko lake kuti uzilima ndi kukhalamo, akutero Yehova.’ ”

12 Uthenga womwewu ndinawuzanso Hezekiya mfumu ya Yuda. Ndinati, “Gonjerani mfumu ya ku Babuloni. Itumikireni iyoyo pamodzi ndi anthu ake ndipo mudzakhala ndi moyo. 13 Nanga inu ndi anthu anu, muferenji ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri, zimene Yehova waopsezera mtundu wina uliwonse umene sudzatumikira mfumu ya ku Babuloni? 14 Musamvere mawu a aneneri akamakuwuzani kuti, ‘Simudzatumikira mfumu ya ku Babuloni,’ chifukwa zimene akukuloseranizo nʼzabodza. 15 Sindinawatume ngakhale iwo akulosera mʼdzina langa. Nʼchifukwa chake, ndidzakupirikitsani ndipo mudzawonongeka kotheratu, inu pamodzi ndi aneneri amene akunenera zabodza kwa inu.”

16 Kenaka ndinawuza ansembe pamodzi ndi anthu ena onse kuti, “Yehova akuti: Musamvere aneneri amene akumanena kuti, ‘Posachedwapa ziwiya za mʼNyumba ya Yehova zibwera kuchokera ku Babuloni.’ Iwowo akunenera zabodza kwa inu. 17 Musawamvere. Tumikirani mfumu ya ku Babuloni, ndipo mudzakhala ndi moyo. Mzindawu usandukirenji bwinja? 18 Ngati iwo ndi aneneri ndipo ali ndi mawu a Yehova, apempheretu kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti ziwiya zimene zatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndiponso mu Yerusalemu zisatengedwe kupita ku Babuloni. 19 Pakuti Yehova akunena za zipilala, za mbiya ya madzi, maphaka ndi ziwiya zina zimene zatsala mu Yerusalemu. 20 Izi ndi zimene Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni sanatenge pamene anatenga ukapolo Yekoniya mwana wa Yehoyakimu mfumu ya Yuda kupita ku Babuloni kuchokera ku Yerusalemu, pamodzi ndi anthu olemekezeka a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. 21 Inde, Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, akunena za zinthu zimene zinatsala mʼNyumba ya Yehova ndi mʼnyumba ya mfumu ya Yuda ndi mu Yerusalemu kuti, 22 ‘Zidzatengedwa kupita ku Babuloni ndipo zidzakhala kumeneko mpaka tsiku limene ndidzawakumbukirenso,’ akutero Yehova. ‘Pamenepo ndidzazitenganso ndi kuzibwezanso ku malo ano.’ ”

Judah to Serve Nebuchadnezzar

27 Early in the reign of Zedekiah[a](A) son of Josiah king of Judah, this word came to Jeremiah from the Lord: This is what the Lord said to me: “Make a yoke(B) out of straps and crossbars and put it on your neck. Then send(C) word to the kings of Edom, Moab, Ammon,(D) Tyre and Sidon(E) through the envoys who have come to Jerusalem to Zedekiah king of Judah. Give them a message for their masters and say, ‘This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: “Tell this to your masters: With my great power and outstretched arm(F) I made(G) the earth and its people and the animals(H) that are on it, and I give(I) it to anyone I please. Now I will give all your countries into the hands of my servant(J) Nebuchadnezzar(K) king of Babylon; I will make even the wild animals subject to him.(L) All nations will serve(M) him and his son and his grandson until the time(N) for his land comes; then many nations and great kings will subjugate(O) him.

“‘“If, however, any nation or kingdom will not serve Nebuchadnezzar king of Babylon or bow its neck under his yoke, I will punish(P) that nation with the sword,(Q) famine(R) and plague,(S) declares the Lord, until I destroy it by his hand. So do not listen to your prophets,(T) your diviners,(U) your interpreters of dreams,(V) your mediums(W) or your sorcerers(X) who tell you, ‘You will not serve(Y) the king of Babylon.’ 10 They prophesy lies(Z) to you that will only serve to remove(AA) you far from your lands; I will banish you and you will perish. 11 But if any nation will bow its neck under the yoke(AB) of the king of Babylon and serve him, I will let that nation remain in its own land to till it and to live(AC) there, declares the Lord.”’”

12 I gave the same message to Zedekiah king of Judah. I said, “Bow your neck under the yoke(AD) of the king of Babylon; serve him and his people, and you will live.(AE) 13 Why will you and your people die(AF) by the sword, famine and plague(AG) with which the Lord has threatened any nation that will not serve the king of Babylon? 14 Do not listen(AH) to the words of the prophets(AI) who say to you, ‘You will not serve the king of Babylon,’ for they are prophesying lies(AJ) to you. 15 ‘I have not sent(AK) them,’ declares the Lord. ‘They are prophesying lies in my name.(AL) Therefore, I will banish you and you will perish,(AM) both you and the prophets who prophesy to you.’”

16 Then I said to the priests and all these people, “This is what the Lord says: Do not listen to the prophets who say, ‘Very soon now the articles(AN) from the Lord’s house will be brought back from Babylon.’ They are prophesying lies to you. 17 Do not listen(AO) to them. Serve the king of Babylon, and you will live.(AP) Why should this city become a ruin? 18 If they are prophets and have the word of the Lord, let them plead(AQ) with the Lord Almighty that the articles remaining in the house of the Lord and in the palace of the king of Judah and in Jerusalem not be taken to Babylon. 19 For this is what the Lord Almighty says about the pillars, the bronze Sea,(AR) the movable stands and the other articles(AS) that are left in this city, 20 which Nebuchadnezzar king of Babylon did not take away when he carried(AT) Jehoiachin[b](AU) son of Jehoiakim king of Judah into exile from Jerusalem to Babylon, along with all the nobles of Judah and Jerusalem— 21 yes, this is what the Lord Almighty, the God of Israel, says about the things that are left in the house of the Lord and in the palace of the king of Judah and in Jerusalem: 22 ‘They will be taken(AV) to Babylon and there they will remain until the day(AW) I come for them,’ declares the Lord. ‘Then I will bring(AX) them back and restore them to this place.’”

Footnotes

  1. Jeremiah 27:1 A few Hebrew manuscripts and Syriac (see also 27:3,12 and 28:1); most Hebrew manuscripts Jehoiakim (Most Septuagint manuscripts do not have this verse.)
  2. Jeremiah 27:20 Hebrew Jeconiah, a variant of Jehoiachin