Add parallel Print Page Options

Yeremiya Amangidwa

26 Yehoyakimu, mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda atayamba kulamulira, Yehova anayankhula ndi Yeremiya kuti, “Kayime mʼbwalo la Nyumba ya Yehova. Ndipo ukayankhule kwa anthu onse okhala mʼmizinda ya ku Yuda amene amabwera kudzapembedza ku Nyumba ya Yehova. Ukawawuze zonse zomwe ndakulamula; usakasiyeko ndi mawu amodzi omwe. Mwina mwake adzamvera, ndipo aliyense adzatembenuka kuleka njira yake yoyipa. Ndiye ine ndidzaleka osapatsa chilango chimene ndinakonzekera kuti ndiwalange nacho chifukwa cha ntchito zawo zoyipa. Ukawawuze kuti, ‘Yehova akuti: Ngati simundimvera Ine ndi kuleka kutsatira malamulo anga, amene ndakupatsani, ndipo ngati simumvera mawu a atumiki anga, aneneri amene ndakhala ndikukutumizirani, ngakhale kuti simunawamvere, ndiye kuti Ine ndidzasandutsa Nyumba ino kukhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala chinthu chotembereredwa pakati pa mitundu yonse ya pa dziko lapansi.’ ”

Ansembe, aneneri ndi anthu onse anamva Yeremiya akuyankhula mawu amenewa mʼNyumba ya Yehova. Yeremiya atangotsiriza kuwawuza anthu aja zonse zimene Yehova anamulamula kuti ayankhule, ansembe, aneneri pamodzi ndi anthu onse anamugwira ndipo anati, “Uyenera kuphedwa! Chifukwa chiyani walosera mʼdzina la Yehova kuti Nyumba ino idzakhala ngati Silo ndipo mzinda uno udzakhala wopanda anthu ngati chipululu?” Anthu onse anamuzungulira Yeremiya mʼNyumba ya Yehova.

10 Koma nduna za ku Yuda zitamva zomwe zinachitikazi, zinanyamuka kuchokera ku nyumba yaufumu kupita ku Nyumba ya Yehova, nakakhala pamalo pawo, pa Chipata Chatsopano cha Nyumba ya Yehova. 11 Pamenepo ansembe ndi aneneri anawuza ndunazo pamodzi ndi anthu onse kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa chifukwa amalosera zoyipira mzinda uno. Inu mwadzimvera nokha zimenezi!”

12 Ndipo Yeremiya anawuza nduna zija ndi anthu onse kuti, “Yehova anandituma kunenera mawu onse amene mwawamva otsutsa Nyumba ino ndi mzinda uno. 13 Tsopano konzani njira zanu ndi zochita zanu ndipo mverani Yehova Mulungu wanu. Mukatero ndiye kuti Yehova adzaleka osakupatsani chilango chimene ankati akupatseni. 14 Kunena za ine, ndili mʼmanja mwanu; mundichite chilichonse chimene mukuganiza kuti ndi chabwino ndi choyenera. 15 Komatu dziwani kuti ngati mundipha, inu pamodzi ndi mzinda uno ndi onse amene amakhala muno, mudzapalamula mlandu wokhetsa magazi a munthu wosalakwa. Ndithudi Yehova anandituma kuti ndidzayankhule mawu onsewa inu mukumva.”

16 Pamenepo ndunazo pamodzi ndi anthu onse anawuza ansembe ndi aneneri kuti, “Munthu uyu sayenera kuphedwa! Pakuti wayankhula kwa ife mʼdzina la Yehova Mulungu wathu.”

17 Akuluakulu ena a mʼdzikomo anayimirira ndi kuwuza gulu lonse la anthu kuti, 18 “Mʼmasiku a Hezekiya mfumu ya ku Yuda, Mika wa ku Moreseti ankalosera. Iye ankawuza anthu kuti Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“ ‘Ziyoni adzatipulidwa ngati munda,
    Yerusalemu adzasanduka bwinja,
    ndipo phiri la Nyumba ya Mulungu lidzasanduka nkhalango yowirira.’

19 Kodi Hezekiya mfumu ya ku Yuda ndi anthu onse anamupha amene uja? Kodi suja mfumu inaopa Yehova ndi kupempha kuti ayikomere mtima? Ndipo suja Yehova anasintha maganizo ake nʼkuleka kuwalanga monga mʼmene anakonzera? Ifetu tikudziyitanira tsoka lalikulu!”

20 (Panalinso munthu wina, Uriya mwana wa Semaya wa ku Kiriati-Yeyarimu, amene ankalosera mʼdzina la Yehova. Iyeyu analosera za mzinda uno ndi dziko lino monga mmene wachitira Yeremiya. 21 Mfumu Yehoyakimu, ankhondo ake onse ndi nduna zake anamva mawu akewo, ndipo anafuna kumupha. Koma Uriya atamva zimenezi, anachita mantha nathawira ku Igupto. 22 Komabe Mfumu Yehoyakimu anatuma Elinatani mwana wa Akibori pamodzi ndi anthu ena, ku Igupto. 23 Iwo anakamutenga Uriya ku Igupto kuja nabwera naye kwa Mfumu Yehoyakimu. Iye anamupha ndi lupanga ndipo mtembo wake anakawutaya ku manda a anthu wamba).

24 Koma Ahikamu mwana wa Safani ndiye anateteza Yeremiya, motero sanamupereke kwa anthu kuti amuphe.

Jeremiah Threatened With Death

26 Early in the reign of Jehoiakim(A) son of Josiah king of Judah, this word came from the Lord: “This is what the Lord says: Stand in the courtyard(B) of the Lord’s house and speak to all the people of the towns of Judah who come to worship in the house of the Lord.(C) Tell(D) them everything I command you; do not omit(E) a word. Perhaps they will listen and each will turn(F) from their evil ways. Then I will relent(G) and not inflict on them the disaster I was planning because of the evil they have done. Say to them, ‘This is what the Lord says: If you do not listen(H) to me and follow my law,(I) which I have set before you, and if you do not listen to the words of my servants the prophets, whom I have sent to you again and again (though you have not listened(J)), then I will make this house like Shiloh(K) and this city a curse[a](L) among all the nations of the earth.’”

The priests, the prophets and all the people heard Jeremiah speak these words in the house of the Lord. But as soon as Jeremiah finished telling all the people everything the Lord had commanded(M) him to say, the priests, the prophets and all the people seized(N) him and said, “You must die!(O) Why do you prophesy in the Lord’s name that this house will be like Shiloh and this city will be desolate and deserted?”(P) And all the people crowded(Q) around Jeremiah in the house of the Lord.

10 When the officials(R) of Judah heard about these things, they went up from the royal palace to the house of the Lord and took their places at the entrance of the New Gate(S) of the Lord’s house. 11 Then the priests and the prophets said to the officials and all the people, “This man should be sentenced to death(T) because he has prophesied against this city. You have heard it with your own ears!”(U)

12 Then Jeremiah said to all the officials(V) and all the people: “The Lord sent me to prophesy(W) against this house and this city all the things you have heard.(X) 13 Now reform(Y) your ways and your actions and obey(Z) the Lord your God. Then the Lord will relent(AA) and not bring the disaster he has pronounced against you. 14 As for me, I am in your hands;(AB) do with me whatever you think is good and right. 15 Be assured, however, that if you put me to death, you will bring the guilt of innocent blood(AC) on yourselves and on this city and on those who live in it, for in truth the Lord has sent me to you to speak all these words(AD) in your hearing.”

16 Then the officials(AE) and all the people said to the priests and the prophets, “This man should not be sentenced to death!(AF) He has spoken to us in the name of the Lord our God.”

17 Some of the elders of the land stepped forward and said to the entire assembly of people, 18 “Micah(AG) of Moresheth prophesied in the days of Hezekiah king of Judah. He told all the people of Judah, ‘This is what the Lord Almighty says:

“‘Zion(AH) will be plowed like a field,
    Jerusalem will become a heap of rubble,(AI)
    the temple hill(AJ) a mound overgrown with thickets.’[b](AK)

19 “Did Hezekiah king of Judah or anyone else in Judah put him to death? Did not Hezekiah(AL) fear the Lord and seek(AM) his favor? And did not the Lord relent,(AN) so that he did not bring the disaster(AO) he pronounced against them? We are about to bring a terrible disaster(AP) on ourselves!”

20 (Now Uriah son of Shemaiah from Kiriath Jearim(AQ) was another man who prophesied in the name of the Lord; he prophesied the same things against this city and this land as Jeremiah did. 21 When King Jehoiakim(AR) and all his officers and officials(AS) heard his words, the king was determined to put him to death.(AT) But Uriah heard of it and fled(AU) in fear to Egypt. 22 King Jehoiakim, however, sent Elnathan(AV) son of Akbor to Egypt, along with some other men. 23 They brought Uriah out of Egypt and took him to King Jehoiakim, who had him struck down with a sword(AW) and his body thrown into the burial place of the common people.)(AX)

24 Furthermore, Ahikam(AY) son of Shaphan supported Jeremiah, and so he was not handed over to the people to be put to death.

Footnotes

  1. Jeremiah 26:6 That is, its name will be used in cursing (see 29:22); or, others will see that it is cursed.
  2. Jeremiah 26:18 Micah 3:12