Add parallel Print Page Options

Zaka 70 za Ukapolo

25 Yehova anayankhula ndi Yeremiya za anthu onse a ku Yuda mʼchaka chachinayi cha ufumu wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya ku Yuda, chimene chinali chaka choyamba cha ufumu wa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni. Choncho mneneri Yeremiya anawuza anthu onse a ku Yuda pamodzi ndi onse amene amakhala mu Yerusalemu kuti: Kwa zaka 23, kuyambira chaka cha 13 cha ufumu wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya ku Yuda mpaka lero lino, Yehova wakhala akundipatsa mauthenga ake ndipo ine ndakhala ndikuyankhula ndi inu kawirikawiri, koma inu simunamvere.

Ndipo ngakhale Yehova kawirikawiri wakhala akukutumizirani atumiki ake onse, aneneri, inuyo simunamvere kapena kutchera khutu. Aneneriwo ankanena kuti, “Ngati aliyense wa inu abwerere, kusiya njira zake zoyipa ndi machitidwe ake oyipa, ndiye kuti mudzakhala mʼdziko limene Yehova anapereka kwa makolo anu kwamuyaya. Musatsatire milungu ina nʼkuyitumikira ndi kuyipembedza. Musapute mkwiyo wanga ndi mafano amene mwapanga ndi manja anu. Mukatero Ine sindidzakuwonongani.

“Koma inu simunandimvere,” akutero Yehova, “ndipo munaputa mkwiyo wanga ndi mafano amene munapanga ndi manja anu. Choncho munadziwononga nokha.”

Nʼchifukwa chake Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Chifukwa simunamvere mawu anga, ndidzayitana mafuko onse akumpoto, pamodzi ndi mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni,” akutero Yehova, “ndipo adzathira nkhondo dziko lino ndi anthu ake pamodzi ndi mitundu yonse ya anthu ozungulira dzikoli. Ndidzawawononga kwathunthu ndi kuwasandutsa chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka, mpaka muyaya. 10 Ndidzathetsa mfuwu wachimwemwe ndi wachisangalalo, mawu a mkwati ndi mkwatibwi, phokoso la mphero ndi kuwala kwa nyale. 11 Dziko lonse lidzakhala bwinja ndi chipululu, ndipo mitundu ina idzatumikira mfumu ya ku Babuloni kwa 70.

12 “Koma zaka 70 zikadzatha, ndidzalanga mfumu ya ku Babuloni pamodzi ndi anthu ake, chifukwa cha zolakwa zawo,” akutero Yehova, “ndipo dziko lawo lidzakhala chipululu mpaka muyaya. 13 Ndidzachita zinthu zonse zimene ndinayankhula zotsutsa dzikolo, zonse zimene zalembedwa mʼbuku lino, ndiponso zonse zimene Yeremiya analosera zotsutsa anthu amenewa. 14 Iwo eni adzakhala akapolo a anthu a mitundu yochuluka ndi mafumu amphamvu. Ndidzawabwezera molingana ndi zochita zawo ndi ntchito za manja awo.”

Chikho cha Ukali wa Mulungu

15 Yehova, Mulungu wa Israeli, anandiwuza kuti, “Tenga chikho ichi chodzaza ndi vinyo wa ukali wanga, ndipo ukamwetse anthu a mitundu yonse kumene ndikukutuma. 16 Akadzamwa adzayamba kudzandira ndi kuchita misala chifukwa cha nkhondo imene ndikuyitumiza pakati pawo.”

17 Choncho ine ndinatenga chikhocho mʼdzanja la Yehova ndipo ndinamwetsa mitundu yonse ya anthu kumene Iye ananditumako: 18 Anandituma ku Yerusalemu ndi ku mizinda ya Yuda, kwa mafumu ake ndi nduna zake kuti ndikawasandutse ngati bwinja ndi chinthu chochititsa mantha ndi chonyozeka ndiponso chotembereredwa, monga mmene alili lero lino. 19 Ananditumanso kwa Farao, mfumu ya ku Igupto, kwa atumiki ake, nduna zake ndi kwa anthu ake onse, 20 ndi kwa anthu ena onse a mitundu yachilendo; mafumu onse a ku Uzi; mafumu onse a Afilisti, a ku Asikeloni, ku Gaza, ku Ekroni ndiponso kwa anthu a ku chigwa chotsala cha Asidodi; 21 Edomu, Mowabu ndi Amoni. 22 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Turo ndi ku Sidoni; kwa mafumu a kutsidya la nyanja; 23 ku Dedani, ku Tema, ku Buzi ndi kwa onse ometa chamʼmbali. 24 Ananditumanso kwa mafumu onse a ku Arabiya ndi mafumu onse a anthu achilendo amene amakhala mʼchipululu. 25 Anandituma kwa mafumu onse a ku Zimuri, Elamu ndi Mediya; 26 ndiponso kwa mafumu onse a kumpoto, akufupi ndi kutali omwe, mafumu onse a dziko lapansi. Ndipo potsiriza pake, idzamwenso ndi mfumu Sesaki.

27 “Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Imwani, ledzerani ndipo musanze, mugwe osadzukanso chifukwa cha nkhondo imene ndikutumiza pakati panu.’ 28 Koma ngati akana kutenga chikhocho mʼdzanja lako ndi kumwa, uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse akuti: Muyenera kumwa ndithu!’ ” 29 Taonani, tsopano ndiyamba kulanga mzinda uno umene umadziwika ndi dzina langa. Kodi inu muganiza kuti simudzalangidwa? Ayi, simudzapulumuka chifukwa ndikutumiza nkhondo pa onse okhala pa dziko lapansi, akutero Yehova Wamphamvuzonse.

30 “Tsopano iwe nenera mawu owatsutsa ndipo uwawuze kuti,

“ ‘Yehova adzabangula kumwamba;
    mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera ku malo ake opatulika.
    Adzabangula mwamphamvu kukalipira dziko lake.
Iye adzafuwula ngati anthu oponda mphesa,
    kukalipira onse amene akukhala pa dziko lapansi.
31 Phokoso lalikulu lidzamveka mpaka kumalekezero a dziko lonse lapansi,
    chifukwa Yehova adzazenga mlandu anthu a mitundu yonse;
adzaweruza mtundu wonse wa anthu
    ndipo oyipa adzawapha ndi lupanga,’ ”
            akutero Yehova.

32 Yehova Wamphamvuzonse akuti,

“Taonani! Mavuto akuti akachoka
    pa mtundu wina akukagwa pa mtundu wina;
mphepo ya mkuntho ikuyambira
    ku malekezero a dziko.”

33 Pa tsiku limenelo, onse ophedwa ndi Yehova adzangoti mbwee ponseponse, pa dziko lonse lapansi. Palibe amene adzawalire kapena kusonkhanitsa mitemboyo kuti ikayikidwe mʼmanda, koma idzakhala mbwee ngati ndowe.

34 Khetsani misozi ndi kufuwula mwamphamvu, abusa inu;
    gubudukani pa fumbi, inu atsogoleri a nkhosa.
Pakuti nthawi yanu yophedwa yafika;
    mudzagwa ndi kuphwanyika ngati mbiya yabwino kwambiri.
35 Abusa adzasowa kothawira,
    atsogoleri a nkhosa adzasowa malo opulumukira.
36 Imvani kulira kwa abusa,
    atsogoleri a nkhosa akulira,
    chifukwa Yehova akuwononga msipu wawo.
37 Makola awo a nkhosa amene anali pamtendere adzasanduka bwinja
    chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.
38 Ngati mkango, Yehova wasiya phanga lake,
    pakuti dziko lawo lasanduka chipululu
chifukwa cha nkhondo ya owazunza
    ndiponso chifukwa cha mkwiyo woopsa wa Yehova.

Seventy Years of Captivity

25 The word came to Jeremiah concerning all the people of Judah in the fourth year of Jehoiakim(A) son of Josiah king of Judah, which was the first year of Nebuchadnezzar(B) king of Babylon. So Jeremiah the prophet said to all the people of Judah(C) and to all those living in Jerusalem: For twenty-three years—from the thirteenth year of Josiah(D) son of Amon king of Judah until this very day—the word of the Lord has come to me and I have spoken to you again and again,(E) but you have not listened.(F)

And though the Lord has sent all his servants the prophets(G) to you again and again, you have not listened or paid any attention.(H) They said, “Turn(I) now, each of you, from your evil ways and your evil practices, and you can stay in the land(J) the Lord gave to you and your ancestors for ever and ever. Do not follow other gods(K) to serve and worship them; do not arouse my anger with what your hands have made. Then I will not harm you.”

“But you did not listen to me,” declares the Lord, “and you have aroused(L) my anger with what your hands have made,(M) and you have brought harm(N) to yourselves.”

Therefore the Lord Almighty says this: “Because you have not listened to my words, I will summon(O) all the peoples of the north(P) and my servant(Q) Nebuchadnezzar(R) king of Babylon,” declares the Lord, “and I will bring them against this land and its inhabitants and against all the surrounding nations. I will completely destroy[a](S) them and make them an object of horror and scorn,(T) and an everlasting ruin.(U) 10 I will banish from them the sounds(V) of joy and gladness, the voices of bride and bridegroom,(W) the sound of millstones(X) and the light of the lamp.(Y) 11 This whole country will become a desolate wasteland,(Z) and these nations will serve(AA) the king of Babylon seventy years.(AB)

12 “But when the seventy years(AC) are fulfilled, I will punish the king of Babylon(AD) and his nation, the land of the Babylonians,[b] for their guilt,” declares the Lord, “and will make it desolate(AE) forever. 13 I will bring on that land all the things I have spoken against it, all that are written(AF) in this book and prophesied by Jeremiah against all the nations. 14 They themselves will be enslaved(AG) by many nations(AH) and great kings; I will repay(AI) them according to their deeds and the work of their hands.”

The Cup of God’s Wrath

15 This is what the Lord, the God of Israel, said to me: “Take from my hand this cup(AJ) filled with the wine of my wrath and make all the nations to whom I send(AK) you drink it. 16 When they drink(AL) it, they will stagger(AM) and go mad(AN) because of the sword(AO) I will send among them.”

17 So I took the cup from the Lord’s hand and made all the nations to whom he sent(AP) me drink it: 18 Jerusalem(AQ) and the towns of Judah, its kings and officials, to make them a ruin(AR) and an object of horror and scorn,(AS) a curse[c](AT)—as they are today;(AU) 19 Pharaoh king(AV) of Egypt,(AW) his attendants, his officials and all his people, 20 and all the foreign people there; all the kings of Uz;(AX) all the kings of the Philistines(AY) (those of Ashkelon,(AZ) Gaza,(BA) Ekron, and the people left at Ashdod); 21 Edom,(BB) Moab(BC) and Ammon;(BD) 22 all the kings of Tyre(BE) and Sidon;(BF) the kings of the coastlands(BG) across the sea; 23 Dedan,(BH) Tema,(BI) Buz(BJ) and all who are in distant places[d];(BK) 24 all the kings of Arabia(BL) and all the kings of the foreign people(BM) who live in the wilderness; 25 all the kings of Zimri,(BN) Elam(BO) and Media;(BP) 26 and all the kings of the north,(BQ) near and far, one after the other—all the kingdoms(BR) on the face of the earth. And after all of them, the king of Sheshak[e](BS) will drink it too.

27 “Then tell them, ‘This is what the Lord Almighty, the God of Israel, says: Drink, get drunk(BT) and vomit, and fall to rise no more because of the sword(BU) I will send among you.’ 28 But if they refuse to take the cup from your hand and drink(BV), tell them, ‘This is what the Lord Almighty says: You must drink it! 29 See, I am beginning to bring disaster(BW) on the city that bears my Name,(BX) and will you indeed go unpunished?(BY) You will not go unpunished, for I am calling down a sword(BZ) on all(CA) who live on the earth,(CB) declares the Lord Almighty.’

30 “Now prophesy all these words against them and say to them:

“‘The Lord will roar(CC) from on high;
    he will thunder(CD) from his holy dwelling(CE)
    and roar mightily against his land.
He will shout like those who tread(CF) the grapes,
    shout against all who live on the earth.
31 The tumult(CG) will resound to the ends of the earth,
    for the Lord will bring charges(CH) against the nations;
he will bring judgment(CI) on all(CJ) mankind
    and put the wicked to the sword,(CK)’”
declares the Lord.

32 This is what the Lord Almighty says:

“Look! Disaster(CL) is spreading
    from nation to nation;(CM)
a mighty storm(CN) is rising
    from the ends of the earth.”(CO)

33 At that time those slain(CP) by the Lord will be everywhere—from one end of the earth to the other. They will not be mourned or gathered(CQ) up or buried,(CR) but will be like dung lying on the ground.

34 Weep and wail, you shepherds;(CS)
    roll(CT) in the dust, you leaders of the flock.
For your time to be slaughtered(CU) has come;
    you will fall like the best of the rams.[f](CV)
35 The shepherds will have nowhere to flee,
    the leaders of the flock no place to escape.(CW)
36 Hear the cry(CX) of the shepherds,(CY)
    the wailing of the leaders of the flock,
    for the Lord is destroying their pasture.
37 The peaceful meadows will be laid waste
    because of the fierce anger of the Lord.
38 Like a lion(CZ) he will leave his lair,
    and their land will become desolate(DA)
because of the sword[g] of the oppressor(DB)
    and because of the Lord’s fierce anger.(DC)

Footnotes

  1. Jeremiah 25:9 The Hebrew term refers to the irrevocable giving over of things or persons to the Lord, often by totally destroying them.
  2. Jeremiah 25:12 Or Chaldeans
  3. Jeremiah 25:18 That is, their names to be used in cursing (see 29:22); or, to be seen by others as cursed
  4. Jeremiah 25:23 Or who clip the hair by their foreheads
  5. Jeremiah 25:26 Sheshak is a cryptogram for Babylon.
  6. Jeremiah 25:34 Septuagint; Hebrew fall and be shattered like fine pottery
  7. Jeremiah 25:38 Some Hebrew manuscripts and Septuagint (see also 46:16 and 50:16); most Hebrew manuscripts anger