Add parallel Print Page Options

Yeremiya ndi Pasuri

20 Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi. Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova. Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse. Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo. Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni. Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’ ”

Madandawulo a Yeremiya

Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi;
    Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana.
Anthu akundinyoza tsiku lonse.
    Aliyense akundiseka kosalekeza.
Nthawi iliyonse ndikamayankhula,
    ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka!
Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka
    ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye
    kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,”
mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga,
    amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga.
Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa,
    koma sindingathe kupirirabe.
10 Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti,
    “Zoopsa ku mbali zonse!
    Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!”
Onse amene anali abwenzi anga
    akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti,
“Mwina mwake adzanyengedwa;
    tidzamugwira
    ndi kulipsira pa iye.”

11 Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu.
    Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana.
Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana.
    Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama
    ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu.
Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga
    popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.

13 Imbirani Yehova!
    Mutamandeni Yehova!
Iye amapulumutsa wosauka
    mʼmanja mwa anthu oyipa.

14 Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa!
    Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga
    ndi uthenga woti:
    “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene
    Yehova anayiwononga mopanda chisoni.
Amve mfuwu mmawa,
    phokoso la nkhondo masana.
17 Chifukwa sanandiphere mʼmimba,
    kuti amayi anga asanduke manda anga,
    mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni
    kuti moyo wanga
    ukhale wamanyazi wokhawokha?

Jeremiah and Pashhur

20 When the priest Pashhur son of Immer,(A) the official(B) in charge of the temple of the Lord, heard Jeremiah prophesying these things, he had Jeremiah the prophet beaten(C) and put in the stocks(D) at the Upper Gate of Benjamin(E) at the Lord’s temple. The next day, when Pashhur released him from the stocks, Jeremiah said to him, “The Lord’s name(F) for you is not Pashhur, but Terror on Every Side.(G) For this is what the Lord says: ‘I will make you a terror to yourself and to all your friends; with your own eyes(H) you will see them fall by the sword of their enemies. I will give(I) all Judah into the hands of the king of Babylon, who will carry(J) them away to Babylon or put them to the sword. I will deliver all the wealth(K) of this city into the hands of their enemies—all its products, all its valuables and all the treasures of the kings of Judah. They will take it away(L) as plunder and carry it off to Babylon. And you, Pashhur, and all who live in your house will go into exile to Babylon. There you will die and be buried, you and all your friends to whom you have prophesied(M) lies.’”

Jeremiah’s Complaint

You deceived[a](N) me, Lord, and I was deceived[b];
    you overpowered(O) me and prevailed.
I am ridiculed(P) all day long;
    everyone mocks(Q) me.
Whenever I speak, I cry out
    proclaiming violence and destruction.(R)
So the word of the Lord has brought me
    insult and reproach(S) all day long.
But if I say, “I will not mention his word
    or speak anymore in his name,”(T)
his word is in my heart like a fire,(U)
    a fire shut up in my bones.
I am weary of holding it in;(V)
    indeed, I cannot.
10 I hear many whispering,
    “Terror(W) on every side!
    Denounce(X) him! Let’s denounce him!”
All my friends(Y)
    are waiting for me to slip,(Z) saying,
“Perhaps he will be deceived;
    then we will prevail(AA) over him
    and take our revenge(AB) on him.”

11 But the Lord(AC) is with me like a mighty warrior;
    so my persecutors(AD) will stumble and not prevail.(AE)
They will fail and be thoroughly disgraced;(AF)
    their dishonor will never be forgotten.
12 Lord Almighty, you who examine the righteous
    and probe the heart and mind,(AG)
let me see your vengeance(AH) on them,
    for to you I have committed(AI) my cause.

13 Sing(AJ) to the Lord!
    Give praise to the Lord!
He rescues(AK) the life of the needy
    from the hands of the wicked.(AL)

14 Cursed be the day I was born!(AM)
    May the day my mother bore me not be blessed!
15 Cursed be the man who brought my father the news,
    who made him very glad, saying,
    “A child is born to you—a son!”
16 May that man be like the towns(AN)
    the Lord overthrew without pity.
May he hear wailing(AO) in the morning,
    a battle cry at noon.
17 For he did not kill me in the womb,(AP)
    with my mother as my grave,
    her womb enlarged forever.
18 Why did I ever come out of the womb(AQ)
    to see trouble(AR) and sorrow
    and to end my days in shame?(AS)

Footnotes

  1. Jeremiah 20:7 Or persuaded
  2. Jeremiah 20:7 Or persuaded